Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

35 Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;
    mumenyane nawo amene akumenyana nane.
Tengani chishango ndi lihawo;
    dzukani ndipo bwerani mundithandize.
Tengani mkondo ndi nthungo,
    kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.
Uzani moyo wanga kuti,
    “Ine ndine chipulumutso chako.”

Iwo amene akufunafuna moyo wanga
    anyozedwe ndi kuchita manyazi;
iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke
    abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo
    pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera
    pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa
    ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa
    ukonde umene iwo abisa uwakole,
    agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova
    ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera,
    “Ndani angafanane nanu Yehova?
Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,
    osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira,
    zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino
    ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli
    ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.
Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14     ndinayendayenda ndi kulira maliro,
    kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.
Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima
    kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;
    ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.
    Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;
    anandikukutira mano awo.
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?
    Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,
    moyo wanga wopambana ku mikango.
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;
    pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19 Musalole adani anga onyenga
    akondwere chifukwa cha masautso anga;
musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa
    andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 Iwowo sayankhula mwamtendere,
    koma amaganizira zonamizira
    iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!
    Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.
    Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!
    Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.
    Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”
    Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga
    achite manyazi ndi kusokonezeka.
Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,
    avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,
    afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.
Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,
    Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu
    ndi za matamando anu tsiku lonse.

Psalm 35

Of David.

Contend,(A) Lord, with those who contend with me;
    fight(B) against those who fight against me.
Take up shield(C) and armor;
    arise(D) and come to my aid.(E)
Brandish spear(F) and javelin[a](G)
    against those who pursue me.
Say to me,
    “I am your salvation.(H)

May those who seek my life(I)
    be disgraced(J) and put to shame;(K)
may those who plot my ruin
    be turned back(L) in dismay.
May they be like chaff(M) before the wind,
    with the angel of the Lord(N) driving them away;
may their path be dark and slippery,
    with the angel of the Lord pursuing them.

Since they hid their net(O) for me without cause(P)
    and without cause dug a pit(Q) for me,
may ruin overtake them by surprise—(R)
    may the net they hid entangle them,
    may they fall into the pit,(S) to their ruin.
Then my soul will rejoice(T) in the Lord
    and delight in his salvation.(U)
10 My whole being will exclaim,
    “Who is like you,(V) Lord?
You rescue the poor from those too strong(W) for them,
    the poor and needy(X) from those who rob them.”

11 Ruthless witnesses(Y) come forward;
    they question me on things I know nothing about.
12 They repay me evil for good(Z)
    and leave me like one bereaved.
13 Yet when they were ill, I put on sackcloth(AA)
    and humbled myself with fasting.(AB)
When my prayers returned to me unanswered,
14     I went about mourning(AC)
    as though for my friend or brother.
I bowed my head in grief
    as though weeping for my mother.
15 But when I stumbled, they gathered in glee;(AD)
    assailants gathered against me without my knowledge.
    They slandered(AE) me without ceasing.
16 Like the ungodly they maliciously mocked;[b](AF)
    they gnashed their teeth(AG) at me.

17 How long,(AH) Lord, will you look on?
    Rescue me from their ravages,
    my precious life(AI) from these lions.(AJ)
18 I will give you thanks in the great assembly;(AK)
    among the throngs(AL) I will praise you.(AM)
19 Do not let those gloat over me
    who are my enemies(AN) without cause;
do not let those who hate me without reason(AO)
    maliciously wink the eye.(AP)
20 They do not speak peaceably,
    but devise false accusations(AQ)
    against those who live quietly in the land.
21 They sneer(AR) at me and say, “Aha! Aha!(AS)
    With our own eyes we have seen it.”

22 Lord, you have seen(AT) this; do not be silent.
    Do not be far(AU) from me, Lord.
23 Awake,(AV) and rise(AW) to my defense!
    Contend(AX) for me, my God and Lord.
24 Vindicate me in your righteousness, Lord my God;
    do not let them gloat(AY) over me.
25 Do not let them think, “Aha,(AZ) just what we wanted!”
    or say, “We have swallowed him up.”(BA)

26 May all who gloat(BB) over my distress(BC)
    be put to shame(BD) and confusion;
may all who exalt themselves over me(BE)
    be clothed with shame and disgrace.
27 May those who delight in my vindication(BF)
    shout for joy(BG) and gladness;
may they always say, “The Lord be exalted,
    who delights(BH) in the well-being of his servant.”(BI)

28 My tongue will proclaim your righteousness,(BJ)
    your praises all day long.(BK)

Footnotes

  1. Psalm 35:3 Or and block the way
  2. Psalm 35:16 Septuagint; Hebrew may mean Like an ungodly circle of mockers,