Add parallel Print Page Options

Bezaleli ndi Oholiabu

31 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Taona, ndasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda. Ndipo ndamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi: Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa, kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja. Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi: Kupanga tenti ya msonkhano, bokosi laumboni pamodzi ndi chophimbira chake, ndiponso zonse za mu tenti, tebulo ndi zida zake, choyikapo nyale cha golide wabwino kwambiri ndi ziwiya zake zonse, guwa lofukizirapo lubani, guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, beseni ndi nsichi yake, 10 ndiponso zovala zonse zolukidwa, zovala zopatulika za Aaroni wansembe pamodzi ndi za ana ake, zovala pamene akutumikira monga ansembe, 11 ndiponso mafuta odzozera ndi lubani wonunkhira wa ku malo opatulika. Iwo azipanga monga momwe Ine ndinakulamulira.”

Za Sabata

12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, 13 “Uza ana a Israeli kuti azisunga Masabata anga. Ichi chidzakhala chizindikiro pakati pa inu ndi Ine pamodzi ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo, chosonyeza kuti Ine ndine amene ndimakuyeretsani.

14 “Motero muzisunga tsiku la Sabata chifukwa ndi loyera kwa inu. Aliyense amene adetsa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake. 15 Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa. 16 Aisraeli onse komanso zidzukulu zawo mʼtsogolo azidzasunga tsiku la Sabata ngati pangano lamuyaya. 17 Tsiku la Sabata lidzakhala chizindikiro chamuyaya pakati pa Ine ndi Aisraeli chosonyeza kuti Yehova analenga za kumwamba ndi dziko lapansi kwa masiku asanu ndi limodzi ndi kuti pa tsiku lachisanu ndi chiwiri analeka kugwira ntchito napumula.”

18 Yehova atamaliza kuyankhula ndi Mose pa phiri la Sinai, anamupatsa Mose miyala iwiri yaumboni, imene Mulungu analembapo ndi chala chake.

Bezalel and Oholiab(A)

31 Then the Lord said to Moses, “See, I have chosen Bezalel(B) son of Uri, the son of Hur,(C) of the tribe of Judah, and I have filled him with the Spirit of God, with wisdom, with understanding, with knowledge(D) and with all kinds of skills(E) to make artistic designs for work in gold, silver and bronze, to cut and set stones, to work in wood, and to engage in all kinds of crafts. Moreover, I have appointed Oholiab(F) son of Ahisamak, of the tribe of Dan,(G) to help him. Also I have given ability to all the skilled workers(H) to make everything I have commanded you: the tent of meeting,(I) the ark of the covenant law(J) with the atonement cover(K) on it, and all the other furnishings of the tent— the table(L) and its articles, the pure gold lampstand(M) and all its accessories, the altar of incense,(N) the altar of burnt offering(O) and all its utensils, the basin(P) with its stand— 10 and also the woven garments(Q), both the sacred garments for Aaron the priest and the garments for his sons when they serve as priests, 11 and the anointing oil(R) and fragrant incense(S) for the Holy Place. They are to make them just as I commanded(T) you.”

The Sabbath

12 Then the Lord said to Moses, 13 “Say to the Israelites, ‘You must observe my Sabbaths.(U) This will be a sign(V) between me and you for the generations to come,(W) so you may know that I am the Lord, who makes you holy.(X)

14 “‘Observe the Sabbath, because it is holy to you. Anyone who desecrates it is to be put to death;(Y) those who do any work on that day must be cut off from their people. 15 For six days work(Z) is to be done, but the seventh day is a day of sabbath rest,(AA) holy to the Lord. Whoever does any work on the Sabbath day is to be put to death. 16 The Israelites are to observe the Sabbath,(AB) celebrating it for the generations to come as a lasting covenant. 17 It will be a sign(AC) between me and the Israelites forever, for in six days the Lord made the heavens and the earth, and on the seventh day he rested and was refreshed.(AD)’”(AE)

18 When the Lord finished speaking to Moses on Mount Sinai,(AF) he gave him the two tablets of the covenant law, the tablets of stone(AG) inscribed by the finger of God.(AH)