Add parallel Print Page Options

Abramu Apulumutsa Loti

14 Pa nthawi imeneyi Amarafeli mfumu ya Sinara, Arioki mfumu ya Elasara, Kedorilaomere mfumu ya Elamu ndi Tidala mfumu ya Goimu anathira nkhondo Bera mfumu ya ku Sodomu, Birisa mfumu ya Gomora, Sinabi mfumu ya Adima, Semeberi mfumu ya Ziboimu ndi mfumu ya Bela (kumeneko ndi ku Zowari). Mafumu onse anathiridwa nkhondowa anagwirizana pamodzi kupita ku Chigwa cha Sidimu (Nyanja ya Mchere). Kwa zaka khumi ndi ziwiri anali pansi pa ulamuliro wa Kedorilaomere, koma mʼchaka cha khumi ndi chitatu anamuwukira.

Mʼchaka cha khumi ndi chinayi, Kedorilaomere mogwirizana ndi mafumu ena aja anapita kukagonjetsa Arefaiwa ku Asiteroti-karanaimu, Zuzimu wa ku Hamu, Aemi wa ku Savekiriataimu amene ankakhala ku Ahori, ku dziko la mapiri la Seiri mpaka ku Eli Parani kufupi ndi chipululu. Kenaka anabwerera napita ku Eni-Misipati (ku Kadesi), ndipo anagonjetsa dera lonse la Aamaleki, kuphatikizanso Aamori amene ankakhala ku Hazazoni Tamara.

Tsono mafumu a ku Sodomu, Gomora, Adima, Zeboimu ndi ku Bela (ku Zowari) anapita ku Chigwa cha Sidimu kukakonzekera kuthira nkhondo Kedorilaomere mfumu ya Elamu, Tidala mfumu ya Goimu, Amarafeli mfumu ya Sinara ndi Arioki mfumu ya Elasara. Mafumu anayi analimbana ndi mafumu asanu. 10 Koma Chigwa cha Sidimu chinali chodzaza ndi maenje aphula. Choncho pamene mafumu a ku Sodomu ndi Gomora amathawa, ankhondo ena anagweramo ndipo ena anathawira ku mapiri. 11 Mafumu anayi aja anatenga katundu yense ndi chakudya chonse cha ku Sodomu ndi Gomora napita nazo. 12 Anatenganso Loti, mwana wa mʼbale wake wa Abramu pamodzi ndi katundu wake popeza ankakhala mu Sodomu.

13 Koma munthu wina amene anathawa, anabwera kudzamufotokozera Abramu Mhebri. Tsono Abramu ankakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya Mamre wa fuko la Aamori, mʼbale wake wa Esikolo ndi Aneri. Onsewa anali pa mgwirizano ndi Abramu. 14 Abramu atamva kuti Loti wagwidwa pa nkhondo, anasonkhanitsa asilikali 318 obadwira mʼbanja lake lomwelo nalondola mpaka ku Dani. 15 Pa nthawi ya usiku Abramu anawagawa asilikali ake kuti athire nkhondo mafumu aja, ndipo anawakantha nawapirikitsa mpaka ku Hoba, cha kumpoto kwa Damasiko. 16 Ndipo anawalanda katundu wawo yense nabwera naye Loti, katundu wake yense, pamodzi ndi akazi ndi anthu ena.

17 Abramu atabwerera kuchokera kogonjetsa Kedorilaomere ndi mafumu amene anali nawo pa mgwirizano, mfumu ya ku Sodomu inabwera kudzakumana naye ku Chigwa cha Save (chimenechi ndicho Chigwa cha Mfumu).

18 Ndipo Melikizedeki mfumu ya ku Salemu anabweretsa buledi ndi vinyo. Iyeyu anali wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba, 19 ndipo anadalitsa Abramu nati,

“Mulungu Wammwambamwamba,
    wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, akudalitse iwe Abramu.
20 Ndipo adalitsike Mulungu Wammwambamwamba
    amene anapereka adani ako mʼdzanja lako.”

Ndipo Abramu anamupatsa iye chakhumi cha zonse anali nazo.

