Add parallel Print Page Options

10 Israeli anali mpesa wotambalala;
    anabereka zipatso zambiri.
Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka,
    anawonjezera kumanga maguwa ansembe.
Pamene dziko lake linkatukuka,
    anakongoletsa miyala yake yopatulika.
Mtima wawo ndi wonyenga
    ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo.
Yehova adzagumula maguwa awo ansembe
    ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.

Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu
    chifukwa sitinaope Yehova.
Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu,
    kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
Mafumu amalonjeza zambiri,
    amalumbira zabodza
    pochita mapangano.
Kotero maweruzo amaphuka
    ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha
    chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni.
Anthu ake adzalirira fanolo,
    chimodzimodzinso ansembe ake adamawo,
amene anakondwera ndi kukongola kwake,
    chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya
    ngati mphatso kwa mfumu yayikulu.
Efereimu adzachititsidwa manyazi
    chifukwa cha mafano ake amitengo.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali
    ngati kanthambi koyenda pa madzi.
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa.
    Ili ndiye tchimo la Israeli.
Minga ndi mitungwi zidzamera
    ndi kuphimba maguwa awo ansembe.
Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!”
    ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”

“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya,
    ndipo wakhala uli pomwepo.
Kodi nkhondo sinagonjetse anthu
    ochita zoyipa ku Gibeya?
10 Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo;
    mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo,
    kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa
    amene amakonda kupuntha tirigu,
choncho Ine ndidzayika goli
    mʼkhosi lake lokongolalo.
Ndidzasenzetsa Efereimu goli,
    Yuda ayenera kulima,
    ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Mufese nokha chilungamo
    ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika.
Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo;
    pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova,
mpaka Iye atabwera
    kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 Koma inu munadzala zolakwa,
    mwakolola zoyipa;
    mwadya chipatso cha chinyengo.
Chifukwa mumadalira mphamvu zanu
    ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga
    kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka,
monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo;
    pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli
    chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu.
Tsiku limeneli likadzafika,
    mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

10 Israel was a spreading vine;(A)
    he brought forth fruit for himself.
As his fruit increased,
    he built more altars;(B)
as his land prospered,(C)
    he adorned his sacred stones.(D)
Their heart is deceitful,(E)
    and now they must bear their guilt.(F)
The Lord will demolish their altars(G)
    and destroy their sacred stones.(H)

Then they will say, “We have no king
    because we did not revere the Lord.
But even if we had a king,
    what could he do for us?”
They make many promises,
    take false oaths(I)
    and make agreements;(J)
therefore lawsuits spring up
    like poisonous weeds(K) in a plowed field.
The people who live in Samaria fear
    for the calf-idol(L) of Beth Aven.[a](M)
Its people will mourn over it,
    and so will its idolatrous priests,(N)
those who had rejoiced over its splendor,
    because it is taken from them into exile.(O)
It will be carried to Assyria(P)
    as tribute(Q) for the great king.(R)
Ephraim will be disgraced;(S)
    Israel will be ashamed(T) of its foreign alliances.
Samaria’s king will be destroyed,(U)
    swept away like a twig on the surface of the waters.
The high places(V) of wickedness[b](W) will be destroyed—
    it is the sin of Israel.
Thorns(X) and thistles will grow up
    and cover their altars.(Y)
Then they will say to the mountains, “Cover us!”(Z)
    and to the hills, “Fall on us!”(AA)

“Since the days of Gibeah,(AB) you have sinned,(AC) Israel,
    and there you have remained.[c]
Will not war again overtake
    the evildoers in Gibeah?
10 When I please, I will punish(AD) them;
    nations will be gathered against them
    to put them in bonds for their double sin.
11 Ephraim is a trained heifer
    that loves to thresh;
so I will put a yoke(AE)
    on her fair neck.
I will drive Ephraim,
    Judah must plow,
    and Jacob must break up the ground.
12 Sow(AF) righteousness(AG) for yourselves,
    reap the fruit of unfailing love,
and break up your unplowed ground;(AH)
    for it is time to seek(AI) the Lord,
until he comes
    and showers his righteousness(AJ) on you.
13 But you have planted wickedness,
    you have reaped evil,(AK)
    you have eaten the fruit of deception.(AL)
Because you have depended on your own strength
    and on your many warriors,(AM)
14 the roar of battle will rise against your people,
    so that all your fortresses will be devastated(AN)
as Shalman(AO) devastated Beth Arbel on the day of battle,
    when mothers were dashed to the ground with their children.(AP)
15 So will it happen to you, Bethel,
    because your wickedness is great.
When that day dawns,
    the king of Israel will be completely destroyed.(AQ)

Footnotes

  1. Hosea 10:5 Beth Aven means house of wickedness (a derogatory name for Bethel, which means house of God).
  2. Hosea 10:8 Hebrew aven, a reference to Beth Aven (a derogatory name for Bethel); see verse 5.
  3. Hosea 10:9 Or there a stand was taken