Add parallel Print Page Options

Kuyipa kwa Mtundu wa Anthu

Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi, ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha. Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”

Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.

Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha, Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima. Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.” Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.

Nowa ndi Chigumula

Mbiri ya Nowa inali yotere:

Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu. 10 Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.

11 Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu. 12 Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi. 13 Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko. 14 Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja. 15 Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake. 16 Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba. 17 Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa. 18 Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho. 19 Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe. 20 Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo. 21 Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”

22 Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.

Wickedness in the World

When human beings began to increase in number on the earth(A) and daughters were born to them, the sons of God(B) saw that the daughters(C) of humans were beautiful,(D) and they married(E) any of them they chose. Then the Lord said, “My Spirit(F) will not contend with[a] humans forever,(G) for they are mortal[b];(H) their days will be a hundred and twenty years.”

The Nephilim(I) were on the earth in those days—and also afterward—when the sons of God went to the daughters of humans(J) and had children by them. They were the heroes of old, men of renown.(K)

The Lord saw how great the wickedness of the human race had become on the earth,(L) and that every inclination of the thoughts of the human heart was only evil all the time.(M) The Lord regretted(N) that he had made human beings on the earth, and his heart was deeply troubled. So the Lord said, “I will wipe from the face of the earth(O) the human race I have created—and with them the animals, the birds and the creatures that move along the ground—for I regret that I have made them.(P) But Noah(Q) found favor in the eyes of the Lord.(R)

Noah and the Flood

This is the account(S) of Noah and his family.

Noah was a righteous man, blameless(T) among the people of his time,(U) and he walked faithfully with God.(V) 10 Noah had three sons: Shem,(W) Ham and Japheth.(X)

11 Now the earth was corrupt(Y) in God’s sight and was full of violence.(Z) 12 God saw how corrupt(AA) the earth had become, for all the people on earth had corrupted their ways.(AB) 13 So God said to Noah, “I am going to put an end to all people, for the earth is filled with violence because of them. I am surely going to destroy(AC) both them and the earth.(AD) 14 So make yourself an ark of cypress[c] wood;(AE) make rooms in it and coat it with pitch(AF) inside and out. 15 This is how you are to build it: The ark is to be three hundred cubits long, fifty cubits wide and thirty cubits high.[d] 16 Make a roof for it, leaving below the roof an opening one cubit[e] high all around.[f] Put a door in the side of the ark and make lower, middle and upper decks. 17 I am going to bring floodwaters(AG) on the earth to destroy all life under the heavens, every creature that has the breath of life in it. Everything on earth will perish.(AH) 18 But I will establish my covenant with you,(AI) and you will enter the ark(AJ)—you and your sons and your wife and your sons’ wives with you. 19 You are to bring into the ark two of all living creatures, male and female, to keep them alive with you.(AK) 20 Two(AL) of every kind of bird, of every kind of animal and of every kind(AM) of creature that moves along the ground will come to you to be kept alive.(AN) 21 You are to take every kind of food that is to be eaten and store it away as food for you and for them.”

22 Noah did everything just as God commanded him.(AO)

Footnotes

  1. Genesis 6:3 Or My spirit will not remain in
  2. Genesis 6:3 Or corrupt
  3. Genesis 6:14 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  4. Genesis 6:15 That is, about 450 feet long, 75 feet wide and 45 feet high or about 135 meters long, 23 meters wide and 14 meters high
  5. Genesis 6:16 That is, about 18 inches or about 45 centimeters
  6. Genesis 6:16 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.