Add parallel Print Page Options

Abusa a Israeli

34 Yehova anandiyankhula kuti: “Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa? Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo. Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza. Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo. Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.

“ ‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani. Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga. Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani. 10 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.

11 “ ‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira. 12 Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima. 13 Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu. 14 Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli. 15 Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 16 Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.

17 “ ‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna. 18 Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu? 19 Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?

20 “ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda. 21 Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali, 22 tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso. 23 Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo. 24 Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.

25 “ ‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo. 26 Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso. 27 Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo. 28 Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze. 29 Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso. 30 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 31 Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’ ”

The Lord Will Be Israel’s Shepherd

34 The word of the Lord came to me: “Son of man, prophesy against the shepherds of Israel; prophesy and say to them: ‘This is what the Sovereign Lord says: Woe to you shepherds of Israel who only take care of yourselves! Should not shepherds take care of the flock?(A) You eat the curds, clothe yourselves with the wool and slaughter the choice animals, but you do not take care of the flock.(B) You have not strengthened the weak or healed(C) the sick or bound up(D) the injured. You have not brought back the strays or searched for the lost. You have ruled them harshly and brutally.(E) So they were scattered because there was no shepherd,(F) and when they were scattered they became food for all the wild animals.(G) My sheep wandered over all the mountains and on every high hill.(H) They were scattered(I) over the whole earth, and no one searched or looked for them.(J)

“‘Therefore, you shepherds, hear the word of the Lord: As surely as I live, declares the Sovereign Lord, because my flock lacks a shepherd and so has been plundered(K) and has become food for all the wild animals,(L) and because my shepherds did not search for my flock but cared for themselves rather than for my flock,(M) therefore, you shepherds, hear the word of the Lord: 10 This is what the Sovereign Lord says: I am against(N) the shepherds and will hold them accountable for my flock. I will remove them from tending the flock so that the shepherds can no longer feed themselves. I will rescue(O) my flock from their mouths, and it will no longer be food for them.(P)

11 “‘For this is what the Sovereign Lord says: I myself will search for my sheep(Q) and look after them. 12 As a shepherd(R) looks after his scattered flock when he is with them, so will I look after my sheep. I will rescue them from all the places where they were scattered on a day of clouds and darkness.(S) 13 I will bring them out from the nations and gather(T) them from the countries, and I will bring them into their own land.(U) I will pasture them on the mountains of Israel, in the ravines and in all the settlements in the land.(V) 14 I will tend them in a good pasture, and the mountain heights of Israel(W) will be their grazing land. There they will lie down in good grazing land, and there they will feed in a rich pasture(X) on the mountains of Israel.(Y) 15 I myself will tend my sheep and have them lie down,(Z) declares the Sovereign Lord.(AA) 16 I will search for the lost and bring back the strays. I will bind up(AB) the injured and strengthen the weak,(AC) but the sleek and the strong I will destroy.(AD) I will shepherd the flock with justice.(AE)

17 “‘As for you, my flock, this is what the Sovereign Lord says: I will judge between one sheep and another, and between rams and goats.(AF) 18 Is it not enough(AG) for you to feed on the good pasture? Must you also trample the rest of your pasture with your feet?(AH) Is it not enough for you to drink clear water? Must you also muddy the rest with your feet? 19 Must my flock feed on what you have trampled and drink what you have muddied with your feet?

20 “‘Therefore this is what the Sovereign Lord says to them: See, I myself will judge between the fat sheep and the lean sheep.(AI) 21 Because you shove with flank and shoulder, butting all the weak sheep with your horns(AJ) until you have driven them away, 22 I will save my flock, and they will no longer be plundered. I will judge between one sheep and another.(AK) 23 I will place over them one shepherd, my servant David, and he will tend(AL) them; he will tend them and be their shepherd.(AM) 24 I the Lord will be their God,(AN) and my servant David(AO) will be prince among them.(AP) I the Lord have spoken.(AQ)

25 “‘I will make a covenant(AR) of peace(AS) with them and rid the land of savage beasts(AT) so that they may live in the wilderness and sleep in the forests in safety.(AU) 26 I will make them and the places surrounding my hill a blessing.[a](AV) I will send down showers in season;(AW) there will be showers of blessing.(AX) 27 The trees will yield their fruit(AY) and the ground will yield its crops;(AZ) the people will be secure(BA) in their land. They will know that I am the Lord, when I break the bars of their yoke(BB) and rescue them from the hands of those who enslaved them.(BC) 28 They will no longer be plundered by the nations, nor will wild animals devour them. They will live in safety,(BD) and no one will make them afraid.(BE) 29 I will provide for them a land renowned(BF) for its crops, and they will no longer be victims of famine(BG) in the land or bear the scorn(BH) of the nations.(BI) 30 Then they will know that I, the Lord their God, am with them and that they, the Israelites, are my people, declares the Sovereign Lord.(BJ) 31 You are my sheep,(BK) the sheep of my pasture,(BL) and I am your God, declares the Sovereign Lord.’”

Footnotes

  1. Ezekiel 34:26 Or I will cause them and the places surrounding my hill to be named in blessings (see Gen. 48:20); or I will cause them and the places surrounding my hill to be seen as blessed