Add parallel Print Page Options

Yehova Ayimba Mlandu Israeli

Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova,
    chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu
    amene mumakhala mʼdzikoli:
“Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi
    mulibe kulabadira za Mulungu.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha.
    Kuba ndi kuchita chigololo;
machimo achita kunyanya
    ndipo akungokhalira kuphana.
Chifukwa chake dziko likulira
    ndipo onse amene amakhalamo akuvutika;
zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga
    ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.

“Koma wina asapeze mnzake chifukwa,
    wina aliyense asayimbe mlandu mnzake,
pakuti anthu ako ali ngati anthu
    amene amayimba mlandu wansembe.
Mumapunthwa usana ndi usiku
    ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi.
Choncho ndidzawononga amayi anu.
    Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa.

“Pakuti mwakana kudziwa,
    Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga;
chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu,
    Inenso ndidzayiwala ana anu.
Ansembe ankati akachuluka
    iwo ankandichimwiranso kwambiri;
    iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga
    ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe.
    Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo,
    ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.

10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta;
    azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana,
chifukwa anasiya Yehova
kuti adzipereke 11     ku zachiwerewere,
ku vinyo wakale ndi watsopano,
    zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 za anthu anga.
Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo
    ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha.
Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa;
    iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri
    ndi kufukiza lubani pa zitunda,
pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi,
    pamene pali mthunzi wabwino.
Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere
    ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.

14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi
    pamene iwo adzachita zachiwerewere,
kapena akazi a ana anu
    pamene adzachita zigololo.
Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere,
    ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako.
    Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!

15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli,
    Yuda asapezeke ndi mlandu wotere.

“Usapite ku Giligala.
    Usapite ku Beti-Aveni.
    Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 Aisraeli ndi nkhutukumve,
    ngosamva ngati ana angʼombe.
Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji
    ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Efereimu waphathana ndi mafano;
    mulekeni!
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha,
    amapitiriza kuchita zachiwerewere;
    atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu
    ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

The Charge Against Israel

Hear the word of the Lord, you Israelites,
    because the Lord has a charge(A) to bring
    against you who live in the land:(B)
“There is no faithfulness,(C) no love,
    no acknowledgment(D) of God in the land.(E)
There is only cursing,[a] lying(F) and murder,(G)
    stealing(H) and adultery;(I)
they break all bounds,
    and bloodshed follows bloodshed.(J)
Because of this the land dries up,(K)
    and all who live in it waste away;(L)
the beasts of the field, the birds in the sky
    and the fish in the sea are swept away.(M)

“But let no one bring a charge,
    let no one accuse another,
for your people are like those
    who bring charges against a priest.(N)
You stumble(O) day and night,
    and the prophets stumble with you.
So I will destroy your mother(P)
    my people are destroyed from lack of knowledge.(Q)

“Because you have rejected knowledge,
    I also reject you as my priests;
because you have ignored the law(R) of your God,
    I also will ignore your children.
The more priests there were,
    the more they sinned against me;
    they exchanged their glorious God[b](S) for something disgraceful.(T)
They feed on the sins of my people
    and relish their wickedness.(U)
And it will be: Like people, like priests.(V)
    I will punish both of them for their ways
    and repay them for their deeds.(W)

10 “They will eat but not have enough;(X)
    they will engage in prostitution(Y) but not flourish,
because they have deserted(Z) the Lord
    to give themselves 11 to prostitution;(AA)
old wine(AB) and new wine
    take away their understanding.(AC)
12 My people consult a wooden idol,(AD)
    and a diviner’s rod speaks to them.(AE)
A spirit of prostitution(AF) leads them astray;(AG)
    they are unfaithful(AH) to their God.
13 They sacrifice on the mountaintops
    and burn offerings on the hills,
under oak,(AI) poplar and terebinth,
    where the shade is pleasant.(AJ)
Therefore your daughters turn to prostitution(AK)
    and your daughters-in-law to adultery.(AL)

14 “I will not punish your daughters
    when they turn to prostitution,
nor your daughters-in-law
    when they commit adultery,
because the men themselves consort with harlots(AM)
    and sacrifice with shrine prostitutes(AN)
    a people without understanding(AO) will come to ruin!(AP)

15 “Though you, Israel, commit adultery,
    do not let Judah become guilty.

“Do not go to Gilgal;(AQ)
    do not go up to Beth Aven.[c](AR)
    And do not swear, ‘As surely as the Lord lives!’(AS)
16 The Israelites are stubborn,(AT)
    like a stubborn heifer.(AU)
How then can the Lord pasture them
    like lambs(AV) in a meadow?
17 Ephraim is joined to idols;
    leave him alone!
18 Even when their drinks are gone,
    they continue their prostitution;
    their rulers dearly love shameful ways.
19 A whirlwind(AW) will sweep them away,
    and their sacrifices will bring them shame.(AX)

Footnotes

  1. Hosea 4:2 That is, to pronounce a curse on
  2. Hosea 4:7 Syriac (see also an ancient Hebrew scribal tradition); Masoretic Text me; / I will exchange their glory
  3. Hosea 4:15 Beth Aven means house of wickedness (a derogatory name for Bethel, which means house of God).