Add parallel Print Page Options

46 “Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo. Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano. Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema. Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu. Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema. Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta. Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.

“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho. 10 Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.

11 “Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse. 12 Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.

13 “Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi. 14 Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo. 15 Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.

16 “ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo. 17 Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake. 18 Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’ ”

19 Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo. 20 Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”

21 Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina. 22 Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu. 23 Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira. 24 Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”

46 “‘This is what the Sovereign Lord says: The gate of the inner court(A) facing east(B) is to be shut on the six working days, but on the Sabbath day and on the day of the New Moon(C) it is to be opened. The prince is to enter from the outside through the portico(D) of the gateway and stand by the gatepost. The priests are to sacrifice his burnt offering(E) and his fellowship offerings. He is to bow down in worship at the threshold of the gateway and then go out, but the gate will not be shut until evening.(F) On the Sabbaths(G) and New Moons the people of the land are to worship in the presence of the Lord at the entrance of that gateway.(H) The burnt offering the prince brings to the Lord on the Sabbath day is to be six male lambs and a ram, all without defect. The grain offering given with the ram is to be an ephah,[a] and the grain offering with the lambs is to be as much as he pleases, along with a hin[b] of olive oil for each ephah.(I) On the day of the New Moon(J) he is to offer a young bull, six lambs and a ram, all without defect.(K) He is to provide as a grain offering one ephah with the bull, one ephah with the ram, and with the lambs as much as he wants to give, along with a hin of oil for each ephah.(L) When the prince enters, he is to go in through the portico(M) of the gateway, and he is to come out the same way.(N)

“‘When the people of the land come before the Lord at the appointed festivals,(O) whoever enters by the north gate to worship is to go out the south gate; and whoever enters by the south gate is to go out the north gate. No one is to return through the gate by which they entered, but each is to go out the opposite gate. 10 The prince is to be among them, going in when they go in and going out when they go out.(P) 11 At the feasts and the appointed festivals, the grain offering is to be an ephah with a bull, an ephah with a ram, and with the lambs as much as he pleases, along with a hin of oil for each ephah.(Q)

12 “‘When the prince provides(R) a freewill offering(S) to the Lord—whether a burnt offering or fellowship offerings—the gate facing east is to be opened for him. He shall offer his burnt offering or his fellowship offerings as he does on the Sabbath day. Then he shall go out, and after he has gone out, the gate will be shut.(T)

13 “‘Every day you are to provide a year-old lamb without defect for a burnt offering to the Lord; morning by morning(U) you shall provide it.(V) 14 You are also to provide with it morning by morning a grain offering, consisting of a sixth of an ephah[c] with a third of a hin[d] of oil(W) to moisten the flour. The presenting of this grain offering to the Lord is a lasting ordinance.(X) 15 So the lamb and the grain offering and the oil shall be provided morning by morning for a regular(Y) burnt offering.(Z)

16 “‘This is what the Sovereign Lord says: If the prince makes a gift from his inheritance to one of his sons, it will also belong to his descendants; it is to be their property by inheritance.(AA) 17 If, however, he makes a gift from his inheritance to one of his servants, the servant may keep it until the year of freedom;(AB) then it will revert to the prince. His inheritance belongs to his sons only; it is theirs. 18 The prince must not take(AC) any of the inheritance(AD) of the people, driving them off their property. He is to give his sons their inheritance out of his own property, so that not one of my people will be separated from their property.’”

19 Then the man brought me through the entrance(AE) at the side of the gate to the sacred rooms facing north,(AF) which belonged to the priests, and showed me a place at the western end. 20 He said to me, “This is the place where the priests are to cook the guilt offering and the sin offering[e] and bake the grain offering, to avoid bringing them into the outer court and consecrating(AG) the people.”(AH)

21 He then brought me to the outer court and led me around to its four corners, and I saw in each corner another court. 22 In the four corners of the outer court were enclosed[f] courts, forty cubits long and thirty cubits wide;[g] each of the courts in the four corners was the same size. 23 Around the inside of each of the four courts was a ledge of stone, with places for fire built all around under the ledge. 24 He said to me, “These are the kitchens where those who minister at the temple are to cook the sacrifices of the people.”

Footnotes

  1. Ezekiel 46:5 That is, probably about 35 pounds or about 16 kilograms; also in verses 7 and 11
  2. Ezekiel 46:5 That is, about 1 gallon or about 3.8 liters; also in verses 7 and 11
  3. Ezekiel 46:14 That is, probably about 6 pounds or about 2.7 kilograms
  4. Ezekiel 46:14 That is, about 1 1/2 quarts or about 1.3 liters
  5. Ezekiel 46:20 Or purification offering
  6. Ezekiel 46:22 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  7. Ezekiel 46:22 That is, about 70 feet long and 53 feet wide or about 21 meters long and 16 meters wide