Add parallel Print Page Options

Nyimbo ya Mose ndi Miriamu

15 Ndipo Mose ndi Aisraeli anayimbira Yehova nyimbo iyi:

“Ine ndidzayimbira Yehova
    pakuti wakwezeka mʼchigonjetso.
Kavalo ndi wokwera wake,
    Iye wawaponya mʼnyanja.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
    ndiye chipulumutso changa.
Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamutamanda,
    Mulungu wa makolo anga, ine ndidzamukweza.
Yehova ndi wankhondo;
    Yehova ndilo dzina lake.
Magaleta a Farao ndi asilikali ake ankhondo
    Iye wawaponya mʼnyanja.
Akatswiri ankhondo amphamvu a Farao
    amizidwa mʼNyanja Yofiira.
Nyanja yakuya inawaphimba;
    Iwo anamira pansi ngati mwala.”

Yehova, dzanja lanu lamanja
    ndi laulemerero chifukwa cha mphamvu zake.
Ndithu Yehova, dzanja lanu lamanja
    linaphwanya mdani.
Ndi ulemerero wanu waukulu,
    munagonjetsa okutsutsani.
Inu munatumiza mkwiyo wanu waukulu;
    ndipo unawapsereza ngati udzu.
Ndi mpweya wotuluka mʼmphuno mwanu
    madzi anawunjikana pamodzi.
Nyanja yakuya ija inasanduka
    madzi owuma gwaa kufika pansi.

Mdaniyo anati,
    “Ine ndidzawalondola, ndipo ndidzawagwira.
Ndidzagawa chuma chawo;
    ndiye chokhumba changa chidzakwaniritsidwa.
Ine ndidzasolola lupanga langa,
    ndi mkono wanga ndidzawawononga.”
10 Koma Inu munawuzira mphepo yanu,
    ndipo nyanja inawaphimba.
Iwo anamira ngati chitsulo
    mʼmadzi amphamvu.

11 Ndithu Yehova, pakati pa milungu,
    ndani afanana nanu? Inu amene muli woyera,
        ndiponso wotamandika wolemekezeka,
        chifukwa cha ntchito zanu,
        zazikulu ndi zodabwitsa?
12 Munatambasula dzanja lanu lamanja
    ndipo dziko linawameza.

13 Ndi chikondi chanu chosasinthika mudzatsogolera
    anthu amene munawawombola.
Ndi mphamvu zanu munawatsogolera
    ku malo anu woyera.
14 Anthu amitundu ina anamva za mbiriyi ndipo ananjenjemera ndi mantha,
    mantha woopsa agwira anthu a dziko la Filisiti.
15 Tsopano mafumu a ku Edomu agwidwa ndi mantha aakulu,
    otsogolera a dziko la Mowabu akunjenjemera ndi mantha,
ndipo anthu a ku Kanaani asungunuka ndi mantha.
16     Onse agwidwa ndi mantha woopsa.
Popeza anaona mphamvu zanu zazikulu,
    iwo ayima chilili ngati mwala mpaka anthu anu,
Inu Yehova atadutsa;
    inde mpaka atadutsa anthu amene munawagula.
17 Inu mudzawalowetsa ndi kuwakhazikitsa
    pa phiri lanu.
Pa malo pamene Inu Yehova munawapanga kuti muzikhalapo;
    malo wopatulika amene Inu Ambuye munawakonza ndi manja anu.
18 “Yehova adzalamula
    mpaka muyaya.”

19 Akavalo a Farao, magaleta ndi oyendetsa akavalo atalowa mʼnyanja, Yehova anawabwezera madziwo mʼnyanja ndi kuwamiza, koma Aisraeli anawoloka nyanjayo powuma. 20 Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina. 21 Miriamu anawayimbira nyimbo iyi:

“Imbirani Yehova,
    chifukwa iye wapambana.
Kavalo ndi wokwerapo wake
    Iye wawamiza mʼnyanja.”

Madzi a ku Mara ndi Elimu

22 Ndipo Mose anatsogolera Israeli kuchoka ku nyanja yofiira ndi kupita ku chipululu cha Suri. Anayenda mʼchipululu masiku atatu wosapeza madzi. 23 Ndipo anafika ku Mara. Koma sanathe kumwa madzi akumeneko chifukwa anali owawa. (Ndi chifukwa chake malowo amatchedwa Mara). 24 Tsono anthu aja anadandaulira Mose ndi kumufunsa kuti, “Kodi tikumwa chiyani?”

25 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anamuonetsa kamtengo. Iye anakaponya mʼmadzimo ndipo madzi anakhala abwino.

