Add parallel Print Page Options

Za Yerusalemu ndi Samariya

23 Yehova anandiyankhula nati: “Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi. Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja. Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.

“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya. Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo. Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye. Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.

“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka. 10 Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.

11 “Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake. 12 Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka. 13 Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.

14 “Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira, 15 atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya. 16 Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana. 17 Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo. 18 Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake. 19 Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto. 20 Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo. 21 Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.

22 “Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse. 23 Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo. 24 Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire. 25 Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto. 26 Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali. 27 Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.

28 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo. 29 Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako, 30 zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo. 31 Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.

32 “Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“Udzamwera chikho cha mkulu wako,
    chikho chachikulu ndi chakuya;
anthu adzakuseka ndi kukunyoza,
    pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni.
    Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu,
    chikho cha mkulu wako Samariya.
34 Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza.
    Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho
    ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake.

Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.

35 “Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”

36 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa. 37 Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo. 38 Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga. 39 Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.

40 “Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka. 41 Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.

42 “Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu. 43 Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’ 44 Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama. 45 Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.

46 “Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo. 47 Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.

48 “Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo. 49 Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

Two Adulterous Sisters

23 The word of the Lord came to me: “Son of man, there were two women, daughters of the same mother.(A) They became prostitutes in Egypt,(B) engaging in prostitution(C) from their youth.(D) In that land their breasts were fondled and their virgin bosoms caressed.(E) The older was named Oholah, and her sister was Oholibah. They were mine and gave birth to sons and daughters. Oholah is Samaria, and Oholibah is Jerusalem.(F)

“Oholah engaged in prostitution while she was still mine; and she lusted after her lovers, the Assyrians(G)—warriors(H) clothed in blue, governors and commanders, all of them handsome young men, and mounted horsemen. She gave herself as a prostitute to all the elite of the Assyrians and defiled herself with all the idols of everyone she lusted after.(I) She did not give up the prostitution she began in Egypt,(J) when during her youth men slept with her, caressed her virgin bosom and poured out their lust on her.(K)

“Therefore I delivered her into the hands(L) of her lovers,(M) the Assyrians, for whom she lusted.(N) 10 They stripped(O) her naked, took away her sons and daughters and killed her with the sword. She became a byword among women,(P) and punishment was inflicted(Q) on her.(R)

11 “Her sister Oholibah saw this,(S) yet in her lust and prostitution she was more depraved than her sister.(T) 12 She too lusted after the Assyrians—governors and commanders, warriors in full dress, mounted horsemen, all handsome young men.(U) 13 I saw that she too defiled herself; both of them went the same way.(V)

14 “But she carried her prostitution still further. She saw men portrayed on a wall,(W) figures of Chaldeans[a] portrayed in red,(X) 15 with belts(Y) around their waists and flowing turbans on their heads; all of them looked like Babylonian chariot officers, natives of Chaldea.[b] 16 As soon as she saw them, she lusted after them and sent messengers(Z) to them in Chaldea.(AA) 17 Then the Babylonians(AB) came to her, to the bed of love, and in their lust they defiled her. After she had been defiled by them, she turned away from them in disgust.(AC) 18 When she carried on her prostitution openly and exposed her naked body,(AD) I turned away(AE) from her in disgust, just as I had turned away from her sister.(AF) 19 Yet she became more and more promiscuous as she recalled the days of her youth, when she was a prostitute in Egypt. 20 There she lusted after her lovers, whose genitals were like those of donkeys and whose emission was like that of horses. 21 So you longed for the lewdness of your youth, when in Egypt your bosom was caressed and your young breasts fondled.[c](AG)

