Add parallel Print Page Options

Mawu a Stefano

Kenaka mkulu wa ansembe anafunsa Stefano kuti, “Kodi zimene akukunenerazi ndi zoona?”

Stefano anayankha kuti, “Abale ndi makolo, tamverani! Mulungu waulemerero anaoneka kwa kholo lathu Abrahamu pamene ankakhala ku Mesopotamiya, asanakakhale ku Harani. Mulungu anati, ‘Tuluka mʼdziko lako, siya abale ako, ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.’

“Ndipo iye anatulukadi mʼdziko la Akaldeya ndi kukakhala ku Harani. Atamwalira abambo ake, Mulungu anamuchotsa kumeneko ndi kumubweretsa mʼdziko lino limene inu mukukhalamo tsopano. Mulungu sanamupatse cholowa kuno, ngakhale kadera kakangʼono kadziko. Koma Mulungu anamulonjeza kuti adzapereka dziko lino kwa iye ndi kwa zidzukulu zake, ngakhale kuti pa nthawi imeneyi analibe mwana. Mulungu anayankhula motere kwa iye: ‘Zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo, ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.’ Mulungu anati, ‘Ine ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo, ndipo pambuyo pake akadzatuluka mʼdzikolo adzandipembedza Ine pamalo pano.’ Kenaka Mulungu anachita pangano la mdulidwe ndi Abrahamu. Ndipo Abrahamu, anabereka Isake, namudula ali ndi masiku asanu ndi atatu. Ndipo Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka makolo khumi ndi awiri aja.

“Makolo athu anachita nsanje ndi Yosefe ndipo anamugulitsa kuti akakhale kapolo ku Igupto. Koma Mulungu anali naye 10 ndipo anamupulumutsa iye kumasautso ake onse. Mulungu anamupatsa Yosefe nzeru ndi chisomo pamaso pa Farao mfumu ya ku Igupto, kotero mfumuyo inamuyika iye kukhala nduna yayikulu ya dziko la Igupto ndiponso nyumba yake yonse yaufumu.

11 “Kenaka munalowa njala mʼdziko la Kanaani, kotero kuti anthu anavutika kwambiri, ndipo makolo athu sanathe kupeza chakudya. 12 Pamene Yakobo anamva kuti ku Igupto kunali tirigu, iye anatuma makolo athu ulendo woyamba. 13 Pa ulendo wawo wachiwiri, Yosefe anadziwulula kwa abale akewo ndipo Farao anadziwa za banja la Yosefe. 14 Izi zinachitika, Yosefe anayitanitsa abambo ake Yakobo ndi banja lonse, onse pamodzi analipo 75. 15 Motero Yakobo anapita ku Igupto, kumene iye ndiponso makolo athu anamwalira. 16 Mitembo yawo anayinyamula ndi kupita nayo ku Sekemu kumene inayikidwa mʼmanda amene Abrahamu anagula kochokera kwa ana a Hamori ku Sekemuko.

17 “Nthawi itayandikira yakuti Mulungu achite zimene analonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu unakula ndi kuchuluka kwambiri mu Igupto. 18 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto. 19 Mfumuyo inachita mwachinyengo ndi mtundu wathu ndi kuwazunza kuti ataye ana awo akhanda kuti afe.

20 “Pa nthawi imeneyo Mose anabadwa, ndipo anali wokongola kwambiri. Iye analeredwa mʼnyumba ya abambo ake kwa miyezi itatu. 21 Atakamutaya, mwana wamkazi wa Farao anamutola nakamulera ngati mwana wake. 22 Mose anaphunzira nzeru zonse za Aigupto, ndipo anali wamphamvu mʼmawu ndi ntchito zake.

23 “Mose ali ndi zaka makumi anayi, anaganizira zokayendera abale ake Aisraeli. 24 Iye ataona mmodzi wa iwo akuzunzidwa ndi Mwigupto, anatchinjiriza Mwisraeliyo, namupha Mwiguptoyo. 25 Mose anaganiza kuti abale ake adzazindikira kuti Mulungu anamuyika kuti awapulumutse koma iwo sanazindikire. 26 Mmawa mwake Mose anaona Aisraeli awiri akukangana. Iye anayesa kuwayanjanitsa ponena kuti, ‘Amuna inu, ndinu abale; chifukwa chiyani mukufuna kupwetekana?’

27 “Koma munthu amene amavutitsa mnzakeyo anakankha Mose ndipo anati, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza. 28 Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja dzulo?’ 29 Mose atamva mawu awa anathawira ku Midiyani, kumene anakhala mlendo ndipo anabereka ana amuna awiri.

