Add parallel Print Page Options

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

13 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;
    anali wolemekezeka mu Israeli.
    Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;
    akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,
zifanizo zopangidwa mwaluso,
    zonsezo zopangidwa ndi amisiri.
Amanena za anthu awa kuti,
    “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe
    ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,
    ngati mame amene amakamuka msanga,
    ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,
    ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.

Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    amene ndinakutulutsani mu Igupto.
Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,
    palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
Ndinakusamalira mʼchipululu,
    mʼdziko lotentha kwambiri.
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;
    iwo atakhuta anayamba kunyada;
    ndipo anandiyiwala Ine.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango,
    ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,
    ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.
Ndidzawapwepweta ngati mkango;
    chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.

“Iwe Israeli, wawonongedwa,
    chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?
    Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,
amene iwe unanena za iwo kuti,
    ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,
    ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,
    machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,
    koma iye ndi mwana wopanda nzeru,
pamene nthawi yake yobadwa yafika
    iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.

14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;
    ndidzawawombola ku imfa.
Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?
    Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?

“Sindidzachitanso chifundo,
15     ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,
mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,
    ikuwomba kuchokera ku chipululu.
Kasupe wake adzaphwa
    ndipo chitsime chake chidzawuma.
Chuma chake chonse chamtengowapatali
    chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,
    chifukwa anawukira Mulungu wawo.
Adzaphedwa ndi lupanga;
    ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,
    akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

The Lord’s Anger Against Israel

13 When Ephraim spoke, people trembled;(A)
    he was exalted(B) in Israel.
    But he became guilty of Baal worship(C) and died.
Now they sin more and more;
    they make(D) idols for themselves from their silver,(E)
cleverly fashioned images,
    all of them the work of craftsmen.(F)
It is said of these people,
    “They offer human sacrifices!
    They kiss[a](G) calf-idols!(H)
Therefore they will be like the morning mist,
    like the early dew that disappears,(I)
    like chaff(J) swirling from a threshing floor,(K)
    like smoke(L) escaping through a window.

“But I have been the Lord your God
    ever since you came out of Egypt.(M)
You shall acknowledge(N) no God but me,(O)
    no Savior(P) except me.
I cared for you in the wilderness,(Q)
    in the land of burning heat.
When I fed them, they were satisfied;
    when they were satisfied, they became proud;(R)
    then they forgot(S) me.(T)
So I will be like a lion(U) to them,
    like a leopard I will lurk by the path.
Like a bear robbed of her cubs,(V)
    I will attack them and rip them open;
like a lion(W) I will devour them—
    a wild animal will tear them apart.(X)

“You are destroyed, Israel,
    because you are against me,(Y) against your helper.(Z)
10 Where is your king,(AA) that he may save you?
    Where are your rulers in all your towns,
of whom you said,
    ‘Give me a king and princes’?(AB)
11 So in my anger I gave you a king,(AC)
    and in my wrath I took him away.(AD)
12 The guilt of Ephraim is stored up,
    his sins are kept on record.(AE)
13 Pains as of a woman in childbirth(AF) come to him,
    but he is a child without wisdom;
when the time(AG) arrives,
    he doesn’t have the sense to come out of the womb.(AH)

14 “I will deliver this people from the power of the grave;(AI)
    I will redeem them from death.(AJ)
Where, O death, are your plagues?
    Where, O grave, is your destruction?(AK)

“I will have no compassion,
15     even though he thrives(AL) among his brothers.
An east wind(AM) from the Lord will come,
    blowing in from the desert;
his spring will fail
    and his well dry up.(AN)
His storehouse will be plundered(AO)
    of all its treasures.
16 The people of Samaria(AP) must bear their guilt,(AQ)
    because they have rebelled(AR) against their God.
They will fall by the sword;(AS)
    their little ones will be dashed(AT) to the ground,
    their pregnant women(AU) ripped open.”[b]

Footnotes

  1. Hosea 13:2 Or “Men who sacrifice / kiss
  2. Hosea 13:16 In Hebrew texts this verse (13:16) is numbered 14:1.