Add parallel Print Page Options

Kutsimikizira kwa Pangano

24 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali. Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”

Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.” Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena.

Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli. Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano. Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe. Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”

Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”

Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri, 10 ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo. 11 Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.

12 Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”

13 Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa. 14 Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”

15 Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo. 16 Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo. 17 Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo. 18 Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.

The Covenant Confirmed

24 Then the Lord said to Moses, “Come up to the Lord, you and Aaron,(A) Nadab and Abihu,(B) and seventy of the elders(C) of Israel. You are to worship at a distance, but Moses alone is to approach(D) the Lord; the others must not come near. And the people may not come up with him.”

When Moses went and told the people all the Lord’s words and laws,(E) they responded with one voice, “Everything the Lord has said we will do.”(F) Moses then wrote(G) down everything the Lord had said.

He got up early the next morning and built an altar(H) at the foot of the mountain and set up twelve stone pillars(I) representing the twelve tribes of Israel. Then he sent young Israelite men, and they offered burnt offerings(J) and sacrificed young bulls as fellowship offerings(K) to the Lord. Moses(L) took half of the blood(M) and put it in bowls, and the other half he splashed(N) against the altar. Then he took the Book of the Covenant(O) and read it to the people. They responded, “We will do everything the Lord has said; we will obey.”(P)

Moses then took the blood, sprinkled it on the people(Q) and said, “This is the blood of the covenant(R) that the Lord has made with you in accordance with all these words.”

Moses and Aaron, Nadab and Abihu, and the seventy elders(S) of Israel went up 10 and saw(T) the God of Israel. Under his feet was something like a pavement made of lapis lazuli,(U) as bright blue as the sky.(V) 11 But God did not raise his hand against these leaders of the Israelites; they saw(W) God, and they ate and drank.(X)

12 The Lord said to Moses, “Come up to me on the mountain and stay here, and I will give you the tablets of stone(Y) with the law and commandments I have written for their instruction.”

13 Then Moses set out with Joshua(Z) his aide, and Moses went up on the mountain(AA) of God. 14 He said to the elders, “Wait here for us until we come back to you. Aaron and Hur(AB) are with you, and anyone involved in a dispute(AC) can go to them.”

15 When Moses went up on the mountain, the cloud(AD) covered it, 16 and the glory(AE) of the Lord settled on Mount Sinai.(AF) For six days the cloud covered the mountain, and on the seventh day the Lord called to Moses from within the cloud.(AG) 17 To the Israelites the glory of the Lord looked like a consuming fire(AH) on top of the mountain. 18 Then Moses entered the cloud as he went on up the mountain. And he stayed on the mountain forty(AI) days and forty nights.(AJ)