Add parallel Print Page Options

Machimo a Yerusalemu

22 Yehova anandiyankhula nati: “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano, wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke. Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.

“ ‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu. Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye. Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga. Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa. 10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo. 11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo. 12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.

13 “ ‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu. 14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi. 15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako. 16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

17 Yehova anandiyankhula nati: 18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva. 19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu. 20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani. 21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo. 22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’ ”

23 Yehova anandiyankhulanso nati, 24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’ 25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye. 26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo. 27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa. 28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule. 29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.

30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze. 31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

Judgment on Jerusalem’s Sins

22 The word of the Lord came to me:

“Son of man, will you judge her? Will you judge this city of bloodshed?(A) Then confront her with all her detestable practices(B) and say: ‘This is what the Sovereign Lord says: You city that brings on herself doom by shedding blood(C) in her midst and defiles herself by making idols, you have become guilty because of the blood you have shed(D) and have become defiled by the idols you have made. You have brought your days to a close, and the end of your years has come.(E) Therefore I will make you an object of scorn(F) to the nations and a laughingstock to all the countries.(G) Those who are near and those who are far away will mock you, you infamous city, full of turmoil.(H)

“‘See how each of the princes of Israel who are in you uses his power to shed blood.(I) In you they have treated father and mother with contempt;(J) in you they have oppressed the foreigner(K) and mistreated the fatherless and the widow.(L) You have despised my holy things and desecrated my Sabbaths.(M) In you are slanderers(N) who are bent on shedding blood;(O) in you are those who eat at the mountain shrines(P) and commit lewd acts.(Q) 10 In you are those who dishonor their father’s bed;(R) in you are those who violate women during their period,(S) when they are ceremonially unclean.(T) 11 In you one man commits a detestable offense with his neighbor’s wife,(U) another shamefully defiles his daughter-in-law,(V) and another violates his sister,(W) his own father’s daughter.(X) 12 In you are people who accept bribes(Y) to shed blood; you take interest(Z) and make a profit from the poor. You extort unjust gain from your neighbors.(AA) And you have forgotten(AB) me, declares the Sovereign Lord.(AC)

13 “‘I will surely strike my hands(AD) together at the unjust gain(AE) you have made and at the blood(AF) you have shed in your midst.(AG) 14 Will your courage endure(AH) or your hands(AI) be strong in the day I deal with you? I the Lord have spoken,(AJ) and I will do it.(AK) 15 I will disperse you among the nations and scatter(AL) you through the countries; and I will put an end to(AM) your uncleanness.(AN) 16 When you have been defiled[a] in the eyes of the nations, you will know that I am the Lord.’”

17 Then the word of the Lord came to me: 18 “Son of man, the people of Israel have become dross(AO) to me; all of them are the copper, tin, iron and lead left inside a furnace.(AP) They are but the dross of silver.(AQ) 19 Therefore this is what the Sovereign Lord says: ‘Because you have all become dross,(AR) I will gather you into Jerusalem. 20 As silver, copper, iron, lead and tin are gathered into a furnace to be melted with a fiery blast, so will I gather you in my anger and my wrath and put you inside the city and melt you.(AS) 21 I will gather you and I will blow(AT) on you with my fiery wrath, and you will be melted inside her.(AU) 22 As silver is melted(AV) in a furnace, so you will be melted inside her, and you will know that I the Lord have poured out my wrath(AW) on you.’”(AX)

23 Again the word of the Lord came to me: 24 “Son of man, say to the land, ‘You are a land that has not been cleansed or rained on in the day of wrath.’(AY) 25 There is a conspiracy(AZ) of her princes[b] within her like a roaring lion(BA) tearing its prey; they devour people,(BB) take treasures and precious things and make many widows(BC) within her. 26 Her priests do violence to my law(BD) and profane my holy things; they do not distinguish between the holy and the common;(BE) they teach that there is no difference between the unclean and the clean;(BF) and they shut their eyes to the keeping of my Sabbaths, so that I am profaned(BG) among them.(BH) 27 Her officials(BI) within her are like wolves(BJ) tearing their prey; they shed blood and kill people(BK) to make unjust gain.(BL) 28 Her prophets whitewash(BM) these deeds for them by false visions and lying divinations.(BN) They say, ‘This is what the Sovereign Lord says’—when the Lord has not spoken.(BO) 29 The people of the land practice extortion and commit robbery;(BP) they oppress the poor and needy and mistreat the foreigner,(BQ) denying them justice.(BR)

30 “I looked for someone among them who would build up the wall(BS) and stand before me in the gap on behalf of the land so I would not have to destroy it, but I found no one.(BT) 31 So I will pour out my wrath on them and consume them with my fiery anger,(BU) bringing down(BV) on their own heads all they have done, declares the Sovereign Lord.(BW)

Footnotes

  1. Ezekiel 22:16 Or When I have allotted you your inheritance
  2. Ezekiel 22:25 Septuagint; Hebrew prophets