Add parallel Print Page Options

Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.

Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse. Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.

Adamu ndi Hava

Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi:

Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba, zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka, koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse. Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.

Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja. Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.

10 Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi. 11 Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide. 12 (Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi). 13 Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi. 14 Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.

15 Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira. 16 Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu; 17 koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”

18 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”

19 Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake. 20 Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse.

Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza. 21 Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu. 22 Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.

23 Munthu uja anati,

“Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga
    ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga;
adzatchedwa ‘mkazi,’
    popeza wachokera mwa mwamuna.”

24 Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.

25 Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.

Thus the heavens and the earth were completed in all their vast array.(A)

By the seventh day(B) God had finished the work he had been doing; so on the seventh day he rested from all his work.(C) Then God blessed the seventh day and made it holy,(D) because on it he rested(E) from all the work of creating(F) that he had done.

Adam and Eve

This is the account(G) of the heavens and the earth when they were created,(H) when the Lord God made the earth and the heavens.

Now no shrub had yet appeared on the earth[a] and no plant had yet sprung up,(I) for the Lord God had not sent rain on the earth(J) and there was no one to work the ground, but streams[b] came up from the earth and watered the whole surface of the ground. Then the Lord God formed(K) a man[c](L) from the dust(M) of the ground(N) and breathed into his nostrils the breath(O) of life,(P) and the man became a living being.(Q)

Now the Lord God had planted a garden in the east, in Eden;(R) and there he put the man he had formed. The Lord God made all kinds of trees grow out of the ground—trees(S) that were pleasing to the eye and good for food. In the middle of the garden were the tree of life(T) and the tree of the knowledge of good and evil.(U)

10 A river(V) watering the garden flowed from Eden;(W) from there it was separated into four headwaters. 11 The name of the first is the Pishon; it winds through the entire land of Havilah,(X) where there is gold. 12 (The gold of that land is good; aromatic resin[d](Y) and onyx are also there.) 13 The name of the second river is the Gihon; it winds through the entire land of Cush.[e] 14 The name of the third river is the Tigris;(Z) it runs along the east side of Ashur. And the fourth river is the Euphrates.(AA)

15 The Lord God took the man and put him in the Garden of Eden(AB) to work it and take care of it. 16 And the Lord God commanded the man, “You are free to eat from any tree in the garden;(AC) 17 but you must not eat from the tree of the knowledge of good and evil,(AD) for when you eat from it you will certainly die.”(AE)

18 The Lord God said, “It is not good for the man to be alone. I will make a helper suitable for him.”(AF)

19 Now the Lord God had formed out of the ground all the wild animals(AG) and all the birds in the sky.(AH) He brought them to the man to see what he would name them; and whatever the man called(AI) each living creature,(AJ) that was its name. 20 So the man gave names to all the livestock, the birds in the sky and all the wild animals.

But for Adam[f] no suitable helper(AK) was found. 21 So the Lord God caused the man to fall into a deep sleep;(AL) and while he was sleeping, he took one of the man’s ribs[g] and then closed up the place with flesh. 22 Then the Lord God made a woman from the rib[h](AM) he had taken out of the man, and he brought her to the man.

23 The man said,

“This is now bone of my bones
    and flesh of my flesh;(AN)
she shall be called(AO) ‘woman,’
    for she was taken out of man.(AP)

24 That is why a man leaves his father and mother and is united(AQ) to his wife, and they become one flesh.(AR)

25 Adam and his wife were both naked,(AS) and they felt no shame.

Footnotes

  1. Genesis 2:5 Or land; also in verse 6
  2. Genesis 2:6 Or mist
  3. Genesis 2:7 The Hebrew for man (adam) sounds like and may be related to the Hebrew for ground (adamah); it is also the name Adam (see verse 20).
  4. Genesis 2:12 Or good; pearls
  5. Genesis 2:13 Possibly southeast Mesopotamia
  6. Genesis 2:20 Or the man
  7. Genesis 2:21 Or took part of the man’s side
  8. Genesis 2:22 Or part