Add parallel Print Page Options

Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,
    umene kale unali wodzaza ndi anthu!
Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!
    Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.
Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,
    tsopano wasanduka kapolo.

Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,
    misozi ili pa masaya pake.
Mwa abwenzi ake onse,
    palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.
Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;
    onse akhala adani ake.

Yuda watengedwa ku ukapolo,
    kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.
Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;
    ndipo alibe malo opumulira.
Onse omuthamangitsa iye amupitirira,
    ndipo alibe kwina kothawira.

Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,
    chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.
Zipata zake zonse zili pululu,
    ansembe akubuwula.
Anamwali ake akulira,
    ndipo ali mʼmasautso woopsa.

Adani ake asanduka mabwana ake;
    odana naye akupeza bwino.
Yehova wamubweretsera mavuto
    chifukwa cha machimo ake ambiri.
Ana ake atengedwa ukapolo
    pamaso pa mdani.

Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni
    wachokeratu.
Akalonga ake ali ngati mbawala
    zosowa msipu;
alibe mphamvu zothawira
    owathamangitsa.

Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,
    Yerusalemu amakumbukira chuma chonse
    chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.
Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,
    panalibe aliyense womuthandiza.
Adani ake ankamuyangʼana
    ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.

Yerusalemu wachimwa kwambiri
    ndipo potero wakhala wodetsedwa.
Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,
    chifukwa aona umaliseche wake.
Iye mwini akubuwula
    ndipo akubisa nkhope yake.

Uve wake umaonekera pa zovala zake;
    iye sanaganizire za tsogolo lake.
Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;
    ndipo analibe womutonthoza.
“Inu Yehova, taonani masautso anga,
    pakuti mdani wapambana.”

10 Adani amulanda
    chuma chake chonse;
iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,
    amene Inu Mulungu munawaletsa
    kulowa mu msonkhano wanu.

11 Anthu ake onse akubuwula
    pamene akufunafuna chakudya;
asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya
    kuti akhale ndi moyo.
“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,
    chifukwa ine ndanyozeka.”

12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?
    Yangʼanani ndipo muone.
Kodi pali mavuto ofanana ndi
    amene andigwerawa,
amene Ambuye anandibweretsera
    pa tsiku la ukali wake?

13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba,
    unalowa mpaka mʼmafupa anga.
Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga
    ndipo anandibweza.
Anandisiya wopanda chilichonse,
    wolefuka tsiku lonse.

14 “Wazindikira machimo anga onse
    ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.
Machimowa afika pakhosi panga,
    ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.
Iye wandipereka
    kwa anthu amene sindingalimbane nawo.

15 “Ambuye wakana
    anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:
wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,
    kuti litekedze anyamata anga;
mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza
    anamwali a Yuda.

16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira
    ndipo maso anga adzaza ndi misozi.
Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,
    palibe aliyense wondilimbitsa mtima.
Ana anga ali okhaokha
    chifukwa mdani watigonjetsa.

17 “Ziyoni wakweza manja ake,
    koma palibe aliyense womutonthoza.
Yehova walamula kuti abale ake
    a Yakobo akhale adani ake;
Yerusalemu wasanduka
    chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18 “Yehova ndi wolungama,
    koma ndine ndinawukira malamulo ake.
Imvani inu anthu a mitundu yonse;
    onani masautso anga.
Anyamata ndi anamwali anga
    agwidwa ukapolo.

19 “Ndinayitana abwenzi anga
    koma anandinyenga.
Ansembe ndi akuluakulu anga
    anafa mu mzinda
pamene ankafunafuna chakudya
    kuti akhale ndi moyo.

20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
    Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
    chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
    ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21 “Anthu amva kubuwula kwanga,
    koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
    iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
    kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
    muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
    chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
    ndipo mtima wanga walefuka.”

[a]How deserted(A) lies the city,
    once so full of people!(B)
How like a widow(C) is she,
    who once was great(D) among the nations!
She who was queen among the provinces
    has now become a slave.(E)

Bitterly she weeps(F) at night,
    tears are on her cheeks.
Among all her lovers(G)
    there is no one to comfort her.
All her friends have betrayed(H) her;
    they have become her enemies.(I)

After affliction and harsh labor,
    Judah has gone into exile.(J)
She dwells among the nations;
    she finds no resting place.(K)
All who pursue her have overtaken her(L)
    in the midst of her distress.

