Masalimo 148
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
148 Tamandani Yehova.
Tamandani Yehova, inu a kumwamba,
mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.
2 Mutamandeni, inu angelo ake onse,
mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.
3 Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi,
mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.
4 Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba
ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.
5 Zonse zitamande dzina la Yehova
pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.
6 Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi;
analamula ndipo sizidzatha.
7 Tamandani Yehova pa dziko lapansi,
inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,
8 inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,
mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,
9 inu mapiri ndi zitunda zonse,
inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,
10 inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,
inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.
11 Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,
inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.
12 Inu anyamata ndi anamwali,
inu nkhalamba ndi ana omwe.
13 Onsewo atamande dzina la Yehova
pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;
ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.
14 Iye wakwezera nyanga anthu ake,
matamando a anthu ake onse oyera mtima,
Aisraeli, anthu a pamtima pake.
Tamandani Yehova.
Psalm 148
New International Version
Psalm 148
Praise the Lord from the heavens;(B)
praise him in the heights above.
2 Praise him, all his angels;(C)
praise him, all his heavenly hosts.(D)
3 Praise him, sun(E) and moon;
praise him, all you shining stars.
4 Praise him, you highest heavens(F)
and you waters above the skies.(G)
5 Let them praise the name(H) of the Lord,
for at his command(I) they were created,
6 and he established them for ever and ever—
he issued a decree(J) that will never pass away.
7 Praise the Lord(K) from the earth,
you great sea creatures(L) and all ocean depths,(M)
8 lightning and hail,(N) snow and clouds,
stormy winds that do his bidding,(O)
9 you mountains and all hills,(P)
fruit trees and all cedars,
10 wild animals(Q) and all cattle,
small creatures and flying birds,
11 kings(R) of the earth and all nations,
you princes and all rulers on earth,
12 young men and women,
old men and children.
13 Let them praise the name of the Lord,(S)
for his name alone is exalted;
his splendor(T) is above the earth and the heavens.(U)
14 And he has raised up for his people a horn,[b](V)
the praise(W) of all his faithful servants,(X)
of Israel, the people close to his heart.(Y)
Praise the Lord.
Footnotes
- Psalm 148:1 Hebrew Hallelu Yah; also in verse 14
- Psalm 148:14 Horn here symbolizes strength.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.