Add parallel Print Page Options

Malamulo a Ansembe

21 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake. Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake, kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha. Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.

“ ‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo. Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.

“ ‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo. Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.

“ ‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.

10 “ ‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni. 11 Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake. 12 Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.

13 “ ‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna. 14 Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake, 15 kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’ ”

16 Yehova anawuza Mose kuti, 17 “Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake. 18 Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri, 19 munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala, 20 kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi. 21 Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake. 22 Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika. 23 Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’ ”

24 Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.

Rules for Priests

21 The Lord said to Moses, “Speak to the priests, the sons of Aaron,(A) and say to them: ‘A priest must not make himself ceremonially unclean(B) for any of his people who die,(C) except for a close relative, such as his mother or father,(D) his son or daughter, his brother, or an unmarried sister who is dependent on him since she has no husband—for her he may make himself unclean.(E) He must not make himself unclean for people related to him by marriage,[a] and so defile himself.

“‘Priests must not shave(F) their heads or shave off the edges of their beards(G) or cut their bodies.(H) They must be holy to their God(I) and must not profane the name of their God.(J) Because they present the food offerings to the Lord,(K) the food of their God,(L) they are to be holy.(M)

“‘They must not marry women defiled by prostitution or divorced from their husbands,(N) because priests are holy to their God.(O) Regard them as holy,(P) because they offer up the food of your God.(Q) Consider them holy, because I the Lord am holy—I who make you holy.(R)

“‘If a priest’s daughter defiles herself by becoming a prostitute, she disgraces her father; she must be burned in the fire.(S)

10 “‘The high priest, the one among his brothers who has had the anointing oil poured on his head(T) and who has been ordained to wear the priestly garments,(U) must not let his hair become unkempt[b] or tear his clothes.(V) 11 He must not enter a place where there is a dead body.(W) He must not make himself unclean,(X) even for his father or mother,(Y) 12 nor leave the sanctuary(Z) of his God or desecrate it, because he has been dedicated by the anointing oil(AA) of his God. I am the Lord.

13 “‘The woman he marries must be a virgin.(AB) 14 He must not marry a widow, a divorced woman, or a woman defiled by prostitution, but only a virgin from his own people, 15 so that he will not defile his offspring among his people. I am the Lord, who makes him holy.’”

16 The Lord said to Moses, 17 “Say to Aaron: ‘For the generations to come none of your descendants who has a defect(AC) may come near to offer the food of his God.(AD) 18 No man who has any defect(AE) may come near: no man who is blind(AF) or lame,(AG) disfigured or deformed; 19 no man with a crippled foot or hand, 20 or who is a hunchback or a dwarf, or who has any eye defect, or who has festering or running sores or damaged testicles.(AH) 21 No descendant of Aaron the priest who has any defect(AI) is to come near to present the food offerings to the Lord.(AJ) He has a defect; he must not come near to offer the food of his God.(AK) 22 He may eat the most holy food of his God,(AL) as well as the holy food; 23 yet because of his defect,(AM) he must not go near the curtain or approach the altar, and so desecrate my sanctuary.(AN) I am the Lord, who makes them holy.(AO)’”

24 So Moses told this to Aaron and his sons and to all the Israelites.

Footnotes

  1. Leviticus 21:4 Or unclean as a leader among his people
  2. Leviticus 21:10 Or not uncover his head