Kumeneko Yehova anawayikira lamulo ndi maweruziro. Kumenekonso Yehova anawayesa. 26 Yehova anati, “Ngati inu mudzamvetsa bwino mawu anga, kuchita zolungama, kumvera malamulo anga ndi kusamalitsa zimene ndikukuwuzani ndiye kuti Ine sindidzayika pa inu matenda amene ndinayika pa anthu a ku Igupto popeza ndine Yehova amene ndimakuchiritsani.”

27 Kenaka anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa makumi asanu ndi awiri, ndipo anamanga misasa yawo kumeneko pafupi ndi madzi.

The Song of Moses and Miriam

15 Then Moses and the Israelites sang this song(A) to the Lord:

“I will sing(B) to the Lord,
    for he is highly exalted.
Both horse and driver(C)
    he has hurled into the sea.(D)

“The Lord is my strength(E) and my defense[a];
    he has become my salvation.(F)
He is my God,(G) and I will praise him,
    my father’s God, and I will exalt(H) him.
The Lord is a warrior;(I)
    the Lord is his name.(J)
Pharaoh’s chariots and his army(K)
    he has hurled into the sea.
The best of Pharaoh’s officers
    are drowned in the Red Sea.[b]
The deep waters(L) have covered them;
    they sank to the depths like a stone.(M)
Your right hand,(N) Lord,
    was majestic in power.
Your right hand,(O) Lord,
    shattered(P) the enemy.

“In the greatness of your majesty(Q)
    you threw down those who opposed you.
You unleashed your burning anger;(R)
    it consumed(S) them like stubble.
By the blast of your nostrils(T)
    the waters piled up.(U)
The surging waters stood up like a wall;(V)
    the deep waters congealed in the heart of the sea.(W)
The enemy boasted,
    ‘I will pursue,(X) I will overtake them.
I will divide the spoils;(Y)
    I will gorge myself on them.
I will draw my sword
    and my hand will destroy them.’
10 But you blew with your breath,(Z)
    and the sea covered them.
They sank like lead
    in the mighty waters.(AA)
11 Who among the gods
    is like you,(AB) Lord?
Who is like you—
    majestic in holiness,(AC)
awesome in glory,(AD)
    working wonders?(AE)

12 “You stretch out(AF) your right hand,
    and the earth swallows your enemies.(AG)
13 In your unfailing love you will lead(AH)
    the people you have redeemed.(AI)
In your strength you will guide them
    to your holy dwelling.(AJ)
14 The nations will hear and tremble;(AK)
    anguish(AL) will grip the people of Philistia.(AM)
15 The chiefs(AN) of Edom(AO) will be terrified,
    the leaders of Moab will be seized with trembling,(AP)
the people[c] of Canaan will melt(AQ) away;
16     terror(AR) and dread will fall on them.
By the power of your arm
    they will be as still as a stone(AS)
until your people pass by, Lord,
    until the people you bought[d](AT) pass by.(AU)
17 You will bring(AV) them in and plant(AW) them
    on the mountain(AX) of your inheritance—
the place, Lord, you made for your dwelling,(AY)
    the sanctuary,(AZ) Lord, your hands established.

18 “The Lord reigns
    for ever and ever.”(BA)

19 When Pharaoh’s horses, chariots and horsemen[e] went into the sea,(BB) the Lord brought the waters of the sea back over them, but the Israelites walked through the sea on dry ground.(BC) 20 Then Miriam(BD) the prophet,(BE) Aaron’s sister, took a timbrel in her hand, and all the women followed her, with timbrels(BF) and dancing.(BG) 21 Miriam sang(BH) to them:

“Sing to the Lord,
    for he is highly exalted.
Both horse and driver(BI)
    he has hurled into the sea.”(BJ)

The Waters of Marah and Elim

22 Then Moses led Israel from the Red Sea and they went into the Desert(BK) of Shur.(BL) For three days they traveled in the desert without finding water.(BM) 23 When they came to Marah, they could not drink its water because it was bitter. (That is why the place is called Marah.[f](BN)) 24 So the people grumbled(BO) against Moses, saying, “What are we to drink?”(BP)

25 Then Moses cried out(BQ) to the Lord, and the Lord showed him a piece of wood. He threw(BR) it into the water, and the water became fit to drink.

There the Lord issued a ruling and instruction for them and put them to the test.(BS) 26 He said, “If you listen carefully to the Lord your God and do what is right in his eyes, if you pay attention to his commands and keep(BT) all his decrees,(BU) I will not bring on you any of the diseases(BV) I brought on the Egyptians, for I am the Lord, who heals(BW) you.”

27 Then they came to Elim, where there were twelve springs and seventy palm trees, and they camped(BX) there near the water.

Footnotes

  1. Exodus 15:2 Or song
  2. Exodus 15:4 Or the Sea of Reeds; also in verse 22
  3. Exodus 15:15 Or rulers
  4. Exodus 15:16 Or created
  5. Exodus 15:19 Or charioteers
  6. Exodus 15:23 Marah means bitter.