Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

14 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
    “Kulibe Mulungu.”
Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;
    palibe amene amachita zabwino.

Yehova kumwamba wayangʼana pansi,
    kuyangʼana anthu onse
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
    amene amafunafuna Mulungu.
Onse atembenukira kumbali,
    onse pamodzi asanduka oyipa;
palibe amene amachita zabwino,
    palibiretu ndi mmodzi yemwe.

Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?
    Akudya anthu anga ngati chakudya chawo
    ndipo satamanda Yehova?
Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,
    pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,
    koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.

Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!
    Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,
    Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!

Psalm 14(A)

For the director of music. Of David.

The fool[a] says in his heart,
    “There is no God.”(B)
They are corrupt, their deeds are vile;
    there is no one who does good.

The Lord looks down from heaven(C)
    on all mankind
to see if there are any who understand,(D)
    any who seek God.(E)
All have turned away,(F) all have become corrupt;(G)
    there is no one who does good,(H)
    not even one.(I)

Do all these evildoers know nothing?(J)

They devour my people(K) as though eating bread;
    they never call on the Lord.(L)
But there they are, overwhelmed with dread,
    for God is present in the company of the righteous.
You evildoers frustrate the plans of the poor,
    but the Lord is their refuge.(M)

Oh, that salvation for Israel would come out of Zion!(N)
    When the Lord restores(O) his people,
    let Jacob rejoice and Israel be glad!

Footnotes

  1. Psalm 14:1 The Hebrew words rendered fool in Psalms denote one who is morally deficient.