Add parallel Print Page Options

Guwa Lansembe Yofukiza

30 Upange guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Likhale lofanana mbali zonse. Mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91. Nyanga zake zipangidwe kumodzi ndi guwalo. Ukute guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse zinayi, pamodzi ndi nyanga zake. Ndipo upange mkombero wagolide kuzungulira guwalo. Upange mphete ziwiri zagolide ndipo uzilumikize ku guwa mʼmunsi mwa mkombero, mphete ziwiri ku mbali zonse ziwiri zoyangʼanana. Mphetozo zizigwira nsichi zonyamulira guwalo. Upange mizati yamtengo wa mkesha ndipo uyikute ndi golide. Uyike guwalo patsogolo pa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano. Apa ndi pamene ndizidzakumana nawe.

“Aaroni ayenera kumafukiza lubani wonunkhira pa guwalo mmawa uliwonse. Pamene akukonza nyale zija afukizenso lubani. Aaroni ayenera kufukizanso lubani pamene ayatsa nyale madzulo kuti lubani akhale akuyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova kwa mibado imene ikubwera. Pa guwapo usafukize lubani wachilendo kapena kuperekapo nsembe yopsereza kapena nsembe yaufa. Usathire pa guwapo ngakhale nsembe yachakumwa. 10 Aaroni azidzapereka nsembe yopepesera machimo pa nyanga za guwalo kamodzi pa chaka. Mwambowu uzidzachitika pogwiritsa ntchito magazi a nsembe yopepesera machimo, ndipo zizidzachitika mʼmibado yanu yonse. Choncho guwa lansembelo lidzakhala loyera ndi loperekedwa kwa Yehova.”

Za Chopereka Chowombolera Moyo

11 Ndipo Yehova anati kwa Mose, 12 “Pamene ukuchita kalembera wa Aisraeli, munthu aliyense ayenera kupereka kwa Yehova chowombolera moyo wake pamene akuwerengedwa. Motero mliri sudzabwera pa iwo pamene ukuwawerenga. 13 Izi ndi zimene aliyense wolembedwa mu kawundula ayenera kupereka: theka la sekeli, kutanthauza ndalama zolemera magalamu asanu ndi limodzi malingana ndi kawerengedwe ka ndalama za ku Nyumba ya Mulungu. Paja sekeli imodzi ikulingana ndi magera makumi awiri. Theka la sekeli chidzakhala chopereka cha kwa Yehova. 14 Aliyense wolembedwa mu kawundula amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira ayenera kupereka chopereka kwa Yehova. 15 Anthu olemera asapereke koposa theka la sekeli ndipo osauka asapereke kuchepera theka la sekeli pamene mukupereka nsembe kwa Yehova yowombolera miyoyo yanu. 16 Ulandire ndalama zopepeserazo kuchokera kwa Aisraeli ndipo zigwiritsidwe ntchito ya ku tenti ya msonkhano. Zoperekazi zidzakhala chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova, ndiponso zowombolera miyoyo yanu.”

Za Beseni Losambira

17 Ndipo Yehova anati kwa Mose, 18 “Upange beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso. Uliyike pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uthiremo madzi. 19 Aaroni ndi ana ake azisamba mʼmanja ndi kutsuka mapazi awo ndi madzi amenewo. 20 Pamene akulowa mu tenti ya msonkhano, iwo asambe madziwa kuti asafe. Ndiponso pamene akupita kukatumikira ku guwa lansembe ndi kupereka nsembe yopsereza kwa Yehova, 21 azisamba mʼmanja mwawo ndi kutsuka mapazi kuti asadzafe. Limeneli ndi lamulo limene Aaroni, pamodzi ndi ana ndi zidzukulu zake mʼtsogolomo ayenera kumadzalitsatira mpaka muyaya.”

Mafuta Wodzozera

22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, 23 “Utenge zonunkhira bwino kwambiri izi: makilogalamu asanu ndi limodzi a mure wamadzi, makilogalamu atatu a zonunkhira bwino za mtundu wa sinamoni, makilogalamu atatu a nzimbe yonunkhira bwino kwambiri, 24 makilogalamu asanu ndi limodzi a mkesha. Zonsezi zikhale malingana ndi muyeso wa ku Nyumba ya Mulungu. Pakhalenso malita anayi a mafuta a olivi. 25 Ugwiritse ntchito zinthu zimenezi kupanga mafuta opatulika odzozera, mafuta onunkhira, apangidwe ndi mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa. Awa adzakhala mafuta opatulika odzozera. 26 Tsono uwagwiritse ntchito podzoza tenti ya msonkhano, Bokosi la Chipangano, 27 tebulo, ndi ziwiya zake zonse, choyikapo nyale ndi zipangizo zake, guwa lofukizirapo lubani, 28 guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso beseni pamodzi ndi nsichi yake. 29 Zonsezi uzipatule kuti zidzakhale zopatulika, ndipo chilichonse chimene chidzakhudza zimenezi chidzakhala chopatulika.

