Hoseya 3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Hoseya Ayanjana ndi Mkazi Wake
3 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele. 3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano. 5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
Hosea 3
New International Version
Hosea’s Reconciliation With His Wife
3 The Lord said to me, “Go, show your love to your wife again, though she is loved by another man and is an adulteress.(A) Love her as the Lord loves the Israelites, though they turn to other gods and love the sacred raisin cakes.(B)”
2 So I bought her for fifteen shekels[a] of silver and about a homer and a lethek[b] of barley. 3 Then I told her, “You are to live with me many days; you must not be a prostitute or be intimate with any man, and I will behave the same way toward you.”
4 For the Israelites will live many days without king or prince,(C) without sacrifice(D) or sacred stones,(E) without ephod(F) or household gods.(G) 5 Afterward the Israelites will return and seek(H) the Lord their God and David their king.(I) They will come trembling(J) to the Lord and to his blessings in the last days.(K)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.