Add parallel Print Page Options

Pemphero la Habakuku

Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;
    Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.
Muzichitenso masiku athu ano,
    masiku athu ano zidziwike;
    mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,
    Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.
            Sela
Ulemerero wake unaphimba mlengalenga
    ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;
    kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,
    mʼmene anabisamo mphamvu zake.
Patsogolo pake pankagwa mliri;
    nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;
    anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.
Mapiri okhazikika anagumuka
    ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.
    Njira zake ndi zachikhalire.
Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,
    mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?
    Kodi munakalipira timitsinje?
Kodi munapsera mtima nyanja
    pamene munakwera pa akavalo anu
    ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Munasolola uta wanu mʼchimake,
    munayitanitsa mivi yambiri.
            Sela
Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
10     mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.
Madzi amphamvu anasefukira;
    nyanja yozama inakokoma
    ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,
    pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,
    pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,
    ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu,
    kukapulumutsa wodzozedwa wanu.
Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,
    munawononga anthu ake onse.
            Sela
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake
    pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,
ankasangalala ngati kuti akudzawononga
    osauka amene akubisala.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,
    kuvundula madzi amphamvu.

16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,
    milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;
mafupa anga anaguluka,
    ndipo mawondo anga anawombana.
Komabe ndikuyembekezera mofatsa,
    tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,
    ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.
Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,
    ndipo mʼminda musatuluke kanthu.
Ngakhale nkhosa
    ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,
    ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;
    amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,
    amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

Habakkuk’s Prayer

A prayer of Habakkuk the prophet. On shigionoth.[a](A)

Lord, I have heard(B) of your fame;
    I stand in awe(C) of your deeds, Lord.(D)
Repeat(E) them in our day,
    in our time make them known;
    in wrath remember mercy.(F)

God came from Teman,(G)
    the Holy One(H) from Mount Paran.[b](I)
His glory covered the heavens(J)
    and his praise filled the earth.(K)
His splendor was like the sunrise;(L)
    rays flashed from his hand,
    where his power(M) was hidden.
Plague(N) went before him;
    pestilence followed his steps.
He stood, and shook the earth;
    he looked, and made the nations tremble.
The ancient mountains crumbled(O)
    and the age-old hills(P) collapsed(Q)
    but he marches on forever.(R)
I saw the tents of Cushan in distress,
    the dwellings of Midian(S) in anguish.(T)

Were you angry with the rivers,(U) Lord?
    Was your wrath against the streams?
Did you rage against the sea(V)
    when you rode your horses
    and your chariots to victory?(W)
You uncovered your bow,
    you called for many arrows.(X)
You split the earth with rivers;
10     the mountains saw you and writhed.(Y)
Torrents of water swept by;
    the deep roared(Z)
    and lifted its waves(AA) on high.

11 Sun and moon stood still(AB) in the heavens
    at the glint of your flying arrows,(AC)
    at the lightning(AD) of your flashing spear.
12 In wrath you strode through the earth
    and in anger you threshed(AE) the nations.
13 You came out(AF) to deliver(AG) your people,
    to save your anointed(AH) one.
You crushed(AI) the leader of the land of wickedness,
    you stripped him from head to foot.
14 With his own spear you pierced his head
    when his warriors stormed out to scatter us,(AJ)
gloating as though about to devour
    the wretched(AK) who were in hiding.
15 You trampled the sea(AL) with your horses,
    churning the great waters.(AM)

16 I heard and my heart pounded,
    my lips quivered at the sound;
decay crept into my bones,
    and my legs trembled.(AN)
Yet I will wait patiently(AO) for the day of calamity
    to come on the nation invading us.
17 Though the fig tree does not bud
    and there are no grapes on the vines,
though the olive crop fails
    and the fields produce no food,(AP)
though there are no sheep in the pen
    and no cattle in the stalls,(AQ)
18 yet I will rejoice in the Lord,(AR)
    I will be joyful in God my Savior.(AS)

19 The Sovereign Lord is my strength;(AT)
    he makes my feet like the feet of a deer,
    he enables me to tread on the heights.(AU)

For the director of music. On my stringed instruments.

Footnotes

  1. Habakkuk 3:1 Probably a literary or musical term
  2. Habakkuk 3:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the middle of verse 9 and at the end of verse 13.