21 Mfumu ya Sodomu inati kwa Abramu, “Ine undipatse anthu okhawo, koma katundu akhale wako.”

22 Koma Abramu anawuza mfumu ya Sodomu kuti, “Ndakweza manja anga kwa Yehova, Mulungu Wammwambamwamba, Mlengi wakumwamba ndi dziko lapansi, kulumbira 23 kuti sindidzalandira kanthu kalikonse kako, ngakhale utakhala ulusi chabe kapena chingwe cha nsapato, kuopa kuti ungamanene kuti, ‘Ndamulemeretsa Abramu.’ 24 Sindidzalandira kanthu kalikonse kupatula zokhazo zimene anthu anga adya ndi gawo la katundu la anthu amene ndinapita nawo monga Aneri, Esikolo ndi Mamre. Iwowa atenge gawo lawo.”

Abram Rescues Lot

14 At the time when Amraphel was king of Shinar,[a](A) Arioch king of Ellasar, Kedorlaomer(B) king of Elam(C) and Tidal king of Goyim, these kings went to war against Bera king of Sodom, Birsha king of Gomorrah, Shinab king of Admah, Shemeber king of Zeboyim,(D) and the king of Bela (that is, Zoar).(E) All these latter kings joined forces in the Valley of Siddim(F) (that is, the Dead Sea Valley(G)). For twelve years they had been subject to Kedorlaomer,(H) but in the thirteenth year they rebelled.

In the fourteenth year, Kedorlaomer(I) and the kings allied with him went out and defeated the Rephaites(J) in Ashteroth Karnaim, the Zuzites in Ham, the Emites(K) in Shaveh Kiriathaim and the Horites(L) in the hill country of Seir,(M) as far as El Paran(N) near the desert. Then they turned back and went to En Mishpat (that is, Kadesh),(O) and they conquered the whole territory of the Amalekites,(P) as well as the Amorites(Q) who were living in Hazezon Tamar.(R)

Then the king of Sodom, the king of Gomorrah,(S) the king of Admah, the king of Zeboyim(T) and the king of Bela (that is, Zoar)(U) marched out and drew up their battle lines in the Valley of Siddim(V) against Kedorlaomer(W) king of Elam,(X) Tidal king of Goyim, Amraphel king of Shinar and Arioch king of Ellasar—four kings against five. 10 Now the Valley of Siddim(Y) was full of tar(Z) pits, and when the kings of Sodom and Gomorrah(AA) fled, some of the men fell into them and the rest fled to the hills.(AB) 11 The four kings seized all the goods(AC) of Sodom and Gomorrah and all their food; then they went away. 12 They also carried off Abram’s nephew Lot(AD) and his possessions, since he was living in Sodom.

13 A man who had escaped came and reported this to Abram the Hebrew.(AE) Now Abram was living near the great trees of Mamre(AF) the Amorite, a brother[b] of Eshkol(AG) and Aner, all of whom were allied with Abram. 14 When Abram heard that his relative(AH) had been taken captive, he called out the 318 trained(AI) men born in his household(AJ) and went in pursuit as far as Dan.(AK) 15 During the night Abram divided his men(AL) to attack them and he routed them, pursuing them as far as Hobah, north of Damascus.(AM) 16 He recovered(AN) all the goods(AO) and brought back his relative Lot and his possessions, together with the women and the other people.

17 After Abram returned from defeating Kedorlaomer(AP) and the kings allied with him, the king of Sodom(AQ) came out to meet him in the Valley of Shaveh (that is, the King’s Valley).(AR)

18 Then Melchizedek(AS) king of Salem(AT) brought out bread(AU) and wine.(AV) He was priest of God Most High,(AW) 19 and he blessed Abram,(AX) saying,

“Blessed be Abram by God Most High,(AY)
    Creator of heaven and earth.(AZ)
20 And praise be to God Most High,(BA)
    who delivered your enemies into your hand.”

Then Abram gave him a tenth of everything.(BB)

21 The king of Sodom(BC) said to Abram, “Give me the people and keep the goods(BD) for yourself.”

22 But Abram said to the king of Sodom,(BE) “With raised hand(BF) I have sworn an oath to the Lord, God Most High,(BG) Creator of heaven and earth,(BH) 23 that I will accept nothing belonging to you,(BI) not even a thread or the strap of a sandal, so that you will never be able to say, ‘I made Abram rich.’ 24 I will accept nothing but what my men have eaten and the share that belongs to the men who went with me—to Aner, Eshkol and Mamre.(BJ) Let them have their share.”

Footnotes

  1. Genesis 14:1 That is, Babylonia; also in verse 9
  2. Genesis 14:13 Or a relative; or an ally