The roads to Zion mourn,(M)
    for no one comes to her appointed festivals.
All her gateways are desolate,(N)
    her priests groan,
her young women grieve,
    and she is in bitter anguish.(O)

Her foes have become her masters;
    her enemies are at ease.
The Lord has brought her grief(P)
    because of her many sins.(Q)
Her children have gone into exile,(R)
    captive before the foe.(S)

All the splendor has departed
    from Daughter Zion.(T)
Her princes are like deer
    that find no pasture;
in weakness they have fled(U)
    before the pursuer.

In the days of her affliction and wandering
    Jerusalem remembers all the treasures
    that were hers in days of old.
When her people fell into enemy hands,
    there was no one to help her.(V)
Her enemies looked at her
    and laughed(W) at her destruction.

Jerusalem has sinned(X) greatly
    and so has become unclean.(Y)
All who honored her despise her,
    for they have all seen her naked;(Z)
she herself groans(AA)
    and turns away.

Her filthiness clung to her skirts;
    she did not consider her future.(AB)
Her fall(AC) was astounding;
    there was none to comfort(AD) her.
“Look, Lord, on my affliction,(AE)
    for the enemy has triumphed.”

10 The enemy laid hands
    on all her treasures;(AF)
she saw pagan nations
    enter her sanctuary(AG)
those you had forbidden(AH)
    to enter your assembly.

11 All her people groan(AI)
    as they search for bread;(AJ)
they barter their treasures for food
    to keep themselves alive.
“Look, Lord, and consider,
    for I am despised.”

12 “Is it nothing to you, all you who pass by?(AK)
    Look around and see.
Is any suffering like my suffering(AL)
    that was inflicted on me,
that the Lord brought on me
    in the day of his fierce anger?(AM)

13 “From on high he sent fire,
    sent it down into my bones.(AN)
He spread a net(AO) for my feet
    and turned me back.
He made me desolate,(AP)
    faint(AQ) all the day long.

14 “My sins have been bound into a yoke[b];(AR)
    by his hands they were woven together.
They have been hung on my neck,
    and the Lord has sapped my strength.
He has given me into the hands(AS)
    of those I cannot withstand.

15 “The Lord has rejected
    all the warriors in my midst;(AT)
he has summoned an army(AU) against me
    to[c] crush my young men.(AV)
In his winepress(AW) the Lord has trampled(AX)
    Virgin Daughter(AY) Judah.

16 “This is why I weep
    and my eyes overflow with tears.(AZ)
No one is near to comfort(BA) me,
    no one to restore my spirit.
My children are destitute
    because the enemy has prevailed.”(BB)

17 Zion stretches out her hands,(BC)
    but there is no one to comfort her.
The Lord has decreed for Jacob
    that his neighbors become his foes;(BD)
Jerusalem has become
    an unclean(BE) thing(BF) among them.

18 “The Lord is righteous,(BG)
    yet I rebelled(BH) against his command.
Listen, all you peoples;
    look on my suffering.(BI)
My young men and young women
    have gone into exile.(BJ)

19 “I called to my allies(BK)
    but they betrayed me.
My priests and my elders
    perished(BL) in the city
while they searched for food
    to keep themselves alive.

20 “See, Lord, how distressed(BM) I am!
    I am in torment(BN) within,
and in my heart I am disturbed,(BO)
    for I have been most rebellious.(BP)
Outside, the sword bereaves;
    inside, there is only death.(BQ)

21 “People have heard my groaning,(BR)
    but there is no one to comfort me.(BS)
All my enemies have heard of my distress;
    they rejoice(BT) at what you have done.
May you bring the day(BU) you have announced
    so they may become like me.

22 “Let all their wickedness come before you;
    deal with them
as you have dealt with me
    because of all my sins.(BV)
My groans(BW) are many
    and my heart is faint.”

Footnotes

  1. Lamentations 1:1 This chapter is an acrostic poem, the verses of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
  2. Lamentations 1:14 Most Hebrew manuscripts; many Hebrew manuscripts and Septuagint He kept watch over my sins
  3. Lamentations 1:15 Or has set a time for me / when he will