Add parallel Print Page Options

Yosefe Amasulira Maloto a Amʼndende Anzake

40 Patapita nthawi, woperekera zakumwa ndi wopanga buledi a ku nyumba kwa mfumu ya ku Igupto analakwira mbuye wawoyo. Farao anapsa mtima ndi akuluakulu awiriwa, ndipo anakawatsekera mʼndende, nakawayika mʼmanja mwa mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa mfumu kuja, mʼndende momwe Yosefe ankasungidwamo. Mkulu wa alonda aja anawapereka mʼmanja mwa Yosefe, ndipo iye anawasamalira.

Iwo anakhala mʼndendemo kwa kanthawi. Usiku wina, aliyense wa anthu awiriwa, wopereka zakumwa pamodzi ndi wopanga buledi wa ku nyumba ya mfumu ya ku Igupto aja, amene ankasungidwa mʼndende, analota maloto. Malotowo anali ndi tanthauzo lake.

Mmawa wake, Yosefe atabwera, anaona kuti nkhope zawo zinali zakugwa. Choncho anafunsa akuluakulu a kwa Farao amene anali naye mʼndende muja kuti, “Bwanji nkhope zanu zili zachisoni lero?”

Iwo anayankha, “Tonse awiri talota maloto, koma palibe wotitanthauzira malotowo.”

Pamenepo Yosefe anawawuza kuti, “Ndi Mulungu yekha amene amapereka matanthauzo a maloto. Uzeni ine maloto anu.”

Choncho mkulu wa operekera zakumwa uja anamuwuza Yosefe maloto ake. Anati, “Mʼmaloto anga ndinaona mtengo wa mpesa, 10 unali ndi nthambi zitatu. Mpesawo utangophukira, unachita maluwa ndipo maphava ake anabereka mphesa zakupsa. 11 Chikho cha Farao chinali mʼmanja mwanga, ndipo ndinatenga mphesa, kupsinyira mu chikho cha Farao ndi kuchipereka mʼmanja mwake.”

12 Yosefe anati kwa iye, “Tanthauzo lake ndi ili: Nthambi zitatuzo ndi masiku atatu. 13 Pakangopita masiku atatu, Farao adzakutulutsa muno. Udzaperekera zakumwa kwa Farao monga momwe umachitira poyamba. 14 Koma zako zikakuyendera bwino, udzandikumbukire ndi kundikomera mtima. Chonde ukandipepesere kwa Farao kuti anditulutse muno. 15 Popezatu ine anangochita mondiba kubwera nane kuno kuchokera ku dziko la Ahebri, ndipo ngakhale kunoko, ine sindinalakwe kali konse kuti ndizipezeka mʼdzenje muno.”

16 Mkulu wa opanga buledi ataona kuti Yosefe wapereka tanthauzo labwino, anati kwa Yosefe, “Inenso ndinalota nditasenza nsengwa zitatu za buledi. 17 Mu nsengwa yapamwamba munali zakudya zamitundumitundu za Farao, koma mbalame zimadya zakudyazo.”

18 Yosefe anati, “Tanthauzo lake ndi ili: nsengwa zitatuzo ndi masiku atatu. 19 Pakangotha masiku atatu Farao adzakutulutsa muno koma adzakupachika. Ndipo mbalame zidzadya mnofu wako.”

20 Tsono tsiku lachitatulo linali lokumbukira kubadwa kwa Farao, ndipo anawakonzera phwando akuluakulu ake onse. Anatulutsa mʼndende mkulu wa operekera zakumwa ndi mkulu wa ophika buledi, ndipo anawayimiritsa pamaso pa nduna zake. 21 Tsono Farao anamubwezera mkulu wa operekera zakumwa uja pa udindo wake, kotero kuti anayamba kuperekeranso zakumwa kwa Farao, 22 koma mkulu wa ophika buledi anamupachika, mofanana ndi mmene Yosefe anatanthauzira maloto.

23 Koma mkulu wa operekera zakumwa uja sanamukumbukire Yosefe ndipo anamuyiwaliratu.

The Cupbearer and the Baker

40 Some time later, the cupbearer(A) and the baker(B) of the king of Egypt offended their master, the king of Egypt. Pharaoh was angry(C) with his two officials,(D) the chief cupbearer and the chief baker, and put them in custody in the house of the captain of the guard,(E) in the same prison where Joseph was confined. The captain of the guard(F) assigned them to Joseph,(G) and he attended them.

After they had been in custody(H) for some time, each of the two men—the cupbearer and the baker of the king of Egypt, who were being held in prison—had a dream(I) the same night, and each dream had a meaning of its own.(J)

When Joseph came to them the next morning, he saw that they were dejected. So he asked Pharaoh’s officials who were in custody(K) with him in his master’s house, “Why do you look so sad today?”(L)

“We both had dreams,” they answered, “but there is no one to interpret them.”(M)

Then Joseph said to them, “Do not interpretations belong to God?(N) Tell me your dreams.”

So the chief cupbearer(O) told Joseph his dream. He said to him, “In my dream I saw a vine in front of me, 10 and on the vine were three branches. As soon as it budded, it blossomed,(P) and its clusters ripened into grapes. 11 Pharaoh’s cup was in my hand, and I took the grapes, squeezed them into Pharaoh’s cup and put the cup in his hand.”

12 “This is what it means,(Q)” Joseph said to him. “The three branches are three days.(R) 13 Within three days(S) Pharaoh will lift up your head(T) and restore you to your position, and you will put Pharaoh’s cup in his hand, just as you used to do when you were his cupbearer.(U) 14 But when all goes well with you, remember me(V) and show me kindness;(W) mention me to Pharaoh(X) and get me out of this prison. 15 I was forcibly carried off from the land of the Hebrews,(Y) and even here I have done nothing to deserve being put in a dungeon.”(Z)

16 When the chief baker(AA) saw that Joseph had given a favorable interpretation,(AB) he said to Joseph, “I too had a dream: On my head were three baskets(AC) of bread.[a] 17 In the top basket were all kinds of baked goods for Pharaoh, but the birds were eating them out of the basket on my head.”

18 “This is what it means,” Joseph said. “The three baskets are three days.(AD) 19 Within three days(AE) Pharaoh will lift off your head(AF) and impale your body on a pole.(AG) And the birds will eat away your flesh.”(AH)

20 Now the third day(AI) was Pharaoh’s birthday,(AJ) and he gave a feast for all his officials.(AK) He lifted up the heads of the chief cupbearer and the chief baker(AL) in the presence of his officials: 21 He restored the chief cupbearer(AM) to his position,(AN) so that he once again put the cup into Pharaoh’s hand(AO) 22 but he impaled the chief baker,(AP) just as Joseph had said to them in his interpretation.(AQ)

23 The chief cupbearer, however, did not remember Joseph; he forgot him.(AR)

Footnotes

  1. Genesis 40:16 Or three wicker baskets