Add parallel Print Page Options

Salimo la matamando la Davide.

145 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
    ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
    ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
    ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
    Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
    ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
    ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
    ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
    wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Yehova ndi wabwino kwa onse;
    amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
    oyera mtima adzakulemekezani.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
    ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
    ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
    ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse
    ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
    ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
    ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Mumatsekula dzanja lanu
    ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
    ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
    onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
    amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
    koma adzawononga anthu onse oyipa.

21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.
    Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera
    ku nthawi za nthawi.

Psalm 145[a]

A psalm of praise. Of David.

I will exalt you,(A) my God the King;(B)
    I will praise your name(C) for ever and ever.
Every day I will praise(D) you
    and extol your name(E) for ever and ever.

Great(F) is the Lord and most worthy of praise;(G)
    his greatness no one can fathom.(H)
One generation(I) commends your works to another;
    they tell(J) of your mighty acts.(K)
They speak of the glorious splendor(L) of your majesty—
    and I will meditate on your wonderful works.[b](M)
They tell(N) of the power of your awesome works—(O)
    and I will proclaim(P) your great deeds.(Q)
They celebrate your abundant goodness(R)
    and joyfully sing(S) of your righteousness.(T)

The Lord is gracious and compassionate,(U)
    slow to anger and rich in love.(V)

The Lord is good(W) to all;
    he has compassion(X) on all he has made.
10 All your works praise you,(Y) Lord;
    your faithful people extol(Z) you.(AA)
11 They tell of the glory of your kingdom(AB)
    and speak of your might,(AC)
12 so that all people may know of your mighty acts(AD)
    and the glorious splendor of your kingdom.(AE)
13 Your kingdom is an everlasting kingdom,(AF)
    and your dominion endures through all generations.

The Lord is trustworthy(AG) in all he promises(AH)
    and faithful in all he does.[c]
14 The Lord upholds(AI) all who fall
    and lifts up all(AJ) who are bowed down.(AK)
15 The eyes of all look to you,
    and you give them their food(AL) at the proper time.
16 You open your hand
    and satisfy the desires(AM) of every living thing.

17 The Lord is righteous(AN) in all his ways
    and faithful in all he does.(AO)
18 The Lord is near(AP) to all who call on him,(AQ)
    to all who call on him in truth.
19 He fulfills the desires(AR) of those who fear him;(AS)
    he hears their cry(AT) and saves them.(AU)
20 The Lord watches over(AV) all who love him,(AW)
    but all the wicked he will destroy.(AX)

21 My mouth will speak(AY) in praise of the Lord.
    Let every creature(AZ) praise his holy name(BA)
    for ever and ever.

Footnotes

  1. Psalm 145:1 This psalm is an acrostic poem, the verses of which (including verse 13b) begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
  2. Psalm 145:5 Dead Sea Scrolls and Syriac (see also Septuagint); Masoretic Text On the glorious splendor of your majesty / and on your wonderful works I will meditate
  3. Psalm 145:13 One manuscript of the Masoretic Text, Dead Sea Scrolls and Syriac (see also Septuagint); most manuscripts of the Masoretic Text do not have the last two lines of verse 13.