Add parallel Print Page Options

Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira;
    yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Apereka cholowa chathu kwa obwera,
    nyumba zathu kwa alendo.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo,
    amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa,
    nkhuni zathunso nʼzogula.
Otilondola atigwira pakhosi;
    tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya
    kuti tipeze chakudya.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale,
    koma chilango chawo chili pa ife.
Akapolo akutilamulira,
    ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe
    chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo,
    chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni,
    ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo,
    akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu;
    anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda;
    achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu;
    kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu.
    Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi,
    chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja,
    nkhandwe zikungoyendayendapo.

19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya;
    mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse?
    Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere;
    mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu,
    ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

Remember, Lord, what has happened to us;
    look, and see our disgrace.(A)
Our inheritance(B) has been turned over to strangers,(C)
    our homes(D) to foreigners.(E)
We have become fatherless,
    our mothers are widows.(F)
We must buy the water we drink;(G)
    our wood can be had only at a price.(H)
Those who pursue us are at our heels;
    we are weary(I) and find no rest.(J)
We submitted to Egypt and Assyria(K)
    to get enough bread.
Our ancestors(L) sinned and are no more,
    and we bear their punishment.(M)
Slaves(N) rule over us,
    and there is no one to free us from their hands.(O)
We get our bread at the risk of our lives
    because of the sword in the desert.
10 Our skin is hot as an oven,
    feverish from hunger.(P)
11 Women have been violated(Q) in Zion,
    and virgins in the towns of Judah.
12 Princes have been hung up by their hands;
    elders(R) are shown no respect.(S)
13 Young men toil at the millstones;
    boys stagger under loads of wood.
14 The elders are gone from the city gate;
    the young men have stopped their music.(T)
15 Joy is gone from our hearts;
    our dancing has turned to mourning.(U)
16 The crown(V) has fallen from our head.(W)
    Woe to us, for we have sinned!(X)
17 Because of this our hearts(Y) are faint,(Z)
    because of these things our eyes(AA) grow dim(AB)
18 for Mount Zion,(AC) which lies desolate,(AD)
    with jackals prowling over it.

19 You, Lord, reign forever;(AE)
    your throne endures(AF) from generation to generation.
20 Why do you always forget us?(AG)
    Why do you forsake(AH) us so long?
21 Restore(AI) us to yourself, Lord, that we may return;
    renew our days as of old
22 unless you have utterly rejected us(AJ)
    and are angry with us beyond measure.(AK)