Add parallel Print Page Options

Yakobo Afika ku Padanaramu

29 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa. Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu. Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.

Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?”

Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”

Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?”

Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”

Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?”

Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”

Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”

Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”

Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo. 10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo. 11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza. 12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.

13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika. 14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.”

Yakobo Akwatira Leya ndi Rakele

Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi. 15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”

16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele. 17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri. 18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”

19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.” 20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.

21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”

22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo. 23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye. 24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.

25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”

26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe. 27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”

28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake. 29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake. 30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.

Ana a Yakobo

31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala. 32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”

33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.

34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.

35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.

Jacob Arrives in Paddan Aram

29 Then Jacob continued on his journey and came to the land of the eastern peoples.(A) There he saw a well in the open country, with three flocks of sheep lying near it because the flocks were watered from that well.(B) The stone(C) over the mouth of the well was large. When all the flocks were gathered there, the shepherds would roll the stone(D) away from the well’s mouth and water the sheep.(E) Then they would return the stone to its place over the mouth of the well.

Jacob asked the shepherds, “My brothers, where are you from?”(F)

“We’re from Harran,(G)” they replied.

He said to them, “Do you know Laban, Nahor’s grandson?”(H)

“Yes, we know him,” they answered.

Then Jacob asked them, “Is he well?”

“Yes, he is,” they said, “and here comes his daughter Rachel(I) with the sheep.(J)

“Look,” he said, “the sun is still high; it is not time for the flocks to be gathered. Water the sheep and take them back to pasture.”

“We can’t,” they replied, “until all the flocks are gathered and the stone(K) has been rolled away from the mouth of the well. Then we will water(L) the sheep.”

While he was still talking with them, Rachel came with her father’s sheep,(M) for she was a shepherd. 10 When Jacob saw Rachel(N) daughter of his uncle Laban, and Laban’s sheep, he went over and rolled the stone(O) away from the mouth of the well and watered(P) his uncle’s sheep.(Q) 11 Then Jacob kissed(R) Rachel and began to weep aloud.(S) 12 He had told Rachel that he was a relative(T) of her father and a son of Rebekah.(U) So she ran and told her father.(V)

13 As soon as Laban(W) heard the news about Jacob, his sister’s son, he hurried to meet him. He embraced him(X) and kissed him and brought him to his home, and there Jacob told him all these things. 14 Then Laban said to him, “You are my own flesh and blood.”(Y)

Jacob Marries Leah and Rachel

After Jacob had stayed with him for a whole month, 15 Laban said to him, “Just because you are a relative(Z) of mine, should you work for me for nothing? Tell me what your wages(AA) should be.”

16 Now Laban had two daughters; the name of the older was Leah,(AB) and the name of the younger was Rachel.(AC) 17 Leah had weak[a] eyes, but Rachel(AD) had a lovely figure and was beautiful.(AE) 18 Jacob was in love with Rachel(AF) and said, “I’ll work for you seven years in return for your younger daughter Rachel.”(AG)

19 Laban said, “It’s better that I give her to you than to some other man. Stay here with me.” 20 So Jacob served seven years to get Rachel,(AH) but they seemed like only a few days to him because of his love for her.(AI)

21 Then Jacob said to Laban, “Give me my wife. My time is completed, and I want to make love to her.(AJ)

22 So Laban brought together all the people of the place and gave a feast.(AK) 23 But when evening came, he took his daughter Leah(AL) and brought her to Jacob, and Jacob made love to her. 24 And Laban gave his servant Zilpah(AM) to his daughter as her attendant.(AN)

25 When morning came, there was Leah! So Jacob said to Laban, “What is this you have done to me?(AO) I served you for Rachel, didn’t I? Why have you deceived me?(AP)

26 Laban replied, “It is not our custom here to give the younger daughter in marriage before the older one.(AQ) 27 Finish this daughter’s bridal week;(AR) then we will give you the younger one also, in return for another seven years of work.(AS)

28 And Jacob did so. He finished the week with Leah, and then Laban gave him his daughter Rachel to be his wife.(AT) 29 Laban gave his servant Bilhah(AU) to his daughter Rachel as her attendant.(AV) 30 Jacob made love to Rachel also, and his love for Rachel was greater than his love for Leah.(AW) And he worked for Laban another seven years.(AX)

Jacob’s Children

31 When the Lord saw that Leah was not loved,(AY) he enabled her to conceive,(AZ) but Rachel remained childless. 32 Leah became pregnant and gave birth to a son.(BA) She named him Reuben,[b](BB) for she said, “It is because the Lord has seen my misery.(BC) Surely my husband will love me now.”

33 She conceived again, and when she gave birth to a son she said, “Because the Lord heard that I am not loved,(BD) he gave me this one too.” So she named him Simeon.[c](BE)

34 Again she conceived, and when she gave birth to a son she said, “Now at last my husband will become attached to me,(BF) because I have borne him three sons.” So he was named Levi.[d](BG)

35 She conceived again, and when she gave birth to a son she said, “This time I will praise the Lord.” So she named him Judah.[e](BH) Then she stopped having children.(BI)

Footnotes

  1. Genesis 29:17 Or delicate
  2. Genesis 29:32 Reuben sounds like the Hebrew for he has seen my misery; the name means see, a son.
  3. Genesis 29:33 Simeon probably means one who hears.
  4. Genesis 29:34 Levi sounds like and may be derived from the Hebrew for attached.
  5. Genesis 29:35 Judah sounds like and may be derived from the Hebrew for praise.