Add parallel Print Page Options

Yerusalemu, Mtengo Wamphesa Wosabereka

15 Yehova anayankhulanso nane kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse. Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo? Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse? Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?

“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu. Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Jerusalem as a Useless Vine

15 The word of the Lord came to me: “Son of man, how is the wood of a vine(A) different from that of a branch from any of the trees in the forest? Is wood ever taken from it to make anything useful?(B) Do they make pegs(C) from it to hang things on? And after it is thrown on the fire as fuel and the fire burns both ends and chars the middle, is it then useful for anything?(D) If it was not useful for anything when it was whole, how much less can it be made into something useful when the fire has burned it and it is charred?

“Therefore this is what the Sovereign Lord says: As I have given the wood of the vine among the trees of the forest as fuel for the fire, so will I treat the people living in Jerusalem. I will set my face against(E) them. Although they have come out of the fire(F), the fire will yet consume them. And when I set my face against them, you will know that I am the Lord.(G) I will make the land desolate(H) because they have been unfaithful,(I) declares the Sovereign Lord.”