30 “Ndipo patapita zaka makumi anayi mngelo anaonekera kwa Mose mʼmalawi amoto pa chitsamba mʼchipululu pafupi ndi Phiri la Sinai. 31 Iye ataona zimenezi, anadabwa. Akupita kuti akaonetsetse pafupi, Mose anamva mawu a Ambuye: 32 ‘Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.’ Mose ananjenjemera chifukwa cha mantha ndipo sanalimbe mtima kuyangʼananso.

33 “Ndipo Ambuye anati kwa Mose, ‘Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika. 34 Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse. Tsopano tiye ndikutume ku Igupto.’

35 “Uyu ndi Mose yemwe uja amene Aisraeli anamukana ndi kunena kuti, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza?’ Iyeyo anatumidwa ndi Mulungu mwini kuti akakhale wowalamulira ndiponso mpulumutsi, mothandizidwa ndi mngelo amene anamuonekera pa chitsamba. 36 Iye anawatulutsa mu Igupto ndipo anachita zodabwitsa ndi zizindikiro zozizwitsa mu Igupto, pa Nyanja Yofiira, ndiponso mʼchipululu kwa zaka makumi anayi.

37 “Uyu ndi Mose uja amene anati kwa Aisraeli, ‘Mulungu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine.’ 38 Iyeyu anali mʼgulu la Aisraeli mʼchipululu pamodzi ndi mngelo amene anamuyankhula pa phiri la Sinai ndiponso makolo athu; ndipo Mose analandira mawu amoyo kuti atipatse ife.

39 “Koma makolo athu anakana kumumvera iye. Iwo anamukana iye ndipo mʼmitima mwawo anatembenukira ku Igupto. 40 Iwo anati kwa Aaroni, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitsogolera kutuluka mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira. 41 Iyi ndi nthawi imene anapanga fano la mwana wangʼombe. Anapereka nsembe kwa fanoli nachita chikondwerero kulemekeza ntchito ya manja awo. 42 Koma Mulungu anawafulatira, nawapereka kuti apembedze zolengedwa zakumwamba. Zimenezi zikugwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la aneneri kuti,

“ ‘Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja
    munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?’
43 Ayi, inu mwanyamula tenti ya Moloki
    ndi nyenyezi ya mulungu wanu Refani,
    mafano amene munapanga kuti muziwapembedza.
Chifukwa chake, Ine ndidzakutumizani kutali, kupitirira dziko la Babuloni.

44 “Makolo athu anali ndi tenti ya msonkhano pakati pawo mʼchipululu. Anayipanga monga momwe Mulungu anawuzira Mose, molingana ndi chithunzi chimene Mose anachiona. 45 Makolo athu, atayilandira Tentiyo, anabwera nayo motsogozedwa ndi Yoswa pamene analanda dziko la mitundu imene Mulungu anayipirikitsa pamaso pawo. Tentiyo inakhala mʼdzikomo mpaka nthawi ya Davide, 46 amene anapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndipo anapempha kuti amʼmangire nyumba Mulungu wa Yakobo. 47 Koma anali Solomoni amene anamanga nyumbayo.

48 “Komatu, Wammwambamwambayo sakhala mʼnyumba zomangidwa ndi anthu. Monga mneneri akunena kuti,

49 “ ‘Kumwamba ndi mpando wanga waufumu,
    ndipo dziko lapansi ndi chopondapo mapazi anga.
Kodi mudzandimangira nyumba yotani?
            Akutero Ambuye.
    Kapena malo opumuliramo Ine ali kuti?
50 Kodi si dzanja langa linapanga zonsezi?’

51 “Anthu wokanika inu, osachita mdulidwe wa mu mtima ndi a makutu ogontha! Inu ofanana ndi makolo anu. Nthawi zonse mumakana kumvera Mzimu Woyera: 52 Kodi analipo mneneri amene makolo anu sanamuzunze? Iwo anapha ngakhale amene ananeneratu za kubwera kwa Wolungamayo. Ndipo tsopano inu munamupereka ndi kumupha Iye. 53 Inu amene munalandira Malamulo amene anaperekedwa ndi angelo ndipo simunawamvere.”

Kuphedwa kwa Stefano

54 Atamva zimenezi, iwo anakwiya kwambiri ndipo anamukukutira mano. 55 Koma Stefano, wodzaza ndi Mzimu Woyera, anayangʼana kumwamba ndipo anaona ulemerero wa Mulungu ndiponso Yesu atayimirira ku dzanja lamanja la Mulungu. 56 Stefano anati, “Taonani, ndikuona kumwamba kotsekuka ndiponso Mwana wa Munthu atayimirira ku dzanja la manja la Mulungu.”

