Add parallel Print Page Options

Ansembe Ayamba Kutumikira

Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Mose anayitana Aaroni, ana ake ndi akuluakulu a Aisraeli. Ndipo anawuza Aaroni kuti, “Tenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yako yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. Zonsezi zikhale zopanda chilema ndipo uzipereke pamaso pa Yehova. Kenaka uwawuze Aisraeli kuti, ‘Tengani mbuzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. Mutengenso mwana wangʼombe ndi mwana wankhosa. Zonsezi zikhale za chaka chimodzi ndi zopanda chilema kuti zikhale nsembe yopsereza. Mutengenso ngʼombe yayimuna ndi nkhosa yayimuna kuti zikhale nsembe yachiyanjano zoti ziperekedwe pamaso pa Yehova. Pamodzi ndi izi mubwerenso ndi nsembe yachakudya yosakaniza ndi mafuta pakuti lero Yehova akuonekerani.’ ”

Anthu anatenga zonse zimene Mose analamula nabwera nazo pa khomo la tenti ya msonkhano. Gululo linasendera pafupi ndi kuyima pamaso pa Yehova. Tsono Mose anati, “Izi ndi zimene Yehova walamula kuti muchite kuti ulemerero wa Yehova ukuonekereni.”

Pambuyo pake Mose anawuza Aaroni kuti, “Sendera pafupi ndi guwa ndipo upereka nsembe yako yopepesera machimo ndi nsembe yako yopsereza ndikuchita mwambo wopepesera machimo ako ndi machimo a anthu. Anthuwa apereke nsembe zawo zopepesera machimo monga momwe Yehova walamulira.”

Choncho Aaroni anasendera pafupi ndi guwa, napha mwana wangʼombe uja kukhala nsembe yake yopepesera machimo. Ana a Aaroni anabwera ndi magazi kwa Aaroni ndipo iye anaviyika chala chake mʼmagaziwo, nawapaka pa nyanga za guwa. Magazi wotsalawo anawathira pa tsinde la guwalo. 10 Kenaka anatentha paguwapo, mafuta, impsyo pamodzi ndi mafuta amene amakuta chiwindi ngati nsembe yopepesera machimoyo, monga momwe Yehova analamulira Mose. 11 Koma nyama ndi chikopa anazitenthera kunja kwa msasa.

12 Kenaka anapha nsembe yopsereza. Ana a Aaroni atabwera ndi magazi kwa iye, Aaroniyo anawawaza mbali zonse za guwa. 13 Ana akewo anamupatsa nyama yoduladula ya nsembe yopsereza ija pamodzi ndi mutu ndipo anazitentha pa guwa. 14 Aaroni anatsuka matumbo ndi miyendo nazitentha pa guwa pamodzi ndi nsembe yopsereza ija.

15 Kenaka Aaroni anapereka zopereka za anthuwo. Anatenga mbuzi yopepesera machimo a anthuwo, yopereka chifukwa cha tchimo, nayipha ndi kuyipereka kuti ikhale yopepesera machimo monga anachitira ndi nsembe yoyamba ija.

16 Anabwera ndi nsembe yopsereza, nayipereka potsata mwambo wake. 17 Anabweranso ndi chopereka cha chakudya. Anatapa ufa dzanja limodzi ndi kutentha pa guwa, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa ija.

18 Tsono Aaroni anapha ngʼombe ndi nkhosa yayimuna monga nsembe yachiyanjano ya anthu. Ana ake anamupatsira magazi ndipo anawawaza mbali zonse za guwa. 19 Anamupatsiranso mafuta a ngʼombeyo ndi nkhosa yayimunayo: mchira wamafuta, mafuta wokuta matumbo, impsyo ndi mafuta wokuta chiwindi. 20 Ana a Aaroni anayika mafutawo pa zidale. Pambuyo pake Aaroni anatentha mafutawo pa guwa lansembe. 21 Koma zidale ndi ntchafu ya kumanja Aaroni anaziweyula ngati chopereka choweyula pamaso pa Yehova.

