Masalimo 14
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
14 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
“Kulibe Mulungu.”
Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;
palibe amene amachita zabwino.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi,
kuyangʼana anthu onse
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
amene amafunafuna Mulungu.
3 Onse atembenukira kumbali,
onse pamodzi asanduka oyipa;
palibe amene amachita zabwino,
palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?
Akudya anthu anga ngati chakudya chawo
ndipo satamanda Yehova?
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,
pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,
koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!
Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,
Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Psalm 14
New International Version
Psalm 14(A)
For the director of music. Of David.
1 The fool[a] says in his heart,
“There is no God.”(B)
They are corrupt, their deeds are vile;
there is no one who does good.
2 The Lord looks down from heaven(C)
on all mankind
to see if there are any who understand,(D)
any who seek God.(E)
3 All have turned away,(F) all have become corrupt;(G)
there is no one who does good,(H)
not even one.(I)
4 Do all these evildoers know nothing?(J)
Footnotes
- Psalm 14:1 The Hebrew words rendered fool in Psalms denote one who is morally deficient.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.