Ezekieli 15
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Yerusalemu, Mtengo Wamphesa Wosabereka
15 Yehova anayankhulanso nane kuti, 2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse. 3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo? 4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse? 5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu. 7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’ ”
Ezekiel 15
New International Version
Jerusalem as a Useless Vine
15 The word of the Lord came to me: 2 “Son of man, how is the wood of a vine(A) different from that of a branch from any of the trees in the forest? 3 Is wood ever taken from it to make anything useful?(B) Do they make pegs(C) from it to hang things on? 4 And after it is thrown on the fire as fuel and the fire burns both ends and chars the middle, is it then useful for anything?(D) 5 If it was not useful for anything when it was whole, how much less can it be made into something useful when the fire has burned it and it is charred?
6 “Therefore this is what the Sovereign Lord says: As I have given the wood of the vine among the trees of the forest as fuel for the fire, so will I treat the people living in Jerusalem. 7 I will set my face against(E) them. Although they have come out of the fire(F), the fire will yet consume them. And when I set my face against them, you will know that I am the Lord.(G) 8 I will make the land desolate(H) because they have been unfaithful,(I) declares the Sovereign Lord.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.