Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni.

127 Yehova akapanda kumanga nyumba,
    omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.
Yehova akapanda kulondera mzinda,
    mlonda akanangolondera pachabe.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa
    ndi kusagona msanga madzulo,
kuvutikira chakudya choti mudye,
    pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.

Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,
    ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja
    mwa munthu wankhondo.
Wodala munthu
    amene motengera mivi mwake mwadzaza.
Iwo sadzachititsidwa manyazi
    pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.