Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

122 Ndinakondwera atandiwuza kuti,
    “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
Mapazi athu akuyima mʼzipata
    zako, Iwe Yerusalemu.

Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda
    umene uli wothithikana pamodzi.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko,
    mafuko a Yehova,
umboni wa kwa Israeli,
    kuti atamande dzina la Yehova.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo,
    mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.

Pemphererani mtendere wa Yerusalemu:
    “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako,
    ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga
    ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu,
    ndidzakufunira zabwino.

Psalm 122

A song of ascents. Of David.

I rejoiced with those who said to me,
    “Let us go to the house of the Lord.”
Our feet are standing
    in your gates, Jerusalem.

Jerusalem is built like a city
    that is closely compacted together.
That is where the tribes go up—
    the tribes of the Lord
to praise the name of the Lord
    according to the statute given to Israel.
There stand the thrones for judgment,
    the thrones of the house of David.

Pray for the peace of Jerusalem:
    “May those who love(A) you be secure.
May there be peace(B) within your walls
    and security within your citadels.(C)
For the sake of my family and friends,
    I will say, “Peace be within you.”
For the sake of the house of the Lord our God,
    I will seek your prosperity.(D)