Add parallel Print Page Options

Yohane Mʼbatizi Akonza Njira

Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene. Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu. Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo. Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti:

“Mawu a wofuwula mʼchipululu,
konzani njira ya Ambuye,
    wongolani njira zake.
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa
    ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa,
misewu yokhotakhota idzawongoledwa,
    ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”

Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera? Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana. Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”

10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”

11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”

12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”

13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.” 14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?”

Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”

15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu. 16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto. 17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.” 18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.

19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita, 20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.

Ubatizo wa Yesu

21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka. 22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”

Makolo a Yesu

23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe,

mwana wa Heli, 24 mwana wa Matate,

mwana wa Levi, mwana wa Meliki,

mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe

25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi,

mwana wa Naomi, mwana wa Esli,

mwana wa Nagai, 26 mwana wa Maati,

mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni,

mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda

27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa,

mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli,

mwana wa Neri, 28 mwana wa Meliki,

mwana wa Adi, mwana wa Kosamu,

mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,

29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara,

mwana wa Yorimu, mwana wa Matati,

mwana wa Levi, 30 mwana wa Simeoni,

mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe,

mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,

31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena,

mwana wa Matata, mwana wa Natani,

mwana wa Davide, 32 mwana wa Yese,

mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi,

mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,

33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni,

mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi,

mwana wa Yuda, 34 mwana wa Yakobo,

mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu,

mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,

35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu,

mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi,

mwana wa Sela, 36 mwana wa Kainane,

mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu,

mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,

37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki,

mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli,

mwana wa Kainane, 38 mwana wa Enosi,

mwana wa Seti,

mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

John the Baptist Prepares the Way(A)(B)

In the fifteenth year of the reign of Tiberius Caesar—when Pontius Pilate(C) was governor of Judea, Herod(D) tetrarch of Galilee, his brother Philip tetrarch of Iturea and Traconitis, and Lysanias tetrarch of Abilene— during the high-priesthood of Annas and Caiaphas,(E) the word of God came to John(F) son of Zechariah(G) in the wilderness. He went into all the country around the Jordan, preaching a baptism of repentance for the forgiveness of sins.(H) As it is written in the book of the words of Isaiah the prophet:

“A voice of one calling in the wilderness,
‘Prepare the way for the Lord,
    make straight paths for him.
Every valley shall be filled in,
    every mountain and hill made low.
The crooked roads shall become straight,
    the rough ways smooth.
And all people will see God’s salvation.’”[a](I)

John said to the crowds coming out to be baptized by him, “You brood of vipers!(J) Who warned you to flee from the coming wrath?(K) Produce fruit in keeping with repentance. And do not begin to say to yourselves, ‘We have Abraham as our father.’(L) For I tell you that out of these stones God can raise up children for Abraham. The ax is already at the root of the trees, and every tree that does not produce good fruit will be cut down and thrown into the fire.”(M)

10 “What should we do then?”(N) the crowd asked.

11 John answered, “Anyone who has two shirts should share with the one who has none, and anyone who has food should do the same.”(O)

12 Even tax collectors came to be baptized.(P) “Teacher,” they asked, “what should we do?”

13 “Don’t collect any more than you are required to,”(Q) he told them.

14 Then some soldiers asked him, “And what should we do?”

He replied, “Don’t extort money and don’t accuse people falsely(R)—be content with your pay.”

15 The people were waiting expectantly and were all wondering in their hearts if John(S) might possibly be the Messiah.(T) 16 John answered them all, “I baptize you with[b] water.(U) But one who is more powerful than I will come, the straps of whose sandals I am not worthy to untie. He will baptize you with[c] the Holy Spirit and fire.(V) 17 His winnowing fork(W) is in his hand to clear his threshing floor and to gather the wheat into his barn, but he will burn up the chaff with unquenchable fire.”(X) 18 And with many other words John exhorted the people and proclaimed the good news to them.

19 But when John rebuked Herod(Y) the tetrarch because of his marriage to Herodias, his brother’s wife, and all the other evil things he had done, 20 Herod added this to them all: He locked John up in prison.(Z)

The Baptism and Genealogy of Jesus(AA)(AB)

21 When all the people were being baptized, Jesus was baptized too. And as he was praying,(AC) heaven was opened 22 and the Holy Spirit descended on him(AD) in bodily form like a dove. And a voice came from heaven: “You are my Son,(AE) whom I love; with you I am well pleased.”(AF)

23 Now Jesus himself was about thirty years old when he began his ministry.(AG) He was the son, so it was thought, of Joseph,(AH)

the son of Heli, 24 the son of Matthat,

the son of Levi, the son of Melki,

the son of Jannai, the son of Joseph,

25 the son of Mattathias, the son of Amos,

the son of Nahum, the son of Esli,

the son of Naggai, 26 the son of Maath,

the son of Mattathias, the son of Semein,

the son of Josek, the son of Joda,

27 the son of Joanan, the son of Rhesa,

the son of Zerubbabel,(AI) the son of Shealtiel,

the son of Neri, 28 the son of Melki,

the son of Addi, the son of Cosam,

the son of Elmadam, the son of Er,

29 the son of Joshua, the son of Eliezer,

the son of Jorim, the son of Matthat,

the son of Levi, 30 the son of Simeon,

the son of Judah, the son of Joseph,

the son of Jonam, the son of Eliakim,

31 the son of Melea, the son of Menna,

the son of Mattatha, the son of Nathan,(AJ)

the son of David, 32 the son of Jesse,

the son of Obed, the son of Boaz,

the son of Salmon,[d] the son of Nahshon,

33 the son of Amminadab, the son of Ram,[e]

the son of Hezron, the son of Perez,(AK)

the son of Judah, 34 the son of Jacob,

the son of Isaac, the son of Abraham,

the son of Terah, the son of Nahor,(AL)

35 the son of Serug, the son of Reu,

the son of Peleg, the son of Eber,

the son of Shelah, 36 the son of Cainan,

the son of Arphaxad,(AM) the son of Shem,

the son of Noah, the son of Lamech,(AN)

37 the son of Methuselah, the son of Enoch,

the son of Jared, the son of Mahalalel,

the son of Kenan,(AO) 38 the son of Enosh,

the son of Seth, the son of Adam,

the son of God.(AP)

Footnotes

  1. Luke 3:6 Isaiah 40:3-5
  2. Luke 3:16 Or in
  3. Luke 3:16 Or in
  4. Luke 3:32 Some early manuscripts Sala
  5. Luke 3:33 Some manuscripts Amminadab, the son of Admin, the son of Arni; other manuscripts vary widely.