Add parallel Print Page Options

Kalata ya Tatenai Yopita kwa Dariyo

Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo. Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.

Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?” Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?” Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.

Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo Analemba kalatayo motere:

Kwa mfumu Dariyo:

Mukhale ndi mtendere wonse.

Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.

Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?” 10 Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.

11 Yankho limene anatipatsa ndi ili:

“Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo. 12 Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.

13 “Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso. 14 Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa. 15 Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’

16 “Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”

17 Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.

Tattenai’s Letter to Darius

Now Haggai(A) the prophet and Zechariah(B) the prophet, a descendant of Iddo, prophesied(C) to the Jews in Judah and Jerusalem in the name of the God of Israel, who was over them. Then Zerubbabel(D) son of Shealtiel and Joshua(E) son of Jozadak set to work(F) to rebuild the house of God in Jerusalem. And the prophets of God were with them, supporting them.

At that time Tattenai,(G) governor of Trans-Euphrates, and Shethar-Bozenai(H) and their associates went to them and asked, “Who authorized you to rebuild this temple and to finish it?”(I) They[a] also asked, “What are the names of those who are constructing this building?” But the eye of their God(J) was watching over the elders of the Jews, and they were not stopped until a report could go to Darius and his written reply be received.

This is a copy of the letter that Tattenai, governor of Trans-Euphrates, and Shethar-Bozenai and their associates, the officials of Trans-Euphrates, sent to King Darius. The report they sent him read as follows:

To King Darius:

Cordial greetings.

The king should know that we went to the district of Judah, to the temple of the great God. The people are building it with large stones and placing the timbers in the walls. The work(K) is being carried on with diligence and is making rapid progress under their direction.

We questioned the elders and asked them, “Who authorized you to rebuild this temple and to finish it?”(L) 10 We also asked them their names, so that we could write down the names of their leaders for your information.

11 This is the answer they gave us:

“We are the servants of the God of heaven and earth, and we are rebuilding the temple(M) that was built many years ago, one that a great king of Israel built and finished. 12 But because our ancestors angered(N) the God of heaven, he gave them into the hands of Nebuchadnezzar the Chaldean, king of Babylon, who destroyed this temple and deported the people to Babylon.(O)

13 “However, in the first year of Cyrus king of Babylon, King Cyrus issued a decree(P) to rebuild this house of God. 14 He even removed from the temple[b] of Babylon the gold and silver articles of the house of God, which Nebuchadnezzar had taken from the temple in Jerusalem and brought to the temple[c] in Babylon.(Q) Then King Cyrus gave them to a man named Sheshbazzar,(R) whom he had appointed governor, 15 and he told him, ‘Take these articles and go and deposit them in the temple in Jerusalem. And rebuild the house of God on its site.’

16 “So this Sheshbazzar came and laid the foundations of the house of God(S) in Jerusalem. From that day to the present it has been under construction but is not yet finished.”

17 Now if it pleases the king, let a search be made in the royal archives(T) of Babylon to see if King Cyrus did in fact issue a decree to rebuild this house of God in Jerusalem. Then let the king send us his decision in this matter.

Footnotes

  1. Ezra 5:4 See Septuagint; Aramaic We.
  2. Ezra 5:14 Or palace
  3. Ezra 5:14 Or palace