57 Koma iwo anatseka mʼmakutu mwawo, ndipo anafuwula kolimba, onse anathamangira kwa iye, 58 anamukokera kunja kwa mzinda ndipo anayamba kumugenda miyala. Mboni zinasungitsa zovala zawo kwa mnyamata otchedwa Saulo.

59 Akumugenda miyala, Stefano anapemphera kuti, “Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.” 60 Ndipo anagwada pansi nafuwula mwamphamvu kuti, “Ambuye musawawerengere tchimoli.” Atanena mawu amenewa anamwalira.

Stephen’s Speech to the Sanhedrin

Then the high priest asked Stephen, “Are these charges true?”

To this he replied: “Brothers and fathers,(A) listen to me! The God of glory(B) appeared to our father Abraham while he was still in Mesopotamia, before he lived in Harran.(C) ‘Leave your country and your people,’ God said, ‘and go to the land I will show you.’[a](D)

“So he left the land of the Chaldeans and settled in Harran. After the death of his father, God sent him to this land where you are now living.(E) He gave him no inheritance here,(F) not even enough ground to set his foot on. But God promised him that he and his descendants after him would possess the land,(G) even though at that time Abraham had no child. God spoke to him in this way: ‘For four hundred years your descendants will be strangers in a country not their own, and they will be enslaved and mistreated.(H) But I will punish the nation they serve as slaves,’ God said, ‘and afterward they will come out of that country and worship me in this place.’[b](I) Then he gave Abraham the covenant of circumcision.(J) And Abraham became the father of Isaac and circumcised him eight days after his birth.(K) Later Isaac became the father of Jacob,(L) and Jacob became the father of the twelve patriarchs.(M)

“Because the patriarchs were jealous of Joseph,(N) they sold him as a slave into Egypt.(O) But God was with him(P) 10 and rescued him from all his troubles. He gave Joseph wisdom and enabled him to gain the goodwill of Pharaoh king of Egypt. So Pharaoh made him ruler over Egypt and all his palace.(Q)

11 “Then a famine struck all Egypt and Canaan, bringing great suffering, and our ancestors could not find food.(R) 12 When Jacob heard that there was grain in Egypt, he sent our forefathers on their first visit.(S) 13 On their second visit, Joseph told his brothers who he was,(T) and Pharaoh learned about Joseph’s family.(U) 14 After this, Joseph sent for his father Jacob and his whole family,(V) seventy-five in all.(W) 15 Then Jacob went down to Egypt, where he and our ancestors died.(X) 16 Their bodies were brought back to Shechem and placed in the tomb that Abraham had bought from the sons of Hamor at Shechem for a certain sum of money.(Y)

17 “As the time drew near for God to fulfill his promise to Abraham, the number of our people in Egypt had greatly increased.(Z) 18 Then ‘a new king, to whom Joseph meant nothing, came to power in Egypt.’[c](AA) 19 He dealt treacherously with our people and oppressed our ancestors by forcing them to throw out their newborn babies so that they would die.(AB)

20 “At that time Moses was born, and he was no ordinary child.[d] For three months he was cared for by his family.(AC) 21 When he was placed outside, Pharaoh’s daughter took him and brought him up as her own son.(AD) 22 Moses was educated in all the wisdom of the Egyptians(AE) and was powerful in speech and action.

23 “When Moses was forty years old, he decided to visit his own people, the Israelites. 24 He saw one of them being mistreated by an Egyptian, so he went to his defense and avenged him by killing the Egyptian. 25 Moses thought that his own people would realize that God was using him to rescue them, but they did not. 26 The next day Moses came upon two Israelites who were fighting. He tried to reconcile them by saying, ‘Men, you are brothers; why do you want to hurt each other?’

