Add parallel Print Page Options

Ndidzakhala pa malo anga aulonda,
    ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo;
ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze,
    ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.

Yankho la Yehova

Tsono Yehova anandiyankha, nati:

“Lemba masomphenyawa
    ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale
    kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake;
    masomphenyawa akunena zamʼtsogolo
    ndipo sizidzalephera kuchitika.
Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere;
    zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.

“Taona, mdani wadzitukumula;
    zokhumba zake sizowongoka,
    koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo;
    ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika.
Pakuti ngodzikonda ngati manda,
    ngosakhutitsidwa ngati imfa,
wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu
    ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse.

“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti,

“Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake
    ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda!
    Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi?
    Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha?
    Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu,
    mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo.
Pakuti wakhetsa magazi a anthu;
    wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo,
    kukweza malo ake okhalapo,
    kuthawa mavuto!
10 Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu,
    kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
11 Mwala pa khoma udzafuwula,
    ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.

12 “Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi
    ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
13 Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize
    kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto,
    ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova,
    monga momwe madzi amadzazira nyanja.

15 “Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa,
    kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera,
    kuti aone umaliseche wawo.
16 Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero.
    Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere!
Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe,
    ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
17 Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni,
    ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga.
Pakuti wakhetsa magazi a anthu;
    wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

18 “Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu,
    kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza?
Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake;
    amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
19 Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’
    Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’
Kodi zimenezi zingathe kulangiza?
    Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva;
    mʼkati mwake mulibe mpweya.
20 Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika;
    dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”