Masalimo 21
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
21 Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu,
chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!
2 Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake
ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake.
Sela
3 Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka
ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.
4 Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa
masiku ochuluka kwamuyaya.
5 Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu;
Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.
6 Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya,
Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.
7 Pakuti mfumu imadalira Yehova;
kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba,
iyo sidzagwedezeka.
8 Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse;
dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.
9 Pa nthawi ya kuonekera kwanu
mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha.
Mu ukali wake Yehova adzawameza,
ndipo moto wake udzawatha.
10 Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi,
zidzukulu zawo pakati pa anthu.
11 Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo
sadzapambana;
12 pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo
pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.
13 Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu,
ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.
Psalm 21
New International Version
Psalm 21[a]
For the director of music. A psalm of David.
2 You have granted him his heart’s desire(C)
and have not withheld the request of his lips.[b]
3 You came to greet him with rich blessings
and placed a crown of pure gold(D) on his head.(E)
4 He asked you for life, and you gave it to him—
length of days, for ever and ever.(F)
5 Through the victories(G) you gave, his glory is great;
you have bestowed on him splendor and majesty.(H)
6 Surely you have granted him unending blessings
and made him glad with the joy(I) of your presence.(J)
7 For the king trusts in the Lord;(K)
through the unfailing love(L) of the Most High(M)
he will not be shaken.(N)
8 Your hand will lay hold(O) on all your enemies;
your right hand will seize your foes.
9 When you appear for battle,
you will burn them up as in a blazing furnace.
The Lord will swallow them up in his wrath,
and his fire will consume them.(P)
10 You will destroy their descendants from the earth,
their posterity from mankind.(Q)
11 Though they plot evil(R) against you
and devise wicked schemes,(S) they cannot succeed.
12 You will make them turn their backs(T)
when you aim at them with drawn bow.
Footnotes
- Psalm 21:1 In Hebrew texts 21:1-13 is numbered 21:2-14.
- Psalm 21:2 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.