27 “But the man who was mistreating the other pushed Moses aside and said, ‘Who made you ruler and judge over us?(AF) 28 Are you thinking of killing me as you killed the Egyptian yesterday?’[e] 29 When Moses heard this, he fled to Midian, where he settled as a foreigner and had two sons.(AG)

30 “After forty years had passed, an angel appeared to Moses in the flames of a burning bush in the desert near Mount Sinai. 31 When he saw this, he was amazed at the sight. As he went over to get a closer look, he heard the Lord say:(AH) 32 ‘I am the God of your fathers,(AI) the God of Abraham, Isaac and Jacob.’[f] Moses trembled with fear and did not dare to look.(AJ)

33 “Then the Lord said to him, ‘Take off your sandals, for the place where you are standing is holy ground.(AK) 34 I have indeed seen the oppression of my people in Egypt. I have heard their groaning and have come down to set them free. Now come, I will send you back to Egypt.’[g](AL)

35 “This is the same Moses they had rejected with the words, ‘Who made you ruler and judge?’(AM) He was sent to be their ruler and deliverer by God himself, through the angel who appeared to him in the bush. 36 He led them out of Egypt(AN) and performed wonders and signs(AO) in Egypt, at the Red Sea(AP) and for forty years in the wilderness.(AQ)

37 “This is the Moses who told the Israelites, ‘God will raise up for you a prophet like me from your own people.’[h](AR) 38 He was in the assembly in the wilderness, with the angel(AS) who spoke to him on Mount Sinai, and with our ancestors;(AT) and he received living words(AU) to pass on to us.(AV)

39 “But our ancestors refused to obey him. Instead, they rejected him and in their hearts turned back to Egypt.(AW) 40 They told Aaron, ‘Make us gods who will go before us. As for this fellow Moses who led us out of Egypt—we don’t know what has happened to him!’[i](AX) 41 That was the time they made an idol in the form of a calf. They brought sacrifices to it and reveled in what their own hands had made.(AY) 42 But God turned away from them(AZ) and gave them over to the worship of the sun, moon and stars.(BA) This agrees with what is written in the book of the prophets:

“‘Did you bring me sacrifices and offerings
    forty years in the wilderness, people of Israel?
43 You have taken up the tabernacle of Molek
    and the star of your god Rephan,
    the idols you made to worship.
Therefore I will send you into exile’[j](BB) beyond Babylon.

44 “Our ancestors had the tabernacle of the covenant law(BC) with them in the wilderness. It had been made as God directed Moses, according to the pattern he had seen.(BD) 45 After receiving the tabernacle, our ancestors under Joshua brought it with them when they took the land from the nations God drove out before them.(BE) It remained in the land until the time of David,(BF) 46 who enjoyed God’s favor and asked that he might provide a dwelling place for the God of Jacob.[k](BG) 47 But it was Solomon who built a house for him.(BH)

48 “However, the Most High(BI) does not live in houses made by human hands.(BJ) As the prophet says:

49 “‘Heaven is my throne,
    and the earth is my footstool.(BK)
What kind of house will you build for me?
says the Lord.
    Or where will my resting place be?
50 Has not my hand made all these things?’[l](BL)

51 “You stiff-necked people!(BM) Your hearts(BN) and ears are still uncircumcised. You are just like your ancestors: You always resist the Holy Spirit! 52 Was there ever a prophet your ancestors did not persecute?(BO) They even killed those who predicted the coming of the Righteous One. And now you have betrayed and murdered him(BP) 53 you who have received the law that was given through angels(BQ) but have not obeyed it.”

The Stoning of Stephen

54 When the members of the Sanhedrin heard this, they were furious(BR) and gnashed their teeth at him. 55 But Stephen, full of the Holy Spirit,(BS) looked up to heaven and saw the glory of God, and Jesus standing at the right hand of God.(BT) 56 “Look,” he said, “I see heaven open(BU) and the Son of Man(BV) standing at the right hand of God.”

57 At this they covered their ears and, yelling at the top of their voices, they all rushed at him, 58 dragged him out of the city(BW) and began to stone him.(BX) Meanwhile, the witnesses(BY) laid their coats(BZ) at the feet of a young man named Saul.(CA)

59 While they were stoning him, Stephen prayed, “Lord Jesus, receive my spirit.”(CB) 60 Then he fell on his knees(CC) and cried out, “Lord, do not hold this sin against them.”(CD) When he had said this, he fell asleep.(CE)

Footnotes

  1. Acts 7:3 Gen. 12:1
  2. Acts 7:7 Gen. 15:13,14
  3. Acts 7:18 Exodus 1:8
  4. Acts 7:20 Or was fair in the sight of God
  5. Acts 7:28 Exodus 2:14
  6. Acts 7:32 Exodus 3:6
  7. Acts 7:34 Exodus 3:5,7,8,10
  8. Acts 7:37 Deut. 18:15
  9. Acts 7:40 Exodus 32:1
  10. Acts 7:43 Amos 5:25-27 (see Septuagint)
  11. Acts 7:46 Some early manuscripts the house of Jacob
  12. Acts 7:50 Isaiah 66:1,2