Add parallel Print Page Options

Yehova Ayimba Mlandu Israeli

Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova,
    chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu
    amene mumakhala mʼdzikoli:
“Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi
    mulibe kulabadira za Mulungu.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha.
    Kuba ndi kuchita chigololo;
machimo achita kunyanya
    ndipo akungokhalira kuphana.
Chifukwa chake dziko likulira
    ndipo onse amene amakhalamo akuvutika;
zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga
    ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.

“Koma wina asapeze mnzake chifukwa,
    wina aliyense asayimbe mlandu mnzake,
pakuti anthu ako ali ngati anthu
    amene amayimba mlandu wansembe.
Mumapunthwa usana ndi usiku
    ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi.
Choncho ndidzawononga amayi anu.
    Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa.

“Pakuti mwakana kudziwa,
    Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga;
chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu,
    Inenso ndidzayiwala ana anu.
Ansembe ankati akachuluka
    iwo ankandichimwiranso kwambiri;
    iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga
    ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe.
    Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo,
    ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.

10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta;
    azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana,
chifukwa anasiya Yehova
kuti adzipereke 11     ku zachiwerewere,
ku vinyo wakale ndi watsopano,
    zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 za anthu anga.
Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo
    ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha.
Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa;
    iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri
    ndi kufukiza lubani pa zitunda,
pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi,
    pamene pali mthunzi wabwino.
Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere
    ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.

14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi
    pamene iwo adzachita zachiwerewere,
kapena akazi a ana anu
    pamene adzachita zigololo.
Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere,
    ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako.
    Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!

15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli,
    Yuda asapezeke ndi mlandu wotere.

“Usapite ku Giligala.
    Usapite ku Beti-Aveni.
    Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 Aisraeli ndi nkhutukumve,
    ngosamva ngati ana angʼombe.
Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji
    ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Efereimu waphathana ndi mafano;
    mulekeni!
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha,
    amapitiriza kuchita zachiwerewere;
    atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu
    ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

Hear the word of the Lord, ye children of Israel: for the Lord hath a controversy with the inhabitants of the land, because there is no truth, nor mercy, nor knowledge of God in the land.

By swearing, and lying, and killing, and stealing, and committing adultery, they break out, and blood toucheth blood.

Therefore shall the land mourn, and every one that dwelleth therein shall languish, with the beasts of the field, and with the fowls of heaven; yea, the fishes of the sea also shall be taken away.

Yet let no man strive, nor reprove another: for thy people are as they that strive with the priest.

Therefore shalt thou fall in the day, and the prophet also shall fall with thee in the night, and I will destroy thy mother.

My people are destroyed for lack of knowledge: because thou hast rejected knowledge, I will also reject thee, that thou shalt be no priest to me: seeing thou hast forgotten the law of thy God, I will also forget thy children.

As they were increased, so they sinned against me: therefore will I change their glory into shame.

They eat up the sin of my people, and they set their heart on their iniquity.

And there shall be, like people, like priest: and I will punish them for their ways, and reward them their doings.

10 For they shall eat, and not have enough: they shall commit whoredom, and shall not increase: because they have left off to take heed to the Lord.

11 Whoredom and wine and new wine take away the heart.

12 My people ask counsel at their stocks, and their staff declareth unto them: for the spirit of whoredoms hath caused them to err, and they have gone a whoring from under their God.

13 They sacrifice upon the tops of the mountains, and burn incense upon the hills, under oaks and poplars and elms, because the shadow thereof is good: therefore your daughters shall commit whoredom, and your spouses shall commit adultery.

14 I will not punish your daughters when they commit whoredom, nor your spouses when they commit adultery: for themselves are separated with whores, and they sacrifice with harlots: therefore the people that doth not understand shall fall.

15 Though thou, Israel, play the harlot, yet let not Judah offend; and come not ye unto Gilgal, neither go ye up to Bethaven, nor swear, The Lord liveth.

16 For Israel slideth back as a backsliding heifer: now the Lord will feed them as a lamb in a large place.

17 Ephraim is joined to idols: let him alone.

18 Their drink is sour: they have committed whoredom continually: her rulers with shame do love, Give ye.

19 The wind hath bound her up in her wings, and they shall be ashamed because of their sacrifices.