Add parallel Print Page Options

Kugonjetsedwa kwa Ogi Mfumu ya ku Basani

Kenaka tinakhota ndi kumayenda mokwera mtunda ndi njira yolowera ku Basani. Ndipo Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anakumana nafe ndipo anamenyana nafe ku Ederi. Yehova anati kwa ine, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”

Choncho Yehova Mulungu wathu anapereka mʼmanja mwathu Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo. Tinawakantha onsewo osasiya ndi mmodzi yemwe. Pa nthawi imeneyo tinatenga mizinda yake yonse. Pa mizinda 60, panalibe ndi umodzi womwe umene sitinawalande, mʼdera lonse la ufumu wa Ogi ku Basani chimene ndi chigawo cha Arigobu. Mizinda yonseyi inali yotetezedwa ndi malinga ataliatali wokhala ndi zitseko ndi zitsulo, komabe panali midzi ina yambiri imene inalibe malinga. Tinawawonongeratu monga momwe tinachitira Sihoni, mfumu ya ku Hesiboni. Tinawononga mzinda uliwonse, amayi, amuna ndi ana omwe. Koma tinafunkha ziweto ndi katundu wawo yense.

Choncho pa nthawi imeneyi tinalanda kwa mafumu awiri Aamori, dera la kummawa kwa Yorodani, kuyambira ku khwawa la Arinoni mpaka ku Phiri la Herimoni. (Asidoni amatcha Herimoni kuti Siriyoni, pamene Aamori amalitcha Seniri). 10 Tinalanda mizinda yonse ya ku mapiri, ku Giliyadi, Basani mpaka ku Saleka ndi Ederi, mizinda ya mu ufumu wa Ogi wa ku Basani. 11 (Ogi, mfumu ya ku Basani, anali yekhayo amene anatsala mwa mtundu wa anthu ataliatali a Chirefai. Bedi lake linali lachitsulo ndipo lalitali kuposa mamita anayi. Mulifupi mwake munali mamita awiri. Bedilo likanalipo ku Raba kwa Aamori).

Kugawana Dziko

12 Dziko limene tinalanda nthawi imeneyo, ndinapatsa fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi dera la kumpoto kwa Aroeri cha mʼmphepete mwa khwawa la Arinoni kuphatikizapo theka la dziko lamapiri la Giliyadi ndi mizinda yake. 13 Theka la fuko la Manase ndinalipatsa dziko lonse lotsala la Giliyadi ndi Basani yense yemwe ndi dera la ufumu wa Ogi. (Chigawo chonse cha Arigobu mu Basani chinkadziwika kuti ndi dziko la Arefai. 14 Yairi, mdzukulu wa Manase, anatenga chigawo chonse cha Arigobu mpaka ku malire a Agesuri ndi Amaakati. Anatcha chigawochi dzina lake, moti mpaka lero Basani amatchedwa Havoti Yairi). 15 Ndipo ndinapereka Giliyadi kwa Makiri. 16 Koma kwa fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi ndinapereka chigawo chochokera ku Giliyadi kutsetsereka mpaka ku khwawa la Arinoni (pakati pa khwawalo ndiye panali malire) ndi kupitirira mpaka ku mtsinje wa Yaboki umene ndi malire Aamoni. 17 Malire ake a chakumadzulo anali Yorodani ku Araba, kuchokera ku Kinereti mpaka ku Nyanja ya Araba (Nyanja ya Mchere), mʼmunsi mwa matsitso a Pisiga.

18 Ndinakulamulirani nthawi imene ija kuti, “Yehova Mulungu wanu wakupatsani dziko ili kuti likhale lanu. Koma amuna amphamvu onse ali ndi zida zankhondo, awoloke kutsogolera abale anu Aisraeli. 19 Koma akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu (ndikudziwa kuti muli ndi ziweto zambiri) zikhoza kumakhalabe mʼmizinda imene ndakupatsani, 20 mpaka Yehova atapereka mpumulo kwa abale anu, nawonso atatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa patsidya pa Yorodani, monga wachitira ndi inu. Kenaka, aliyense wa inu akhoza kudzabwerera ku dziko limene ndinakupatsani.”

Mose Aletsedwa Kuwoloka Yorodani

21 Nthawi imeneyo ndinamulamula Yoswa kuti, “Waona wekha ndi maso ako zonse zimene Yehova Mulungu wako anachitira mafumu awiriwa. Yehova adzachita zomwezo ndi mafumu ena onse kumene mukupitako. 22 Musawaope chifukwa Yehova Mulungu mwini adzakumenyerani nkhondo.”

23 Nthawi imeneyo ndinachonderera Yehova kuti, 24 “Ambuye Mulungu, mwayamba tsopano kuonetsa mtumiki wanu ukulu wanu ndi dzanja lanu lamphamvu. Ndi mulungu uti ali kumwamba kapena pa dziko lapansi amene angachite ntchito zozizwitsa zimene mumachita? 25 Mundilole ndipite ndi kukaona dziko labwinolo kutsidya kwa Yorodani dziko la mapiri abwinowo ndi Lebanoni.”

