Add parallel Print Page Options

Kupembedza Mafano Mʼnyumba ya Mulungu

Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira. Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira. Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu. Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.

Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.

Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”

Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo. Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.

Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.” 10 Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza. 11 Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.

12 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’ 13 Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’ ”

14 Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi. 15 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”

16 Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.

17 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo! 18 Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

Idolatry in the Temple

In the sixth year, in the sixth month on the fifth day, while I was sitting in my house and the elders(A) of Judah were sitting before(B) me, the hand of the Sovereign Lord came on me there.(C) I looked, and I saw a figure like that of a man.[a] From what appeared to be his waist down he was like fire, and from there up his appearance was as bright as glowing metal.(D) He stretched out what looked like a hand(E) and took me by the hair of my head. The Spirit lifted me up(F) between earth and heaven and in visions(G) of God he took me to Jerusalem, to the entrance of the north gate of the inner court,(H) where the idol that provokes to jealousy(I) stood. And there before me was the glory(J) of the God of Israel, as in the vision I had seen in the plain.(K)

Then he said to me, “Son of man, look toward the north.” So I looked, and in the entrance north of the gate of the altar I saw this idol(L) of jealousy.

And he said to me, “Son of man, do you see what they are doing—the utterly detestable(M) things the Israelites are doing here, things that will drive me far from my sanctuary?(N) But you will see things that are even more detestable.”

Then he brought me to the entrance to the court. I looked, and I saw a hole in the wall. He said to me, “Son of man, now dig into the wall.” So I dug into the wall and saw a doorway there.

And he said to me, “Go in and see the wicked and detestable things they are doing here.” 10 So I went in and looked, and I saw portrayed all over the walls(O) all kinds of crawling things and unclean(P) animals and all the idols of Israel.(Q) 11 In front of them stood seventy elders(R) of Israel, and Jaazaniah son of Shaphan was standing among them. Each had a censer(S) in his hand, and a fragrant cloud of incense(T) was rising.(U)

12 He said to me, “Son of man, have you seen what the elders of Israel are doing in the darkness,(V) each at the shrine of his own idol? They say, ‘The Lord does not see(W) us; the Lord has forsaken the land.’” 13 Again, he said, “You will see them doing things that are even more detestable.”

14 Then he brought me to the entrance of the north gate of the house of the Lord, and I saw women sitting there, mourning the god Tammuz.(X) 15 He said to me, “Do you see this, son of man? You will see things that are even more detestable than this.”

16 He then brought me into the inner court(Y) of the house of the Lord, and there at the entrance to the temple, between the portico and the altar,(Z) were about twenty-five men. With their backs toward the temple of the Lord and their faces toward the east, they were bowing down to the sun(AA) in the east.(AB)

17 He said to me, “Have you seen this, son of man? Is it a trivial matter for the people of Judah to do the detestable things(AC) they are doing here? Must they also fill the land with violence(AD) and continually arouse my anger?(AE) Look at them putting the branch to their nose! 18 Therefore I will deal with them in anger;(AF) I will not look on them with pity(AG) or spare them. Although they shout in my ears, I will not listen(AH) to them.”

Footnotes

  1. Ezekiel 8:2 Or saw a fiery figure