Add parallel Print Page Options

Chenjezo kwa Ansembe

“Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.” Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”

“Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.” Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire. Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa. Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.

“Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse. Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”

Kusakhulupirika kwa Yuda

10 Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?

11 Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo. 12 Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.

13 China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu. 14 Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.

15 Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.

16 Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.

Tsiku la Chiweruzo

17 Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu.

Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?”

Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”

Additional Warning to the Priests

“And now, you priests, this warning is for you.(A) If you do not listen,(B) and if you do not resolve to honor(C) my name,” says the Lord Almighty, “I will send a curse(D) on you, and I will curse your blessings.(E) Yes, I have already cursed them, because you have not resolved to honor me.

“Because of you I will rebuke your descendants[a]; I will smear on your faces the dung(F) from your festival sacrifices, and you will be carried off with it.(G) And you will know that I have sent you this warning so that my covenant with Levi(H) may continue,” says the Lord Almighty. “My covenant was with him, a covenant(I) of life and peace,(J) and I gave them to him; this called for reverence(K) and he revered me and stood in awe of my name. True instruction(L) was in his mouth and nothing false was found on his lips. He walked(M) with me in peace(N) and uprightness,(O) and turned many from sin.(P)

“For the lips of a priest(Q) ought to preserve knowledge, because he is the messenger(R) of the Lord Almighty and people seek instruction from his mouth.(S) But you have turned from the way(T) and by your teaching have caused many to stumble;(U) you have violated the covenant(V) with Levi,”(W) says the Lord Almighty. “So I have caused you to be despised(X) and humiliated(Y) before all the people, because you have not followed my ways but have shown partiality(Z) in matters of the law.”(AA)

Breaking Covenant Through Divorce

10 Do we not all have one Father[b]?(AB) Did not one God create us?(AC) Why do we profane the covenant(AD) of our ancestors by being unfaithful(AE) to one another?

11 Judah has been unfaithful. A detestable(AF) thing has been committed in Israel and in Jerusalem: Judah has desecrated the sanctuary the Lord loves(AG) by marrying(AH) women who worship a foreign god.(AI) 12 As for the man who does this, whoever he may be, may the Lord remove(AJ) him from the tents of Jacob[c](AK)—even though he brings an offering(AL) to the Lord Almighty.

13 Another thing you do: You flood the Lord’s altar with tears.(AM) You weep and wail(AN) because he no longer looks with favor(AO) on your offerings or accepts them with pleasure from your hands.(AP) 14 You ask,(AQ) “Why?” It is because the Lord is the witness(AR) between you and the wife of your youth.(AS) You have been unfaithful to her, though she is your partner, the wife of your marriage covenant.(AT)

15 Has not the one God made you?(AU) You belong to him in body and spirit. And what does the one God seek? Godly offspring.[d](AV) So be on your guard,(AW) and do not be unfaithful(AX) to the wife of your youth.

16 “The man who hates and divorces his wife,(AY)” says the Lord, the God of Israel, “does violence to the one he should protect,”[e](AZ) says the Lord Almighty.

So be on your guard,(BA) and do not be unfaithful.

Breaking Covenant Through Injustice

17 You have wearied(BB) the Lord with your words.

“How have we wearied him?” you ask.(BC)

By saying, “All who do evil are good in the eyes of the Lord, and he is pleased(BD) with them” or “Where is the God of justice?(BE)

Footnotes

  1. Malachi 2:3 Or will blight your grain
  2. Malachi 2:10 Or father
  3. Malachi 2:12 Or 12 May the Lord remove from the tents of Jacob anyone who gives testimony in behalf of the man who does this
  4. Malachi 2:15 The meaning of the Hebrew for the first part of this verse is uncertain.
  5. Malachi 2:16 Or “I hate divorce,” says the Lord, the God of Israel, “because the man who divorces his wife covers his garment with violence,”