Add parallel Print Page Options

Chiweruzo cha Israeli

“Ansembe inu, imvani izi!
    Inu Aisraeli, tcherani khutu!
Inu nyumba yaufumu, mvetserani!
    Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu:
Inu munali ngati msampha ku Mizipa,
    munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
Owukira azama mʼmoyo wakupha,
    Ine ndidzawalanga onsewo.
Ndimadziwa zonse za Efereimu;
    Aisraeli ndi osabisika kwa Ine.
Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere;
    Israeli wadziyipitsa.

“Ntchito zawo siziwalola
    kubwerera kwa Mulungu wawo.
Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere;
    Iwo sadziwa Yehova.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa;
    Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo;
    Yudanso anagwa nawo pamodzi.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo
    kukapereka nsembe kwa Yehova,
iwo sadzamupeza;
    Iye wawachokera.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova;
    amabereka ana amʼchigololo
ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano
    chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.

“Womba lipenga mu Gibeya,
    liza mbetete mu Rama.
Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni;
    iwe Benjamini tsogolera.
Efereimu adzasanduka bwinja
    pa tsiku la chilango.
Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi
    pakati pa mafuko a Israeli.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu
    amene amasuntha miyala ya mʼmalire.
Ndidzawakhutulira ukali wanga
    ngati madzi a chigumula.
11 Efereimu waponderezedwa,
    akulangidwa chifukwa chotsatira
    mafano.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu,
    ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.

13 “Efereimu ataona nthenda yake,
    ndi Yuda ataona zilonda zake,
pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya,
    ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza.
Koma mfumuyo singathe kukuchizani,
    singathe kuchiritsa mabala anu.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu.
    Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda.
Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo;
    ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga
    mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo.
Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga;
    mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”