Add parallel Print Page Options

Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,
    umene kale unali wodzaza ndi anthu!
Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!
    Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.
Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,
    tsopano wasanduka kapolo.

Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,
    misozi ili pa masaya pake.
Mwa abwenzi ake onse,
    palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.
Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;
    onse akhala adani ake.

Yuda watengedwa ku ukapolo,
    kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.
Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;
    ndipo alibe malo opumulira.
Onse omuthamangitsa iye amupitirira,
    ndipo alibe kwina kothawira.

Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,
    chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.
Zipata zake zonse zili pululu,
    ansembe akubuwula.
Anamwali ake akulira,
    ndipo ali mʼmasautso woopsa.

Adani ake asanduka mabwana ake;
    odana naye akupeza bwino.
Yehova wamubweretsera mavuto
    chifukwa cha machimo ake ambiri.
Ana ake atengedwa ukapolo
    pamaso pa mdani.

Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni
    wachokeratu.
Akalonga ake ali ngati mbawala
    zosowa msipu;
alibe mphamvu zothawira
    owathamangitsa.

Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,
    Yerusalemu amakumbukira chuma chonse
    chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.
Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,
    panalibe aliyense womuthandiza.
Adani ake ankamuyangʼana
    ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.

Yerusalemu wachimwa kwambiri
    ndipo potero wakhala wodetsedwa.
Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,
    chifukwa aona umaliseche wake.
Iye mwini akubuwula
    ndipo akubisa nkhope yake.

Uve wake umaonekera pa zovala zake;
    iye sanaganizire za tsogolo lake.
Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;
    ndipo analibe womutonthoza.
“Inu Yehova, taonani masautso anga,
    pakuti mdani wapambana.”

10 Adani amulanda
    chuma chake chonse;
iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,
    amene Inu Mulungu munawaletsa
    kulowa mu msonkhano wanu.

11 Anthu ake onse akubuwula
    pamene akufunafuna chakudya;
asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya
    kuti akhale ndi moyo.
“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,
    chifukwa ine ndanyozeka.”

12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?
    Yangʼanani ndipo muone.
Kodi pali mavuto ofanana ndi
    amene andigwerawa,
amene Ambuye anandibweretsera
    pa tsiku la ukali wake?

13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba,
    unalowa mpaka mʼmafupa anga.
Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga
    ndipo anandibweza.
Anandisiya wopanda chilichonse,
    wolefuka tsiku lonse.

14 “Wazindikira machimo anga onse
    ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.
Machimowa afika pakhosi panga,
    ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.
Iye wandipereka
    kwa anthu amene sindingalimbane nawo.

15 “Ambuye wakana
    anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:
wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,
    kuti litekedze anyamata anga;
mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza
    anamwali a Yuda.

16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira
    ndipo maso anga adzaza ndi misozi.
Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,
    palibe aliyense wondilimbitsa mtima.
Ana anga ali okhaokha
    chifukwa mdani watigonjetsa.

17 “Ziyoni wakweza manja ake,
    koma palibe aliyense womutonthoza.
Yehova walamula kuti abale ake
    a Yakobo akhale adani ake;
Yerusalemu wasanduka
    chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18 “Yehova ndi wolungama,
    koma ndine ndinawukira malamulo ake.
Imvani inu anthu a mitundu yonse;
    onani masautso anga.
Anyamata ndi anamwali anga
    agwidwa ukapolo.

19 “Ndinayitana abwenzi anga
    koma anandinyenga.
Ansembe ndi akuluakulu anga
    anafa mu mzinda
pamene ankafunafuna chakudya
    kuti akhale ndi moyo.

20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
    Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
    chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
    ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21 “Anthu amva kubuwula kwanga,
    koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
    iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
    kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
    muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
    chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
    ndipo mtima wanga walefuka.”