Add parallel Print Page Options

114 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto,
    nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu,
    Israeli anasanduka ufumu wake.

Nyanja inaona ndi kuthawa,
    mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna,
    timapiri ngati ana ankhosa.

Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa?
    iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna,
    inu timapiri, ngati ana ankhosa?

Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi,
    pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime,
    thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

Psalm 114

When Israel came out of Egypt,(A)
    Jacob from a people of foreign tongue,
Judah(B) became God’s sanctuary,(C)
    Israel his dominion.

The sea looked and fled,(D)
    the Jordan turned back;(E)
the mountains leaped(F) like rams,
    the hills like lambs.

Why was it, sea, that you fled?(G)
    Why, Jordan, did you turn back?
Why, mountains, did you leap like rams,
    you hills, like lambs?

Tremble, earth,(H) at the presence of the Lord,
    at the presence of the God of Jacob,
who turned the rock into a pool,
    the hard rock into springs of water.(I)