Add parallel Print Page Options

“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’ ”

Kulangidwa ndi Kubwezeretsedwa kwa Israeli

“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo,
    pakuti si mkazi wanga,
    ndipo ine sindine mwamuna wake.
Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake,
    ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Akapanda kutero ndidzamuvula,
    ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa;
ndidzamuwumitsa ngati chipululu,
    adzakhala ngati dziko lopanda madzi,
    ndi kumupha ndi ludzu.
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake,
    chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere
    ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi.
Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga,
    zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi,
    ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga;
    ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza;
    adzazifunafuna koma sadzazipeza.
Pamenepo iye adzati,
    ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja,
    pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
Iye sanazindikire kuti ndine amene
    ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta.
Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide,
    zimene ankapangira mafano a Baala.

“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola,
    ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa.
Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa,
    zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake
    pamaso pa zibwenzi zake;
    palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse:
    zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano,
    za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu,
    imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake.
Ndidzayisandutsa chithukuluzi,
    ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku
    amene anafukiza lubani kwa Abaala;
anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali
    ndipo anathamangira zibwenzi zake,
    koma Ine anandiyiwala,”
            akutero Yehova.

14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo;
    ndidzapita naye ku chipululu
    ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa,
    ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo.
Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake,
    monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.

16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti,
    “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’
    sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake;
    sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano
    ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga
    ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga.
Ndidzachotsa mʼdzikomo uta,
    lupanga ndi zida zonse zankhondo,
    kuti onse apumule mwamtendere.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya;
    ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro,
    mwachikondi ndi mwachifundo.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika
    ndipo udzadziwa Yehova.

21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,”
    akutero Yehova.
“Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo
    ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu,
    vinyo ndi mafuta,
    ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga:
    ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’
Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’
    ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’ ”

[a]“Say of your brothers, ‘My people,’ and of your sisters, ‘My loved one.’(A)

Israel Punished and Restored

“Rebuke your mother,(B) rebuke her,
    for she is not my wife,
    and I am not her husband.
Let her remove the adulterous(C) look from her face
    and the unfaithfulness from between her breasts.
Otherwise I will strip(D) her naked
    and make her as bare as on the day she was born;(E)
I will make her like a desert,(F)
    turn her into a parched land,
    and slay her with thirst.
I will not show my love to her children,(G)
    because they are the children of adultery.(H)
Their mother has been unfaithful
    and has conceived them in disgrace.
She said, ‘I will go after my lovers,(I)
    who give me my food and my water,
    my wool and my linen, my olive oil and my drink.’(J)
Therefore I will block her path with thornbushes;
    I will wall her in so that she cannot find her way.(K)
She will chase after her lovers but not catch them;
    she will look for them but not find them.(L)
Then she will say,
    ‘I will go back to my husband(M) as at first,(N)
    for then I was better off(O) than now.’
She has not acknowledged(P) that I was the one
    who gave her the grain, the new wine and oil,(Q)
who lavished on her the silver and gold(R)
    which they used for Baal.(S)

“Therefore I will take away my grain(T) when it ripens,
    and my new wine(U) when it is ready.
I will take back my wool and my linen,
    intended to cover her naked body.
10 So now I will expose(V) her lewdness
    before the eyes of her lovers;(W)
    no one will take her out of my hands.(X)
11 I will stop(Y) all her celebrations:(Z)
    her yearly festivals, her New Moons,
    her Sabbath days—all her appointed festivals.(AA)
12 I will ruin her vines(AB) and her fig trees,(AC)
    which she said were her pay from her lovers;(AD)
I will make them a thicket,(AE)
    and wild animals will devour them.(AF)
13 I will punish her for the days
    she burned incense(AG) to the Baals;(AH)
she decked herself with rings and jewelry,(AI)
    and went after her lovers,(AJ)
    but me she forgot,(AK)
declares the Lord.(AL)

14 “Therefore I am now going to allure her;
    I will lead her into the wilderness(AM)
    and speak tenderly to her.
15 There I will give her back her vineyards,
    and will make the Valley of Achor[b](AN) a door of hope.
There she will respond[c](AO) as in the days of her youth,(AP)
    as in the day she came up out of Egypt.(AQ)

16 “In that day,” declares the Lord,
    “you will call me ‘my husband’;(AR)
    you will no longer call me ‘my master.[d]
17 I will remove the names of the Baals from her lips;(AS)
    no longer will their names be invoked.(AT)
18 In that day I will make a covenant for them
    with the beasts of the field, the birds in the sky
    and the creatures that move along the ground.(AU)
Bow and sword and battle
    I will abolish(AV) from the land,
    so that all may lie down in safety.(AW)
19 I will betroth(AX) you to me forever;
    I will betroth you in[e] righteousness and justice,(AY)
    in[f] love and compassion.(AZ)
20 I will betroth you in[g] faithfulness,
    and you will acknowledge(BA) the Lord.(BB)

21 “In that day I will respond,”
    declares the Lord
“I will respond(BC) to the skies,
    and they will respond to the earth;
22 and the earth will respond to the grain,
    the new wine and the olive oil,(BD)
    and they will respond to Jezreel.[h](BE)
23 I will plant(BF) her for myself in the land;
    I will show my love to the one I called ‘Not my loved one.[i](BG)
I will say to those called ‘Not my people,[j]’ ‘You are my people’;(BH)
    and they will say, ‘You are my God.(BI)’”

Footnotes

  1. Hosea 2:1 In Hebrew texts 2:1-23 is numbered 2:3-25.
  2. Hosea 2:15 Achor means trouble.
  3. Hosea 2:15 Or sing
  4. Hosea 2:16 Hebrew baal
  5. Hosea 2:19 Or with
  6. Hosea 2:19 Or with
  7. Hosea 2:20 Or with
  8. Hosea 2:22 Jezreel means God plants.
  9. Hosea 2:23 Hebrew Lo-Ruhamah (see 1:6)
  10. Hosea 2:23 Hebrew Lo-Ammi (see 1:9)