Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova.

36 Uthenga uli mu mtima mwanga
    wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa:
Mu mtima mwake
    mulibe kuopa Mulungu.
Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri,
    sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.
Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo;
    iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.
Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa;
    iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo
    ndipo sakana cholakwa chilichonse.

Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba,
    kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.
Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu,
    chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu.
Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.
    Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali!
Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu
    amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu;
    Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo;
    mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.

10 Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani,
    chilungamo chanu kwa olungama mtima.
11 Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane,
    kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.
12 Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa,
    aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!

Psalm 36[a]

For the director of music. Of David the servant of the Lord.

I have a message from God in my heart
    concerning the sinfulness of the wicked:[b](A)
There is no fear(B) of God
    before their eyes.(C)

In their own eyes they flatter themselves
    too much to detect or hate their sin.(D)
The words of their mouths(E) are wicked and deceitful;(F)
    they fail to act wisely(G) or do good.(H)
Even on their beds they plot evil;(I)
    they commit themselves to a sinful course(J)
    and do not reject what is wrong.(K)

Your love, Lord, reaches to the heavens,
    your faithfulness(L) to the skies.(M)
Your righteousness(N) is like the highest mountains,(O)
    your justice like the great deep.(P)
    You, Lord, preserve both people and animals.(Q)
How priceless is your unfailing love, O God!(R)
    People take refuge in the shadow of your wings.(S)
They feast on the abundance of your house;(T)
    you give them drink from your river(U) of delights.(V)
For with you is the fountain of life;(W)
    in your light(X) we see light.

10 Continue your love(Y) to those who know you,(Z)
    your righteousness to the upright in heart.(AA)
11 May the foot of the proud not come against me,
    nor the hand of the wicked(AB) drive me away.
12 See how the evildoers lie fallen—
    thrown down, not able to rise!(AC)

Footnotes

  1. Psalm 36:1 In Hebrew texts 36:1-12 is numbered 36:2-13.
  2. Psalm 36:1 Or A message from God: The transgression of the wicked / resides in their hearts.