Add parallel Print Page Options

Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli

33 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. Iye anati:

“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai
    ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;
    anawala kuchokera pa Phiri la Parani.
Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo
    kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;
    opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.
Onse amagwada pansi pa mapazi anu
    kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
malamulo amene Mose anatipatsa,
    chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
Iye anali mfumu ya Yesuruni
    pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,
    pamodzi ndi mafuko a Israeli.

“Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,
    anthu ake asachepe pa chiwerengero.”

Ndipo ponena za Yuda anati:

“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;
    mubweretseni kwa anthu ake.
Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.
    Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”

Za fuko la Alevi anati:

“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za
    mtumiki wanu wokhulupirika.
Munamuyesa ku Masa;
    munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,
    ‘Sindilabadira za iwo.’
Sanasamale za abale ake
    kapena ana ake,
koma anayangʼanira mawu anu
    ndipo anateteza pangano lanu.
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu
    ndi malamulo anu kwa Israeli.
Amafukiza lubani pamaso panu
    ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse
    ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.
Menyani adani awo mʼchiwuno
    kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”

12 Za fuko la Benjamini anati:

“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,
    pakuti amamuteteza tsiku lonse,
    ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”

13 Za fuko la Yosefe anati:

“Yehova adalitse dziko lake
    ndi mame ambiri ochokera kumwamba
    ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa
    ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa
    ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo
    ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.
Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,
    wapaderadera pakati pa abale ake.
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;
    nyanga zake zili ngati za njati.
Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,
    ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.
Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;
    nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”

18 Za fuko la Zebuloni anati:

“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,
    ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,
    kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;
kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,
    chuma chobisika mu mchenga.”

20 Za fuko la Gadi anati:

“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!
    Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,
    kukhadzula mkono kapena mutu.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;
    gawo la mtsogoleri anasungira iye.
Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,
    anachita chifuniro cha Yehova molungama,
    ndiponso malamulo onena za Israeli.”

22 Za fuko la Dani anati:

“Dani ndi mwana wamkango,
    amene akutuluka ku Basani.”

23 Za fuko la Nafutali anati:

“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova
    ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;
    cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”

24 Za fuko la Aseri anati:

“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;
    abale ake amukomere mtima,
    ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,
    ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.

26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,
    amene amakwera pa thambo kukuthandizani
    ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,
    ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.
Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,
    adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;
    zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere
mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,
    kumene thambo limagwetsa mame.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala!
    Wofanana nanu ndani
    anthu opulumutsidwa ndi Yehova?
Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu
    ndi lupanga lanu la ulemerero.
Adani ako adzakugonjera,
    ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”

Moses Blesses the Tribes(A)

33 This is the blessing(B) that Moses the man of God(C) pronounced on the Israelites before his death. He said:

“The Lord came from Sinai(D)
    and dawned over them from Seir;(E)
    he shone forth(F) from Mount Paran.(G)
He came with[a] myriads of holy ones(H)
    from the south, from his mountain slopes.[b]
Surely it is you who love(I) the people;
    all the holy ones are in your hand.(J)
At your feet they all bow down,(K)
    and from you receive instruction,
the law that Moses gave us,(L)
    the possession of the assembly of Jacob.(M)
He was king(N) over Jeshurun[c](O)
    when the leaders of the people assembled,
    along with the tribes of Israel.

“Let Reuben live and not die,
    nor[d] his people be few.”(P)

And this he said about Judah:(Q)

“Hear, Lord, the cry of Judah;
    bring him to his people.
With his own hands he defends his cause.
    Oh, be his help against his foes!”

About Levi(R) he said:

“Your Thummim and Urim(S) belong
    to your faithful servant.(T)
You tested(U) him at Massah;
    you contended with him at the waters of Meribah.(V)
He said of his father and mother,(W)
    ‘I have no regard for them.’
He did not recognize his brothers
    or acknowledge his own children,
but he watched over your word
    and guarded your covenant.(X)
10 He teaches(Y) your precepts to Jacob
    and your law to Israel.(Z)
He offers incense before you(AA)
    and whole burnt offerings on your altar.(AB)
11 Bless all his skills, Lord,
    and be pleased with the work of his hands.(AC)
Strike down those who rise against him,
    his foes till they rise no more.”

12 About Benjamin(AD) he said:

“Let the beloved of the Lord rest secure in him,(AE)
    for he shields him all day long,(AF)
    and the one the Lord loves(AG) rests between his shoulders.(AH)

13 About Joseph(AI) he said:

“May the Lord bless his land
    with the precious dew from heaven above
    and with the deep waters that lie below;(AJ)
14 with the best the sun brings forth
    and the finest the moon can yield;
15 with the choicest gifts of the ancient mountains(AK)
    and the fruitfulness of the everlasting hills;
16 with the best gifts of the earth and its fullness
    and the favor of him who dwelt in the burning bush.(AL)
Let all these rest on the head of Joseph,
    on the brow of the prince among[e] his brothers.(AM)
17 In majesty he is like a firstborn bull;
    his horns(AN) are the horns of a wild ox.(AO)
With them he will gore(AP) the nations,
    even those at the ends of the earth.
Such are the ten thousands of Ephraim;(AQ)
    such are the thousands of Manasseh.(AR)

18 About Zebulun(AS) he said:

“Rejoice, Zebulun, in your going out,
    and you, Issachar,(AT) in your tents.
19 They will summon peoples to the mountain(AU)
    and there offer the sacrifices of the righteous;(AV)
they will feast on the abundance of the seas,(AW)
    on the treasures hidden in the sand.”

20 About Gad(AX) he said:

“Blessed is he who enlarges Gad’s domain!(AY)
    Gad lives there like a lion,
    tearing at arm or head.
21 He chose the best land for himself;(AZ)
    the leader’s portion was kept for him.(BA)
When the heads of the people assembled,
    he carried out the Lord’s righteous will,(BB)
    and his judgments concerning Israel.”

22 About Dan(BC) he said:

“Dan is a lion’s cub,
    springing out of Bashan.”

23 About Naphtali(BD) he said:

“Naphtali is abounding with the favor of the Lord
    and is full of his blessing;
    he will inherit southward to the lake.”

24 About Asher(BE) he said:

“Most blessed of sons is Asher;
    let him be favored by his brothers,
    and let him bathe his feet in oil.(BF)
25 The bolts of your gates will be iron and bronze,(BG)
    and your strength will equal your days.(BH)

26 “There is no one like the God of Jeshurun,(BI)
    who rides(BJ) across the heavens to help you(BK)
    and on the clouds(BL) in his majesty.(BM)
27 The eternal(BN) God is your refuge,(BO)
    and underneath are the everlasting(BP) arms.
He will drive out your enemies before you,(BQ)
    saying, ‘Destroy them!’(BR)
28 So Israel will live in safety;(BS)
    Jacob will dwell[f] secure
in a land of grain and new wine,
    where the heavens drop dew.(BT)
29 Blessed are you, Israel!(BU)
    Who is like you,(BV)
    a people saved by the Lord?(BW)
He is your shield and helper(BX)
    and your glorious sword.
Your enemies will cower before you,
    and you will tread on their heights.(BY)

Footnotes

  1. Deuteronomy 33:2 Or from
  2. Deuteronomy 33:2 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
  3. Deuteronomy 33:5 Jeshurun means the upright one, that is, Israel; also in verse 26.
  4. Deuteronomy 33:6 Or but let
  5. Deuteronomy 33:16 Or of the one separated from
  6. Deuteronomy 33:28 Septuagint; Hebrew Jacob’s spring is