30 “Udzoze Aaroni ndi ana ake aamuna ndi kuwapatula kuti akhale ansembe onditumikira. 31 Tsono awuze a Israeli kuti, mafuta wodzozera awa adzakhala wopatulika mpaka muyaya. 32 Musadzadzozere munthu wamba mafuta amenewa, ndipo musadzapange mafuta wofanana ndi amenewa. Mafutawa ndi wopatulika ndipo akhale woyera kwa inu. 33 Wina aliyense amene adzapanga mafuta wonunkhira wofanana nawo kapena kudzozera mafutawa munthu wamba osati wansembe ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”

Za Zofukiza

34 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tenga muyeso wofanana wa zinthu zonunkhira izi: sitakate, onika, galibanumu pamodzi ndi lubani weniweni. 35 Uziphatikize pamodzi zonsezi ndi kupanga lubani monga amachitira mmisiri wopanga zonunkhira. Athire mchere ndipo akhale woyera ndi wopatulika. 36 Upere gawo lina mosalala kwambiri ndipo utapepo pangʼono ndi kuyika patsogolo pa Bokosi la Chipangano mu tenti ya msonkhano, kumene ine ndidzakumane nawe. Lubani ameneyu kwa inu adzakhala wopatulika kwambiri. 37 Musapange lubani wanu potsatira njira iyi. Lubani yense wopangidwa mwa njira iyi akhale wopatulika, woperekedwa kwa Yehova. 38 Aliyense amene adzapanga wofanana naye kuti asangalale ndi fungo lake ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”

The Altar of Incense(A)

30 “Make an altar(B) of acacia wood for burning incense.(C) It is to be square, a cubit long and a cubit wide, and two cubits high[a]—its horns(D) of one piece with it. Overlay the top and all the sides and the horns with pure gold, and make a gold molding around it.(E) Make two gold rings(F) for the altar below the molding—two on each of the opposite sides—to hold the poles used to carry it. Make the poles of acacia wood and overlay them with gold.(G) Put the altar in front of the curtain that shields the ark of the covenant law—before the atonement cover(H) that is over the tablets of the covenant law—where I will meet with you.

“Aaron must burn fragrant incense(I) on the altar every morning when he tends the lamps. He must burn incense again when he lights the lamps at twilight so incense will burn regularly before the Lord for the generations to come.(J) Do not offer on this altar any other incense(K) or any burnt offering or grain offering, and do not pour a drink offering on it. 10 Once a year(L) Aaron shall make atonement(M) on its horns. This annual atonement must be made with the blood of the atoning sin offering[b](N) for the generations to come.(O) It is most holy to the Lord.”

Atonement Money

11 Then the Lord said to Moses, 12 “When you take a census(P) of the Israelites to count them, each one must pay the Lord a ransom(Q) for his life at the time he is counted. Then no plague(R) will come on them when you number them. 13 Each one who crosses over to those already counted is to give a half shekel,[c] according to the sanctuary shekel,(S) which weighs twenty gerahs. This half shekel is an offering to the Lord. 14 All who cross over, those twenty years old or more,(T) are to give an offering to the Lord. 15 The rich are not to give more than a half shekel and the poor are not to give less(U) when you make the offering to the Lord to atone for your lives. 16 Receive the atonement(V) money from the Israelites and use it for the service of the tent of meeting.(W) It will be a memorial(X) for the Israelites before the Lord, making atonement for your lives.”

Basin for Washing

17 Then the Lord said to Moses, 18 “Make a bronze basin,(Y) with its bronze stand, for washing. Place it between the tent of meeting and the altar, and put water in it. 19 Aaron and his sons are to wash their hands and feet(Z) with water(AA) from it. 20 Whenever they enter the tent of meeting, they shall wash with water so that they will not die.(AB) Also, when they approach the altar to minister by presenting a food offering to the Lord, 21 they shall wash their hands and feet so that they will not die. This is to be a lasting ordinance(AC) for Aaron and his descendants for the generations to come.”(AD)

Anointing Oil

22 Then the Lord said to Moses, 23 “Take the following fine spices:(AE) 500 shekels[d] of liquid myrrh,(AF) half as much (that is, 250 shekels) of fragrant cinnamon,(AG) 250 shekels[e] of fragrant calamus,(AH) 24 500 shekels(AI) of cassia(AJ)—all according to the sanctuary shekel—and a hin[f] of olive oil. 25 Make these into a sacred anointing oil, a fragrant blend, the work of a perfumer.(AK) It will be the sacred anointing oil.(AL) 26 Then use it to anoint(AM) the tent of meeting, the ark of the covenant law, 27 the table and all its articles, the lampstand and its accessories, the altar of incense, 28 the altar of burnt offering and all its utensils, and the basin with its stand. 29 You shall consecrate them(AN) so they will be most holy, and whatever touches them will be holy.(AO)

30 “Anoint Aaron and his sons and consecrate(AP) them so they may serve me as priests.(AQ) 31 Say to the Israelites, ‘This is to be my sacred anointing oil(AR) for the generations to come.(AS) 32 Do not pour it on anyone else’s body and do not make any other oil using the same formula. It is sacred, and you are to consider it sacred.(AT) 33 Whoever makes perfume like it and puts it on anyone other than a priest must be cut off(AU) from their people.’”

Incense

34 Then the Lord said to Moses, “Take fragrant spices(AV)—gum resin, onycha and galbanum—and pure frankincense, all in equal amounts, 35 and make a fragrant blend of incense,(AW) the work of a perfumer.(AX) It is to be salted and pure and sacred. 36 Grind some of it to powder and place it in front of the ark of the covenant law in the tent of meeting, where I will meet(AY) with you. It shall be most holy(AZ) to you. 37 Do not make any incense with this formula for yourselves; consider it holy(BA) to the Lord. 38 Whoever makes incense like it to enjoy its fragrance must be cut off(BB) from their people.”

Footnotes

  1. Exodus 30:2 That is, about 1 1/2 feet long and wide and 3 feet high or about 45 centimeters long and wide and 90 centimeters high
  2. Exodus 30:10 Or purification offering
  3. Exodus 30:13 That is, about 1/5 ounce or about 5.8 grams; also in verse 15
  4. Exodus 30:23 That is, about 12 1/2 pounds or about 5.8 kilograms; also in verse 24
  5. Exodus 30:23 That is, about 6 1/4 pounds or about 2.9 kilograms
  6. Exodus 30:24 That is, probably about 1 gallon or about 3.8 liters