Add parallel Print Page Options

Kuyesedwa kwa Yesu

Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu, kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.

Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”

Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’ ”

Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi. Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna. Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”

Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’ ”

Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano. 10 Pakuti kwalembedwa,

“Adzalamulira angelo ake za iwe
    kuti akutchinjirize mosamala;
11 ndipo adzakunyamula ndi manja awo,
    kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”

12 Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’ ”

13 Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.

Yesu Akanidwa ku Nazareti

14 Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi. 15 Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.

16 Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba. 17 Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,

18 “Mzimu wa Ambuye ali pa Ine;
    chifukwa wandidzoza
    kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka.
Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe
    ndi kwa osaona kuti apenyenso,
kumasulidwa kwa osautsidwa,
19     ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”

20 Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye, 21 ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”

22 Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”

23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”

24 Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo. 25 Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo. 26 Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni. 27 Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”

28 Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi. 29 Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho. 30 Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.

Yesu Atulutsa Mzimu Woyipa

31 Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu. 32 Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.

33 Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti 34 “Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”

35 Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.

36 Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!” 37 Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize. 39 Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.

40 Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa. 41 Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.

42 Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere. 43 Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.” 44 Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.

Jesus Is Tested in the Wilderness(A)

Jesus, full of the Holy Spirit,(B) left the Jordan(C) and was led by the Spirit(D) into the wilderness, where for forty days(E) he was tempted[a] by the devil.(F) He ate nothing during those days, and at the end of them he was hungry.

The devil said to him, “If you are the Son of God,(G) tell this stone to become bread.”

Jesus answered, “It is written: ‘Man shall not live on bread alone.’[b](H)

The devil led him up to a high place and showed him in an instant all the kingdoms of the world.(I) And he said to him, “I will give you all their authority and splendor; it has been given to me,(J) and I can give it to anyone I want to. If you worship me, it will all be yours.”

Jesus answered, “It is written: ‘Worship the Lord your God and serve him only.’[c](K)

The devil led him to Jerusalem and had him stand on the highest point of the temple. “If you are the Son of God,” he said, “throw yourself down from here. 10 For it is written:

“‘He will command his angels concerning you
    to guard you carefully;
11 they will lift you up in their hands,
    so that you will not strike your foot against a stone.’[d](L)

12 Jesus answered, “It is said: ‘Do not put the Lord your God to the test.’[e](M)

13 When the devil had finished all this tempting,(N) he left him(O) until an opportune time.

Jesus Rejected at Nazareth

14 Jesus returned to Galilee(P) in the power of the Spirit, and news about him spread through the whole countryside.(Q) 15 He was teaching in their synagogues,(R) and everyone praised him.

16 He went to Nazareth,(S) where he had been brought up, and on the Sabbath day he went into the synagogue,(T) as was his custom. He stood up to read,(U) 17 and the scroll of the prophet Isaiah was handed to him. Unrolling it, he found the place where it is written:

18 “The Spirit of the Lord is on me,(V)
    because he has anointed me
    to proclaim good news(W) to the poor.
He has sent me to proclaim freedom for the prisoners
    and recovery of sight for the blind,
to set the oppressed free,
19     to proclaim the year of the Lord’s favor.”[f](X)

20 Then he rolled up the scroll, gave it back to the attendant and sat down.(Y) The eyes of everyone in the synagogue were fastened on him. 21 He began by saying to them, “Today this scripture is fulfilled(Z) in your hearing.”

22 All spoke well of him and were amazed at the gracious words that came from his lips. “Isn’t this Joseph’s son?” they asked.(AA)

23 Jesus said to them, “Surely you will quote this proverb to me: ‘Physician, heal yourself!’ And you will tell me, ‘Do here in your hometown(AB) what we have heard that you did in Capernaum.’”(AC)

24 “Truly I tell you,” he continued, “no prophet is accepted in his hometown.(AD) 25 I assure you that there were many widows in Israel in Elijah’s time, when the sky was shut for three and a half years and there was a severe famine throughout the land.(AE) 26 Yet Elijah was not sent to any of them, but to a widow in Zarephath in the region of Sidon.(AF) 27 And there were many in Israel with leprosy[g] in the time of Elisha the prophet, yet not one of them was cleansed—only Naaman the Syrian.”(AG)

28 All the people in the synagogue were furious when they heard this. 29 They got up, drove him out of the town,(AH) and took him to the brow of the hill on which the town was built, in order to throw him off the cliff. 30 But he walked right through the crowd and went on his way.(AI)

Jesus Drives Out an Impure Spirit(AJ)

31 Then he went down to Capernaum,(AK) a town in Galilee, and on the Sabbath he taught the people. 32 They were amazed at his teaching,(AL) because his words had authority.(AM)

33 In the synagogue there was a man possessed by a demon, an impure spirit. He cried out at the top of his voice, 34 “Go away! What do you want with us,(AN) Jesus of Nazareth?(AO) Have you come to destroy us? I know who you are(AP)—the Holy One of God!”(AQ)

35 “Be quiet!” Jesus said sternly.(AR) “Come out of him!” Then the demon threw the man down before them all and came out without injuring him.

36 All the people were amazed(AS) and said to each other, “What words these are! With authority(AT) and power he gives orders to impure spirits and they come out!” 37 And the news about him spread throughout the surrounding area.(AU)

Jesus Heals Many(AV)(AW)

38 Jesus left the synagogue and went to the home of Simon. Now Simon’s mother-in-law was suffering from a high fever, and they asked Jesus to help her. 39 So he bent over her and rebuked(AX) the fever, and it left her. She got up at once and began to wait on them.

40 At sunset, the people brought to Jesus all who had various kinds of sickness, and laying his hands on each one,(AY) he healed them.(AZ) 41 Moreover, demons came out of many people, shouting, “You are the Son of God!”(BA) But he rebuked(BB) them and would not allow them to speak,(BC) because they knew he was the Messiah.

42 At daybreak, Jesus went out to a solitary place. The people were looking for him and when they came to where he was, they tried to keep him from leaving them. 43 But he said, “I must proclaim the good news of the kingdom of God(BD) to the other towns also, because that is why I was sent.” 44 And he kept on preaching in the synagogues of Judea.(BE)

Footnotes

  1. Luke 4:2 The Greek for tempted can also mean tested.
  2. Luke 4:4 Deut. 8:3
  3. Luke 4:8 Deut. 6:13
  4. Luke 4:11 Psalm 91:11,12
  5. Luke 4:12 Deut. 6:16
  6. Luke 4:19 Isaiah 61:1,2 (see Septuagint); Isaiah 58:6
  7. Luke 4:27 The Greek word traditionally translated leprosy was used for various diseases affecting the skin.