Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

24 Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo,
    dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja
    ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.

Ndani angakwere phiri la Yehova?
    Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera,
    amene sapereka moyo wake kwa fano
    kapena kulumbira mwachinyengo.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova
    ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova;
    amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo.
            Sela

Tukulani mitu yanu inu zipata;
    tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
    kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
    Yehova Wamphamvuzonse,
    Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Tukulani mitu yanu, inu zipata;
    tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
    kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
    Yehova Wamphamvuzonse,
    Iye ndiye Mfumu yaulemerero.
            Sela

Psalm 24

Of David. A psalm.

The earth is the Lord’s,(A) and everything in it,
    the world, and all who live in it;(B)
for he founded it on the seas
    and established it on the waters.(C)

Who may ascend the mountain(D) of the Lord?
    Who may stand in his holy place?(E)
The one who has clean hands(F) and a pure heart,(G)
    who does not trust in an idol(H)
    or swear by a false god.[a]

They will receive blessing(I) from the Lord
    and vindication(J) from God their Savior.
Such is the generation of those who seek him,
    who seek your face,(K) God of Jacob.[b][c]

Lift up your heads, you gates;(L)
    be lifted up, you ancient doors,
    that the King(M) of glory(N) may come in.(O)
Who is this King of glory?
    The Lord strong and mighty,(P)
    the Lord mighty in battle.(Q)
Lift up your heads, you gates;
    lift them up, you ancient doors,
    that the King of glory may come in.
10 Who is he, this King of glory?
    The Lord Almighty(R)
    he is the King of glory.

Footnotes

  1. Psalm 24:4 Or swear falsely
  2. Psalm 24:6 Two Hebrew manuscripts and Syriac (see also Septuagint); most Hebrew manuscripts face, Jacob
  3. Psalm 24:6 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 10.