Add parallel Print Page Options

Sarai ndi Hagara

16 Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara; ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.”

Abramu anamvera Sarai. Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi. Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba.

Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai. Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”

Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.

Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri. Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?”

Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”

Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere. 10 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”

11 Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti,

“Ndiwe woyembekezera
    ndipo udzabala mwana wamwamuna.
Udzamutcha dzina lake Ismaeli,
    pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.
12 Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala;
    adzadana ndi aliyense
    ndipo anthu onse adzadana naye,
adzakhala mwaudani pakati pa abale ake
    onse.”

13 Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.” 14 Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.

15 Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli. 16 Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.

Hagar and Ishmael

16 Now Sarai,(A) Abram’s wife, had borne him no children.(B) But she had an Egyptian slave(C) named Hagar;(D) so she said to Abram, “The Lord has kept me from having children.(E) Go, sleep with my slave; perhaps I can build a family through her.”(F)

Abram agreed to what Sarai said. So after Abram had been living in Canaan(G) ten years,(H) Sarai his wife took her Egyptian slave Hagar and gave her to her husband to be his wife. He slept with Hagar,(I) and she conceived.

When she knew she was pregnant, she began to despise her mistress.(J) Then Sarai said to Abram, “You are responsible for the wrong I am suffering. I put my slave in your arms, and now that she knows she is pregnant, she despises me. May the Lord judge between you and me.”(K)

“Your slave is in your hands,(L)” Abram said. “Do with her whatever you think best.” Then Sarai mistreated(M) Hagar; so she fled from her.

The angel of the Lord(N) found Hagar near a spring(O) in the desert; it was the spring that is beside the road to Shur.(P) And he said, “Hagar,(Q) slave of Sarai, where have you come from, and where are you going?”(R)

“I’m running away from my mistress Sarai,” she answered.

Then the angel of the Lord told her, “Go back to your mistress and submit to her.” 10 The angel added, “I will increase your descendants so much that they will be too numerous to count.”(S)

11 The angel of the Lord(T) also said to her:

“You are now pregnant
    and you will give birth to a son.(U)
You shall name him(V) Ishmael,[a](W)
    for the Lord has heard of your misery.(X)
12 He will be a wild donkey(Y) of a man;
    his hand will be against everyone
    and everyone’s hand against him,
and he will live in hostility
    toward[b] all his brothers.(Z)

13 She gave this name to the Lord who spoke to her: “You are the God who sees me,(AA)” for she said, “I have now seen[c] the One who sees me.”(AB) 14 That is why the well(AC) was called Beer Lahai Roi[d];(AD) it is still there, between Kadesh(AE) and Bered.

15 So Hagar(AF) bore Abram a son,(AG) and Abram gave the name Ishmael(AH) to the son she had borne. 16 Abram was eighty-six years old(AI) when Hagar bore him Ishmael.

Footnotes

  1. Genesis 16:11 Ishmael means God hears.
  2. Genesis 16:12 Or live to the east / of
  3. Genesis 16:13 Or seen the back of
  4. Genesis 16:14 Beer Lahai Roi means well of the Living One who sees me.