Add parallel Print Page Options

Nsembe Zachakudya

“ ‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani, ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova. Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

“ ‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta. Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta. Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya. Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa. Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova. 10 Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

11 “ ‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi. 12 Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova. 13 Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.

14 “ ‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha. 15 Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya. 16 Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

The Grain Offering

“‘When anyone brings a grain offering(A) to the Lord, their offering is to be of the finest flour.(B) They are to pour olive oil(C) on it,(D) put incense on it(E) and take it to Aaron’s sons the priests. The priest shall take a handful of the flour(F) and oil, together with all the incense,(G) and burn this as a memorial[a] portion(H) on the altar, a food offering,(I) an aroma pleasing to the Lord.(J) The rest of the grain offering belongs to Aaron and his sons;(K) it is a most holy(L) part of the food offerings presented to the Lord.

“‘If you bring a grain offering baked in an oven,(M) it is to consist of the finest flour: either thick loaves made without yeast and with olive oil mixed in or thin loaves(N) made without yeast and brushed with olive oil.(O) If your grain offering is prepared on a griddle,(P) it is to be made of the finest flour mixed with oil, and without yeast. Crumble it and pour oil on it; it is a grain offering. If your grain offering is cooked in a pan,(Q) it is to be made of the finest flour and some olive oil. Bring the grain offering made of these things to the Lord; present it to the priest, who shall take it to the altar. He shall take out the memorial portion(R) from the grain offering and burn it on the altar as a food offering, an aroma pleasing to the Lord.(S) 10 The rest of the grain offering belongs to Aaron and his sons;(T) it is a most holy part of the food offerings presented to the Lord.(U)

11 “‘Every grain offering you bring to the Lord must be made without yeast,(V) for you are not to burn any yeast or honey in a food offering presented to the Lord. 12 You may bring them to the Lord as an offering of the firstfruits,(W) but they are not to be offered on the altar as a pleasing aroma. 13 Season all your grain offerings with salt.(X) Do not leave the salt of the covenant(Y) of your God out of your grain offerings; add salt to all your offerings.

14 “‘If you bring a grain offering of firstfruits(Z) to the Lord, offer crushed heads of new grain roasted in the fire. 15 Put oil and incense(AA) on it; it is a grain offering. 16 The priest shall burn the memorial portion(AB) of the crushed grain and the oil, together with all the incense,(AC) as a food offering presented to the Lord.(AD)

Footnotes

  1. Leviticus 2:2 Or representative; also in verses 9 and 16