Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

126 Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,
    tinali ngati amene akulota.
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;
    malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.
Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,
    “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
Yehova watichitira zinthu zazikulu,
    ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,
    monga mitsinje ya ku Negevi.
Iwo amene amafesa akulira,
    adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
Iye amene amayendayenda nalira,
    atanyamula mbewu yokafesa,
adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,
    atanyamula mitolo yake.

Psalm 126

A song of ascents.

When the Lord restored(A) the fortunes of[a] Zion,
    we were like those who dreamed.[b]
Our mouths were filled with laughter,(B)
    our tongues with songs of joy.(C)
Then it was said among the nations,
    “The Lord has done great things(D) for them.”
The Lord has done great things(E) for us,
    and we are filled with joy.(F)

Restore our fortunes,[c](G) Lord,
    like streams in the Negev.(H)
Those who sow with tears(I)
    will reap(J) with songs of joy.(K)
Those who go out weeping,(L)
    carrying seed to sow,
will return with songs of joy,
    carrying sheaves with them.

Footnotes

  1. Psalm 126:1 Or Lord brought back the captives to
  2. Psalm 126:1 Or those restored to health
  3. Psalm 126:4 Or Bring back our captives