22 Kenaka Aaroni anakweza manja ake pa anthuwo nawadalitsa. Ndipo atatha kupereka nsembe yopepesera machimo, nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano, anatsika pa guwapo.

23 Ndipo Mose pamodzi ndi Aaroni analowa mu tenti ya msonkhano. Atatulukamo anadalitsa anthuwo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse. 24 Pomwepo moto unatuluka pamaso pa Yehova niwutentha nsembe zopsereza ndi mafuta zimene zinali pa guwa. Anthu onse ataona zimenezi anafuwula mwachimwemwe ndipo anaweramitsa nkhope zawo pansi.

The Priests Begin Their Ministry

On the eighth day(A) Moses summoned Aaron and his sons and the elders(B) of Israel. He said to Aaron, “Take a bull calf for your sin offering[a] and a ram for your burnt offering, both without defect, and present them before the Lord. Then say to the Israelites: ‘Take a male goat(C) for a sin offering,(D) a calf(E) and a lamb(F)—both a year old and without defect—for a burnt offering, and an ox[b](G) and a ram for a fellowship offering(H) to sacrifice before the Lord, together with a grain offering mixed with olive oil. For today the Lord will appear to you.(I)’”

They took the things Moses commanded to the front of the tent of meeting, and the entire assembly came near and stood before the Lord. Then Moses said, “This is what the Lord has commanded you to do, so that the glory of the Lord(J) may appear to you.”

Moses said to Aaron, “Come to the altar and sacrifice your sin offering and your burnt offering and make atonement for yourself and the people;(K) sacrifice the offering that is for the people and make atonement for them, as the Lord has commanded.(L)

So Aaron came to the altar and slaughtered the calf as a sin offering(M) for himself. His sons brought the blood to him,(N) and he dipped his finger into the blood and put it on the horns of the altar; the rest of the blood he poured out at the base of the altar.(O) 10 On the altar he burned the fat, the kidneys and the long lobe of the liver from the sin offering, as the Lord commanded Moses; 11 the flesh and the hide(P) he burned up outside the camp.(Q)

12 Then he slaughtered the burnt offering.(R) His sons handed him the blood,(S) and he splashed it against the sides of the altar. 13 They handed him the burnt offering piece by piece, including the head, and he burned them on the altar.(T) 14 He washed the internal organs and the legs and burned them on top of the burnt offering on the altar.(U)

15 Aaron then brought the offering that was for the people.(V) He took the goat for the people’s sin offering and slaughtered it and offered it for a sin offering as he did with the first one.

16 He brought the burnt offering and offered it in the prescribed way.(W) 17 He also brought the grain offering, took a handful of it and burned it on the altar in addition to the morning’s burnt offering.(X)

18 He slaughtered the ox and the ram as the fellowship offering for the people.(Y) His sons handed him the blood, and he splashed it against the sides of the altar. 19 But the fat portions of the ox and the ram—the fat tail, the layer of fat, the kidneys and the long lobe of the liver— 20 these they laid on the breasts, and then Aaron burned the fat on the altar. 21 Aaron waved the breasts and the right thigh before the Lord as a wave offering,(Z) as Moses commanded.

22 Then Aaron lifted his hands toward the people and blessed them.(AA) And having sacrificed the sin offering, the burnt offering and the fellowship offering, he stepped down.

23 Moses and Aaron then went into the tent of meeting.(AB) When they came out, they blessed the people; and the glory of the Lord(AC) appeared to all the people. 24 Fire(AD) came out from the presence of the Lord and consumed the burnt offering and the fat portions on the altar. And when all the people saw it, they shouted for joy and fell facedown.(AE)

Footnotes

  1. Leviticus 9:2 Or purification offering; here and throughout this chapter
  2. Leviticus 9:4 The Hebrew word can refer to either male or female; also in verses 18 and 19.