22 “Therefore, Oholibah, this is what the Sovereign Lord says: I will stir up your lovers(AH) against you, those you turned away from in disgust, and I will bring them against you from every side(AI) 23 the Babylonians(AJ) and all the Chaldeans,(AK) the men of Pekod(AL) and Shoa and Koa, and all the Assyrians with them, handsome young men, all of them governors and commanders, chariot officers and men of high rank, all mounted on horses.(AM) 24 They will come against you with weapons,[d] chariots and wagons(AN) and with a throng of people; they will take up positions against you on every side with large and small shields and with helmets. I will turn you over to them for punishment,(AO) and they will punish you according to their standards. 25 I will direct my jealous anger(AP) against you, and they will deal with you in fury. They will cut off your noses and your ears, and those of you who are left will fall by the sword. They will take away your sons and daughters,(AQ) and those of you who are left will be consumed by fire.(AR) 26 They will also strip(AS) you of your clothes and take your fine jewelry.(AT) 27 So I will put a stop(AU) to the lewdness and prostitution you began in Egypt. You will not look on these things with longing or remember Egypt anymore.

28 “For this is what the Sovereign Lord says: I am about to deliver you into the hands(AV) of those you hate, to those you turned away from in disgust. 29 They will deal with you in hatred and take away everything you have worked for. They will leave you stark naked,(AW) and the shame of your prostitution will be exposed.(AX) Your lewdness(AY) and promiscuity(AZ) 30 have brought this on you, because you lusted after the nations and defiled yourself with their idols.(BA) 31 You have gone the way of your sister; so I will put her cup(BB) into your hand.(BC)

32 “This is what the Sovereign Lord says:

“You will drink your sister’s cup,
    a cup large and deep;
it will bring scorn and derision,(BD)
    for it holds so much.(BE)
33 You will be filled with drunkenness and sorrow,
    the cup of ruin and desolation,
    the cup of your sister Samaria.(BF)
34 You will drink it(BG) and drain it dry
    and chew on its pieces—
    and you will tear your breasts.

I have spoken, declares the Sovereign Lord.(BH)

35 “Therefore this is what the Sovereign Lord says: Since you have forgotten(BI) me and turned your back on me,(BJ) you must bear(BK) the consequences of your lewdness and prostitution.”

36 The Lord said to me: “Son of man, will you judge Oholah and Oholibah? Then confront(BL) them with their detestable practices,(BM) 37 for they have committed adultery and blood is on their hands. They committed adultery with their idols; they even sacrificed their children, whom they bore to me, as food for them.(BN) 38 They have also done this to me: At that same time they defiled my sanctuary(BO) and desecrated my Sabbaths.(BP) 39 On the very day they sacrificed their children to their idols, they entered my sanctuary and desecrated(BQ) it. That is what they did in my house.(BR)

40 “They even sent messengers for men who came from far away,(BS) and when they arrived you bathed yourself for them, applied eye makeup(BT) and put on your jewelry.(BU) 41 You sat on an elegant couch,(BV) with a table(BW) spread before it on which you had placed the incense(BX) and olive oil that belonged to me.(BY)

42 “The noise of a carefree(BZ) crowd was around her; drunkards(CA) were brought from the desert along with men from the rabble, and they put bracelets(CB) on the wrists of the woman and her sister and beautiful crowns on their heads.(CC) 43 Then I said about the one worn out by adultery, ‘Now let them use her as a prostitute,(CD) for that is all she is.’ 44 And they slept with her. As men sleep with a prostitute, so they slept with those lewd women, Oholah and Oholibah. 45 But righteous judges will sentence them to the punishment of women who commit adultery and shed blood,(CE) because they are adulterous and blood is on their hands.(CF)

46 “This is what the Sovereign Lord says: Bring a mob(CG) against them and give them over to terror and plunder.(CH) 47 The mob will stone them and cut them down with their swords; they will kill their sons and daughters(CI) and burn(CJ) down their houses.(CK)

48 “So I will put an end(CL) to lewdness in the land, that all women may take warning and not imitate you.(CM) 49 You will suffer the penalty for your lewdness and bear the consequences of your sins of idolatry.(CN) Then you will know that I am the Sovereign Lord.(CO)

Footnotes

  1. Ezekiel 23:14 Or Babylonians
  2. Ezekiel 23:15 Or Babylonia; also in verse 16
  3. Ezekiel 23:21 Syriac (see also verse 3); Hebrew caressed because of your young breasts
  4. Ezekiel 23:24 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.