Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

21 Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu,
    chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!
Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake
    ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake.
            Sela
Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka
    ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.
Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa
    masiku ochuluka kwamuyaya.
Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu;
    Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.
Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya,
    Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.
Pakuti mfumu imadalira Yehova;
    kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba,
    iyo sidzagwedezeka.

Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse;
    dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.
Pa nthawi ya kuonekera kwanu
    mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha.
Mu ukali wake Yehova adzawameza,
    ndipo moto wake udzawatha.
10 Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi,
    zidzukulu zawo pakati pa anthu.
11 Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo
    sadzapambana;
12 pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo
    pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.

13 Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu,
    ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.

Psalm 21[a]

For the director of music. A psalm of David.

The king rejoices in your strength, Lord.(A)
    How great is his joy in the victories you give!(B)

You have granted him his heart’s desire(C)
    and have not withheld the request of his lips.[b]
You came to greet him with rich blessings
    and placed a crown of pure gold(D) on his head.(E)
He asked you for life, and you gave it to him—
    length of days, for ever and ever.(F)
Through the victories(G) you gave, his glory is great;
    you have bestowed on him splendor and majesty.(H)
Surely you have granted him unending blessings
    and made him glad with the joy(I) of your presence.(J)
For the king trusts in the Lord;(K)
    through the unfailing love(L) of the Most High(M)
    he will not be shaken.(N)

Your hand will lay hold(O) on all your enemies;
    your right hand will seize your foes.
When you appear for battle,
    you will burn them up as in a blazing furnace.
The Lord will swallow them up in his wrath,
    and his fire will consume them.(P)
10 You will destroy their descendants from the earth,
    their posterity from mankind.(Q)
11 Though they plot evil(R) against you
    and devise wicked schemes,(S) they cannot succeed.
12 You will make them turn their backs(T)
    when you aim at them with drawn bow.

13 Be exalted(U) in your strength, Lord;(V)
    we will sing and praise your might.

Footnotes

  1. Psalm 21:1 In Hebrew texts 21:1-13 is numbered 21:2-14.
  2. Psalm 21:2 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.