26 Koma chifukwa cha inu, Yehova anakwiya nane osandimvera. Yehova anati, “Basi pakwana, usayankhulenso ndi ine zimenezi. 27 Pita pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo uyangʼane kumadzulo, kumpoto, kummwera ndi kummawa. Ulione dzikolo ndi maso ako pakuti suwoloka Yorodaniyu. 28 Koma langiza Yoswa ndipo umulimbikitse ndi kumupatsa mphamvu pakuti adzatsogolera anthu awa kuwoloka ndipo adzawathandiza kuti atenge dziko limene ulioneli.” 29 Ndipo tinakhala mʼchigwa pafupi ndi Beti-Peori.

Defeat of Og King of Bashan

Next we turned and went up along the road toward Bashan, and Og king of Bashan(A) with his whole army marched out to meet us in battle at Edrei.(B) The Lord said to me, “Do not be afraid(C) of him, for I have delivered him into your hands, along with his whole army and his land. Do to him what you did to Sihon king of the Amorites, who reigned in Heshbon.”

So the Lord our God also gave into our hands Og king of Bashan and all his army. We struck them down,(D) leaving no survivors.(E) At that time we took all his cities.(F) There was not one of the sixty cities that we did not take from them—the whole region of Argob, Og’s kingdom(G) in Bashan.(H) All these cities were fortified with high walls and with gates and bars, and there were also a great many unwalled villages. We completely destroyed[a] them, as we had done with Sihon king of Heshbon, destroying[b](I) every city—men, women and children. But all the livestock(J) and the plunder from their cities we carried off for ourselves.

So at that time we took from these two kings of the Amorites(K) the territory east of the Jordan, from the Arnon Gorge as far as Mount Hermon.(L) (Hermon is called Sirion(M) by the Sidonians; the Amorites call it Senir.)(N) 10 We took all the towns on the plateau, and all Gilead, and all Bashan as far as Salekah(O) and Edrei, towns of Og’s kingdom in Bashan. 11 (Og king of Bashan was the last of the Rephaites.(P) His bed was decorated with iron and was more than nine cubits long and four cubits wide.[c] It is still in Rabbah(Q) of the Ammonites.)

Division of the Land

12 Of the land that we took over at that time, I gave the Reubenites and the Gadites the territory north of Aroer(R) by the Arnon Gorge, including half the hill country of Gilead, together with its towns. 13 The rest of Gilead and also all of Bashan, the kingdom of Og, I gave to the half-tribe of Manasseh.(S) (The whole region of Argob in Bashan used to be known as a land of the Rephaites.(T) 14 Jair,(U) a descendant of Manasseh, took the whole region of Argob as far as the border of the Geshurites and the Maakathites;(V) it was named(W) after him, so that to this day Bashan is called Havvoth Jair.[d]) 15 And I gave Gilead to Makir.(X) 16 But to the Reubenites and the Gadites I gave the territory extending from Gilead down to the Arnon Gorge (the middle of the gorge being the border) and out to the Jabbok River,(Y) which is the border of the Ammonites. 17 Its western border was the Jordan in the Arabah,(Z) from Kinnereth(AA) to the Sea of the Arabah(AB) (that is, the Dead Sea(AC)), below the slopes of Pisgah.

18 I commanded you at that time: “The Lord your God has given(AD) you this land to take possession of it. But all your able-bodied men, armed for battle, must cross over ahead of the other Israelites.(AE) 19 However, your wives,(AF) your children and your livestock(AG) (I know you have much livestock) may stay in the towns I have given you, 20 until the Lord gives rest to your fellow Israelites as he has to you, and they too have taken over the land that the Lord your God is giving them across the Jordan. After that, each of you may go back to the possession I have given you.”

Moses Forbidden to Cross the Jordan

21 At that time I commanded Joshua: “You have seen with your own eyes all that the Lord your God has done to these two kings. The Lord will do the same to all the kingdoms over there where you are going. 22 Do not be afraid(AH) of them;(AI) the Lord your God himself will fight(AJ) for you.”

23 At that time I pleaded(AK) with the Lord: 24 “Sovereign Lord, you have begun to show to your servant your greatness(AL) and your strong hand. For what god(AM) is there in heaven or on earth who can do the deeds and mighty works(AN) you do?(AO) 25 Let me go over and see the good land(AP) beyond the Jordan—that fine hill country and Lebanon.(AQ)

26 But because of you the Lord was angry(AR) with me and would not listen to me. “That is enough,” the Lord said. “Do not speak to me anymore about this matter. 27 Go up to the top of Pisgah(AS) and look west and north and south and east.(AT) Look at the land with your own eyes, since you are not going to cross(AU) this Jordan.(AV) 28 But commission(AW) Joshua, and encourage(AX) and strengthen him, for he will lead this people across(AY) and will cause them to inherit the land that you will see.” 29 So we stayed in the valley near Beth Peor.(AZ)

Footnotes

  1. Deuteronomy 3:6 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them.
  2. Deuteronomy 3:6 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them.
  3. Deuteronomy 3:11 That is, about 14 feet long and 6 feet wide or about 4 meters long and 1.8 meters wide
  4. Deuteronomy 3:14 Or called the settlements of Jair