Add parallel Print Page Options

Kuchimwa kwa Munthu

Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’ ”

Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu, koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’ ”

“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo. “Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”

Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso. Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.

Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo. Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”

10 Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”

11 Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”

12 Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”

13 Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?”

Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”

14 Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi,

“Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse
    ndi nyama zakuthengo zonse.
Udzayenda chafufumimba
    ndipo udzadya fumbi
    masiku onse a moyo wako.
15 Ndipo ndidzayika chidani
    pakati pa iwe ndi mkaziyo,
    pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake;
Iye adzaphwanya mutu wako
    ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”

16 Kwa mkaziyo Iye anati,

“Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati;
    ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana.
Udzakhumba mwamuna wako,
    ndipo adzakulamulira.”

17 Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’

“Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe,
    movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo
    masiku onse a moyo wako.
18 Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula
    ndipo udzadya zomera zakuthengo.
19 Kuti upeze chakudya udzayenera
    kukhetsa thukuta,
mpaka utabwerera ku nthaka
    pakuti unachokera kumeneko;
pakuti ndiwe fumbi
    ku fumbi komweko udzabwerera.”

20 Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.

21 Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka. 22 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.” 23 Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera. 24 Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

The Fall

Now the serpent(A) was more crafty than any of the wild animals the Lord God had made. He said to the woman, “Did God really say, ‘You must not eat from any tree in the garden’?(B)

The woman said to the serpent, “We may eat fruit from the trees in the garden,(C) but God did say, ‘You must not eat fruit from the tree that is in the middle of the garden, and you must not touch it, or you will die.’”(D)

“You will not certainly die,” the serpent said to the woman.(E) “For God knows that when you eat from it your eyes will be opened, and you will be like God,(F) knowing good and evil.”

When the woman saw that the fruit of the tree was good for food and pleasing to the eye, and also desirable(G) for gaining wisdom, she took some and ate it. She also gave some to her husband,(H) who was with her, and he ate it.(I) Then the eyes of both of them were opened, and they realized they were naked;(J) so they sewed fig leaves together and made coverings for themselves.(K)

Then the man and his wife heard the sound of the Lord God as he was walking(L) in the garden in the cool of the day, and they hid(M) from the Lord God among the trees of the garden. But the Lord God called to the man, “Where are you?”(N)

10 He answered, “I heard you in the garden, and I was afraid(O) because I was naked;(P) so I hid.”

11 And he said, “Who told you that you were naked?(Q) Have you eaten from the tree that I commanded you not to eat from?(R)

12 The man said, “The woman you put here with me(S)—she gave me some fruit from the tree, and I ate it.”

13 Then the Lord God said to the woman, “What is this you have done?”

The woman said, “The serpent deceived me,(T) and I ate.”

14 So the Lord God said to the serpent, “Because you have done this,

“Cursed(U) are you above all livestock
    and all wild animals!
You will crawl on your belly
    and you will eat dust(V)
    all the days of your life.
15 And I will put enmity
    between you and the woman,
    and between your offspring[a](W) and hers;(X)
he will crush[b] your head,(Y)
    and you will strike his heel.”

16 To the woman he said,

“I will make your pains in childbearing very severe;
    with painful labor you will give birth to children.(Z)
Your desire will be for your husband,
    and he will rule over you.(AA)

17 To Adam he said, “Because you listened to your wife and ate fruit from the tree about which I commanded you, ‘You must not eat from it,’(AB)

“Cursed(AC) is the ground(AD) because of you;
    through painful toil(AE) you will eat food from it
    all the days of your life.(AF)
18 It will produce thorns and thistles(AG) for you,
    and you will eat the plants of the field.(AH)
19 By the sweat of your brow(AI)
    you will eat your food(AJ)
until you return to the ground,
    since from it you were taken;
for dust you are
    and to dust you will return.”(AK)

20 Adam[c] named his wife Eve,[d](AL) because she would become the mother of all the living.

21 The Lord God made garments of skin for Adam and his wife and clothed them.(AM) 22 And the Lord God said, “The man has now become like one of us,(AN) knowing good and evil. He must not be allowed to reach out his hand and take also from the tree of life(AO) and eat, and live forever.” 23 So the Lord God banished him from the Garden of Eden(AP) to work the ground(AQ) from which he had been taken. 24 After he drove the man out, he placed on the east side[e] of the Garden of Eden(AR) cherubim(AS) and a flaming sword(AT) flashing back and forth to guard the way to the tree of life.(AU)

Footnotes

  1. Genesis 3:15 Or seed
  2. Genesis 3:15 Or strike
  3. Genesis 3:20 Or The man
  4. Genesis 3:20 Eve probably means living.
  5. Genesis 3:24 Or placed in front